< 2 Chronicles 14 >

1 Abijah slept with his ancestors, and they buried him in the city of David. Asa, his son, became king in his place. In his days the land was quiet ten years.
Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.
2 Asa did what was good and right in the eyes of Yahweh his God,
Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
3 for he took away the foreign altars and the high places. He broke down the stone pillars and cut down the Asherah poles.
Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera.
4 He commanded Judah to seek Yahweh, the God of their ancestors, and to carry out the law and the commandments.
Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake.
5 Also he took away the high places and the incense altars from all the cities of Judah. The kingdom had rest under him.
Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake.
6 He built fortified cities in Judah, for the land was quiet, and he had no war in those years, because Yahweh had given him peace.
Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.
7 For Asa said to Judah, “Let us build these cities and make walls around them, and towers, gates, and bars; the land is still ours because we have sought Yahweh our God. We have sought him, and he has given us peace on every side.” So they built and succeeded.
Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.
8 Asa had an army that carried shields and spears; from Judah he had 300,000 men, and from Benjamin, 280,000 men who carried shields and drew bows. All of these were mighty men.
Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.
9 Zerah the Cushite came against them with an army of one million soldiers and three hundred chariots; he came to Mareshah.
Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa.
10 Then Asa went out to meet him, and they set the battle lines in order in the Valley of Zephathah at Mareshah.
Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.
11 Asa cried to Yahweh, his God, and said, “Yahweh, there is no one but you to help one who has no strength when he is facing many. Help us, Yahweh our God, for we rely on you, and in your name we have come against this vast number. Yahweh, you are our God; do not let man defeat you.”
Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”
12 So Yahweh struck the Cushites before Asa and Judah; the Cushites fled.
Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa,
13 Asa and the soldiers with him pursued them to Gerar. So many Cushites fell that they could not recover, for they were completely destroyed before Yahweh and his army. The army carried away very much plunder.
ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo.
14 The army destroyed all the villages around Gerar, for terror of Yahweh had come on the inhabitants. The army plundered all the villages, and there was much booty in them.
Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko.
15 The army also destroyed the tent settlements of the shepherding nomads; they carried away sheep in abundance, as well as camels, and then they returned to Jerusalem.
Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 Chronicles 14 >