< 1 Kings 9 >

1 After Solomon had finished building the house of Yahweh and the king's palace, and after he had accomplished all that he wanted to do,
Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene ankafuna,
2 Yahweh appeared to Solomon a second time, as he had appeared to him at Gibeon.
Yehova anamuonekera kachiwiri, monga momwe anamuonekera ku Gibiyoni.
3 Then Yahweh said to him, “I have heard your prayer and your request that you have made before me. I have set apart this house, which you have built, to myself, to put my name there forever. My eyes and my heart will be there for all time.
Yehova ananena kwa iye kuti: “Ndamva pemphero ndi pembedzero lako pa zimene wapempha pamaso panga. Ndayipatula Nyumba iyi, imene wamanga, poyikamo Dzina langa mpaka muyaya. Maso anga ndi mtima wanga zidzakhala pamenepo nthawi zonse.
4 As for you, if you walk before me as David your father walked in integrity of heart and in uprightness, obeying all that I have commanded you and keeping my statutes and my decrees,
“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika, mwangwiro ndi moona mtima monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
5 then I will establish the throne of your kingdom over Israel forever, as I promised David your father, saying, 'A descendant of yours will never fail to be on the throne of Israel.'
Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu pa Israeli mpaka muyaya, monga ndinalonjezera abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu pa mpando waufumu wa Israeli.’
6 But if you turn away, you or your children, and do not keep my commandments and my statutes that I have placed before you, and if you go and worship other gods and bow down to them,
“Koma ngati iwe kapena ana ako mudzapatuka ndi kuleka kusunga malamulo ndi mawu anga amene ndakupatsani ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
7 then will I cut off Israel from off the ground that I have given them; and this house that I have set apart to my name, I will cast it out of my sight, and Israel will become an example to be mocked and an object of ridicule among all peoples.
pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko limene ndinawapatsa ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndayipatula chifukwa cha Dzina langa. Pamenepo Aisraeli adzasanduka mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
8 This temple will become a heap of ruins, and everyone who passes by it will be shocked and will hiss. They will ask, 'Why has Yahweh done this to this land and to this house?'
Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzatsonya ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
9 Others will answer, 'Because they forsook Yahweh, their God, who had brought their ancestors out of the land of Egypt, and they laid hold of other gods and bowed down to them and worshiped them. That is why Yahweh has brought all this disaster on them.'”
Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova Mulungu wawo amene anatulutsa makolo awo mʼdziko la Igupto, ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”
10 It came about at the end of twenty years that Solomon had finished building the two buildings, the temple of Yahweh and the king's palace.
Patatha zaka makumi awiri, ndiye nthawi imene Solomoni anamanga nyumba ziwirizi: Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu,
11 Now Hiram, the king of Tyre, had furnished Solomon with cedar and cypress trees, and with gold—all that Solomon desired—so King Solomon gave Hiram twenty cities in the land of Galilee.
Mfumu Solomoni anapereka mizinda makumi awiri ya ku Galileya kwa Hiramu mfumu ya ku Turo chifukwa Hiramu nʼkuti atapereka mitengo yonse ya mkungudza ndi ya payini ndiponso golide yense zimene Solomoni ankazifuna.
12 Hiram came out from Tyre to see the cities that Solomon had given him, but they did not please him.
Koma Hiramu atabwera kuchokera ku Turo kudzaona mizinda imene Solomoni anamupatsa, sanasangalatsidwe nayo mizindayo.
13 So Hiram said, “What cities are these which you have given me, my brother?” Hiram called them the Land of Kabul, which they are still called today.
Iye anafunsa kuti, “Mʼbale wanga, kodi iyi nʼkukhala mizinda yondipatsa?” Ndipo iye anayitcha mizindayo Dziko la Kabuli, dzina lomwe amatchedwa mpaka lero lino.
14 Hiram had sent to the king 120 talents of gold.
Koma Hiramu anali atatumiza kwa mfumu golide oposa makilogalamu 4,000.
15 This is the account of the forced labor which King Solomon imposed to build the temple of Yahweh and his own palace, the Millo, the wall of Jerusalem, and Hazor, and Megiddo, and Gezer.
Izi ndi zimene anachita Mfumu Solomoni: Analamula anthu kuti agwire ntchito yathangata pomanga Nyumba ya Yehova, nyumba yake, malo achitetezo a Milo, mpanda wa Yerusalemu, Hazori, Megido ndi Gezeri.
