< Song of Solomon 4 >
1 My darling, you are beautiful, you are very beautiful! Underneath your veil, your eyes are [as gentle as] [MET] doves. Your [long black] hair [moves from side to side] like [SIM] a flock of [black] goats moving down the slopes of Gilead Mountain.
Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga! Ndithudi, ndiwe wokongola! Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
2 Your teeth are [very white] like [SIM] a flock of sheep [whose wool] has [just] been (shorn/cut off) and that have come up from being washed [in a stream]. You have all of your teeth; none of them is missing.
Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene, zochokera kozisambitsa kumene. Iliyonse ili ndi ana amapasa; palibe imene ili yokha.
3 Your lips are like [SIM] a scarlet ribbon, and your mouth is lovely. Beneath your veil, your [round, rosy/red] cheeks are like [SIM] the halves of a pomegranate.
Milomo yako ili ngati mbota yofiira; pakamwa pako ndi pokongola kwambiri. Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
4 Your [long] neck is [beautiful] like [SIM] the tower of [King] David that was built using layers/rows of stone. [The ornaments on your necklaces are like] 1,000 [HYP] shields that are hanging [on the walls of a tower]; each one belongs to a warrior.
Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide, yomangidwa bwino ndi yosalala; pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000, zishango zonsezo za anthu ankhondo.
5 Your breasts are [as beautiful] [SIM] as two (fawns/young gazelles) that eat [grass] among lilies.
Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala, ngati ana amapasa a nswala amene akudya pakati pa maluwa okongola.
6 Until dawn [tomorrow morning] and the nighttime shadows/darkness disappear, I will [lie close to your breasts] that are [like] [MET] hills that are covered with incense [DOU].
Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira ndipo mithunzi ikayamba kuthawa, ndidzapita ku phiri la mure ndi ku chitunda cha lubani.
7 My darling, you are completely beautiful; your body is perfectly [formed]!
Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga; palibe chilema pa iwe.
8 My bride, [it is as though you are in] [MET] Lebanon [far away, where I cannot reach you]; come back to me. [It is as though you are inaccessible] [MET] on the top of Hermon Mountain or the nearby peaks. Come from where the lions have their dens and where the leopards live on the mountains.
Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga, tiye tichoke ku Lebanoni, utsikepo pa msonga ya Amana, kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni, kuchoka ku mapanga a mikango ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
9 My bride [DOU], you who are dearer to me than my sister, you have captured my affection [IDM] by only once quickly looking at me, and by one [strand of] jewels in your necklace.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima, iwe wanditenga mtima ndi kapenyedwe ka maso ako, ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
10 My bride, your love for me is delightful! It more delightful than wine! And the fragrance of your perfume is more pleasing than any spice!
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa! Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo, ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
11 Being kissed by you is [as enjoyable as eating] [MTY] honey; your kisses are as sweet as milk [mixed with] honey. The aroma of your clothes is like [SIM] the aroma of [cedar trees in] Lebanon.
Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi; pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi. Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
12 My bride, [you who are dearer to me than] [MET] my sister, you are [like] [MET] a garden that is locked [in order that other men cannot enter it]; [you are like] [MET] a spring or a fountain that is covered [in order that others may not drink from it].
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa; ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
13 You are [like] [MET] an orchard of pomegranate trees full of delicious fruit, and plenty of [plants that produce] henna and nard [spices],
Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza; muli zipatso zokoma kwambiri, muli hena ndi nadi,
14 and saffron and calamus and cinnamon and many other kinds of incense, and myrrh and aloes and many [other] fine spices.
nadi ndi safiro, kalamusi ndi sinamoni, komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino. Mulinso mure ndi aloe ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
15 [You are like] [MET] a fountain in a garden, [like] [MET] a spring of clear water that flows [down] from [the mountains of] Lebanon.
Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda, chitsime cha madzi oyenda, mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.
16 [I want] the north wind and the south wind to come, and blow on my garden, [in order that] the fragrance [of the spices will] spread through the air. [Similarly], I want the one who loves me to come and enjoy [cuddling up to me] [like] [MET, EUP] someone comes into a garden and enjoys eating the fruit [that grows there].
Dzuka, iwe mphepo yakumpoto, ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera! Uzira pa munda wanga, kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse. Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.