< Genesis 22 >

1 After these dedes God dyd proue Abraham and sayde vnto him: Abraham. And he answered: here am I.
Nthawi ina zitatha izi, Mulungu anamuyesa Abrahamu. Iye anati, “Abrahamu!” Ndipo iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
2 And he sayde: take thy only sonne Isaac whome thou louest and get the vnto the lande of Moria and sacrifyce him there for a sacrifyce vpon one of the mountayns which I will shewe the
Ndipo Mulungu anati, “Tenga Isake, mwana wako yekhayo amene umamukonda ndi kupita naye ku dziko la Moriya. Ukamupereke iye ngati nsembe yopsereza pa limodzi la mapiri a kumeneko limene ndidzakuwuza.”
3 Than Abraham rose vp early in the mornynge and sadled his asse and toke two of his meyny wyth him and Isaac his sonne: ad clove wod for the sacrifyce and rose vp and gott him to the place which God had appoynted him.
Abrahamu anadzuka mmamawa wake namangirira chokhalira pa bulu. Atadula nkhuni zokwanira zowotchera nsembe yopsereza, Abrahamu, antchito ake awiri pamodzi ndi Isake ananyamuka kupita kumalo kumene Mulungu anamuwuza Abrahamu.
4 The thirde daye Abraham lyfte vp his eyes and sawe the place a farr of
Pa tsiku lachitatu, Abrahamu anakweza maso ake ndipo anaona malowo chapatali.
5 and sayde vnto his yong men: byde here with the asse. I and the lad will goo yonder and worshippe and come agayne vnto you.
Ndipo Abrahamu anati kwa antchito ake aja, “Bakhalani pano ndi buluyu. Ine ndi mnyamatayu tipita uko kukapemphera, koma tibweranso.”
6 And Abraham toke the wodd of the sacrifyce and layde it vpon Isaac his sonne and toke fyre in his hande and a knyfe. And they went both of them together.
Abrahamu anatenga nkhuni za nsembe yopsereza zija namusenzetsa mwana wake Isake, ndipo iye mwini anatenga moto ndi mpeni. Pamene awiriwo amayendera pamodzi,
7 Than spake Isaac vnto Abraham his father and sayde: My father? And he answered here am I my sonne. And he sayde: Se here is fyre and wodd but where is the shepe for sacrifyce?
Isake anati kwa abambo ake Abrahamu, “Abambo?” Abrahamu anayankha, “Ee mwana wanga.” Isake anafunsa, “Moto ndi nkhuni zilipo, koma nanga mwana wankhosa wa nsembe yopsereza ali kuti?”
8 And Abraham sayde: my sonne God wyll prouyde him a shepe for sacrifyce. So went they both together.
Abrahamu anayankha, “Mwana wanga, Mulungu adzipezera yekha mwana wankhosa wa nsembe yopsereza.” Ndipo awiriwo anapitiriza ulendo.
9 And when they came vnto the place which God shewed him Abraha made an aulter there and dressed the wodd ad bownde Isaac his sonne and layde him on the aulter aboue apon the wodd.
Atafika pamalo pamene Mulungu anamuwuza paja, Abrahamu anamangapo guwa lansembe nayika nkhuni pamwamba pa guwapo. Kenaka anamumanga mwana wake Isake namugoneka paguwapo, pamwamba pa nkhuni paja.
10 And Abraham stretched forth his hande and toke the knyfe to haue kylled his sonne.
Kenaka Abrahamu anatambasula dzanja lake natenga mpeni kuti aphe mwana wake.
11 Than the angell of the LORde called vnto him from heauen saynge: Abraham Abraham. And he answered: here am I.
Koma mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba nati, “Abrahamu! Abrahamu!” Iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
12 And he sayde: laye not thy handes apon the childe nether do any thinge at all vnto him for now I knowe that thou fearest God in yt thou hast not kepte thine only sonne fro me.
Mngeloyo anati, “Usatambasulire mwanayo dzanja lako kuti umuphe, pakuti tsopano ndadziwa kuti iwe umaopa Mulungu. Iwe sunandimane mwana wako mmodzi yekhayo.”
13 And Abraham lyfted vp his eyes and loked aboute: and beholde there was a ram caught by the hornes in a thykette. And he went and toke the ram and offred him vp for a sacrifyce in the steade of his sonne
Abrahamu anatukula maso ake ndipo anaona nkhosa yamphongo itakoledwa ndi nyanga zake mu ziyangoyango. Iye anapita nakatenga nkhosa ija ndikuyipha ngati nsembe yopsereza mʼmalo mwa mwana wake.
14 And Abraham called the name of the place the LORde will see: wherfore it is a come saynge this daye: in the mounte will the LORde be sene.
Choncho Abrahamu anatcha malo amenewa kuti Yehova-Yire (Wopereka). Ndipo mpaka lero amatchula malowo kuti ndi “Pa phiri la Yehova wopereka.”
15 And the Angell of the LORde cryed vnto Abraham from heaven the seconde tyme
Mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba kachiwiri
16 saynge: by my selfe haue I sworne (sayth the LORde) because thou hast done this thinge and hast not spared thy only sonne
ndipo anati, “Ndikulumbira mwa Ine ndekha kuti popeza wachita zimenezi, wosandikaniza mwana wako mmodzi yekhayu,
17 that I will blesse th and multiplye thy seed as the starres of heaven and as the sonde vpo the seesyde. And thy seed shall possesse the gates of hys enymies.
ndidzakudalitsa ndithu ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati nyenyezi zamlengalenga komanso ngati mchenga wa mʼmphepete mwa nyanja. Zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo,
18 And in thy seed shall all the nations of the earth be blessed because thou hast obeyed my voyce.
ndipo kudzera mwa chidzukulu chako, mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi idzadalitsika, chifukwa iwe wandimvera.”
19 So turned Abraham agayne vnto his yonge men and they rose vp and wet to gether to Berseba. And Abraham dwelt at Berseba
Kenaka Abrahamu anabwerera kumene anasiya antchito ake kuja nanyamukira nawo pamodzi kupita ku Beeriseba. Ndipo Abrahamu anakhala ku Beeriseba.
20 And it chaused after these thiges that one tolde Abraham saynge: Beholde Milcha she hath also borne childern vnto thy brother Nachor:
Patapita nthawi, Abrahamu anamva kuti, “Milika nayenso anaberekera Nahori, mʼbale wake ana.
21 Hus his eldest sonne and Bus his brother and Lemuell the father of the Sinans
Woyamba anali Huzi ndipo kenaka mʼbale wake Buzi. Anaberekanso Kemueli, amene anali abambo ake a Aramu.
22 and Cesed and Haso and Pildas and Iedlaph and Bethuel.
Ana ena ndi Kesede Hazo, Pilidasi, Yidilafi ndi Betueli.”
23 And Bethuel begat Rebecca. These. viij. dyd Milcha bere to Nachor Abrahams brother
Betueli anabereka Rebeka. Milika anaberekera Nahori, mʼbale wake wa Abrahamu, ana aamuna asanu ndi atatu amenewa.
24 And his concubyne called Rheuma she bare also Tebah Gaham Thahas and Maacha.
Mkazi wake wachiwiri, dzina lake Reuma, anamubaliranso Nahori ana awa: Teba, Gahamu, Tahasi ndi Maaka.

< Genesis 22 >