16 Pharaoh king of Egypt had gone up and taken Gezer. He burned it and killed the Canaanites in the city. Then Pharaoh gave the city to his daughter, Solomon's wife, as a wedding gift.
(Farao mfumu ya ku Igupto inali itathira nkhondo ndi kulanda Gezeri. Iye anatentha mzindawo. Anapha Akanaani amene ankakhala mʼmenemo ndipo kenaka anawupereka ngati mphatso yaukwati kwa mwana wake wamkazi amene anakwatiwa ndi Solomoni.
17 So Solomon rebuilt Gezer and Beth Horon the Lower,
Ndipo Solomoni anamanganso Gezeri.) Iye anamanga Beti-Horoni Wakumunsi,
18 Baalath and Tamar in the wilderness in the land of Judah,
Baalati ndi Tadimori ku chipululu, mʼdziko lake lomwelo,
19 and all the store cities that he possessed, and the cities for his chariots and the cities for his horsemen, and whatever he wished to build for his pleasure in Jerusalem, in Lebanon, and in all the lands under his rule.
pamodzinso ndi mizinda yake yosungira chuma ndiponso mizinda yosungiramo magaleta ndi akavalo ake. Anamanganso chilichonse chimene anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.
20 As for all the people who were left of the Amorites, the Hittites, the Perizzites, the Hivites, and the Jebusites, who were not of the people of Israel,
Panali anthu amene anatsala pakati pa mitundu ya Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi (anthu awa sanali Aisraeli).
21 their descendants who were left after them in the land, whom the people of Israel were not able to totally destroy—Solomon made them into forced laborers, which they are to this day.
Zimenezi ndiye zinali zidzukulu zawo zotsalira mʼdzikoli, anthu amene Aisraeli sanathe kuwawononga kotheratu. Solomoni anawatenga ndi kukhala akapolo ake ogwira ntchito yathangata, monga zilili mpaka lero lino.
22 However, Solomon made no forced laborers of the people of Israel. Instead, they became his soldiers and his servants, his officials, and his officers and commanders of his chariot forces and his horsemen.
Koma Solomoni sanagwiritse ntchito ya ukapolo Mwisraeli aliyense; iwo anali anthu ake ankhondo, nduna zake, atsogoleri a ankhondo, akapitawo ake, olamulira magaleta ndi oyendetsa magaleta ake.
23 These were also the chief officers managing the supervisors who were over Solomon's works, 550 of them, who supervised the people who did the work.
Amenewa ndiwo anali akuluakulu oyangʼanira ntchito za Solomoni. Anthu okwana 550 ndiwo ankayangʼanira anthu amene ankagwira ntchitowo.
24 Pharaoh's daughter moved from the city of David to the house that Solomon had built for her. Later, Solomon built the Millo.
Mwana wamkazi wa Farao atachoka mu Mzinda wa Davide, kupita ku nyumba ya mfumu imene Solomoni anamumangira, Solomoni anamanga malo achitetezo a Milo.
25 Three times each year Solomon offered burnt offerings and peace offerings on the altar that he built for Yahweh, burning incense with them on the altar that was before Yahweh. So he completed the temple and was now using it.
Katatu pa chaka Solomoni ankapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe limene anamangira Yehova ndiponso ankafukiza lubani pamaso pa Yehova. Potero ankakwaniritsa zoyenera kuchitika mu Nyumba ya Yehova.
26 King Solomon built a fleet of ships in Ezion Geber, which is near Elath on the shore of the Red Sea, in the land of Edom.
Mfumu Solomoni anapanganso sitima zapamadzi ku Ezioni Geberi, malo amene ali pafupi ndi Eloti ku Edomu, mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
27 Hiram sent servants to Solomon's fleet, sailors who were familiar with the sea, with Solomon's own servants.
Ndipo Hiramu anatumiza anthu ake oyendetsa sitima zapamadzi amene ankadziwa za pa nyanja kuti aziyendetsa pamodzi ndi anthu a Solomoni.
28 They went to Ophir with servants of Solomon. From there they brought back 420 talents of gold for King Solomon.
Iwo anapita ku Ofiri ndipo anakatenga golide okwana makilogalamu 14,000, amene anamupereka kwa Mfumu Solomoni.

< 1 Kings 9 >