< Romans 1 >
1 [I], Paul, who serve Christ Jesus, [am writing this letter]. God chose me to be an apostle, and I was appointed by him {he appointed me} in order that [I should proclaim] (the good message/the gospel) that [comes from him].
Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
2 Long before [Jesus came to earth, God] promised [that he would reveal] this good message by means of what his prophets [wrote] in the sacred Scriptures.
umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
3 This good message is [about the one whom we know as] his Son. As to his Son’s physical/human nature, he was born a descendant of [King] David.
Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
4 As to his divine nature, it was shown {[God] showed} powerfully that he is (God’s own Son/the man who is also God). [God] showed this by his Holy Spirit causing him to become alive again after he died. He is Jesus Christ our Lord.
Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
5 He is the one who appointed me, who did not deserve it, [to be] an apostle. He did that in order that [many] among the non-Jews would honor [him] and would obey him as a result of their believing [my message about him].
ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
6 You [believers] who are living in Rome [city] are included among those whom God has chosen to belong to Jesus Christ.
Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
7 [I am writing this letter] to all of [you in Rome] whom God loves and whom he has chosen [to become his] people. [I pray that] God our Father and Jesus Christ our Lord will [continue to] act kindly toward you and [will continue to] cause you to have [inner] peace.
Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
8 As I begin [this letter], I thank my God for all you [believers in Rome]. It is because of [what] Jesus Christ [has done for us that] I [am able to do that]. I thank him because your trusting [in Jesus Christ] is something that people all over [the Roman Empire] [HYP] are talking about.
Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
9 God, whom I devotedly serve as I [proclaim to people] the gospel concerning his Son, knows that I tell the truth when I say that I always mention you whenever [DOU] I pray [to God] [HYP].
Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
10 I especially ask God that if he desires [me to visit you], somehow at last I shall be able to do so.
Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
11 [I pray this] because I long to visit you to help you spiritually, in order that you will become stronger [spiritually].
Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
12 I long to visit you in order that you and I might encourage each other [by means of our sharing with each other] how each of us trusts [in Jesus].
ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
13 My fellow believers, many times I planned to visit you. I certainly want you to know [LIT] that. [But I have not been able to come to you because] I have been hindered {[things] have always prevented me} until the present time. I have wanted to come in order that I might help you to mature spiritually [IDM], as [I have helped people to mature spiritually] in many other non-Jewish groups [HYP].
Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
14 I feel obliged [to proclaim the gospel to all non-Jewish people], specifically to [people who know] the Greek [language and culture] and to those who do not know it, to people who are educated and to those who are uneducated.
Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
15 So what I have eagerly desired is that I might proclaim this good message to you who are living in Rome also.
Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
16 [That leads me to say that] I very confidently proclaim [LIT] the good message [about what Christ has done], because this good message is the powerful [means] that God [uses] to save [from the guilt of their sins] all people who trust [in what Christ has done for them]. Specifically, God first has saved the Jews [who believe the good message], and then he has saved non-Jews.
Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
17 By means of this good message God reveals how he erases the record of people’s sins (OR, declares people no longer guilty for having sinned); and his doing this is entirely because [IDM] they trust [in Christ. This is confirmed] by what [a prophet long ago] wrote [that God said], “Those (whose record of sin [I] have erased/whom [I] have declared no longer guilty for sin) because they trust [in me] will live [forever].”
Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
18 From [where God rules in] heaven he is making it clear to all [non-Jewish] people who show no respect for God and who do wicked things, that he is angry with them [and that they deserve to be punished] {[that he would punish them]} [MTY]. By means of [their behaving] wickedly, they keep other people [from believing what they know] to be true [about God].
Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
19 [Everyone] can clearly know what God [is like], because God himself has revealed to everyone [what he is like].
Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
20 [People] cannot see what God is like. But ever since he created the world, by means of what he created he has clearly revealed what he is like. He has made clear to everyone that he has always been able to do very powerful things. [Therefore, we should recognize that] God is powerful, [completely different from all that he created]. So no one has a basis for saying, [“We never knew about God].” (aïdios )
Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios )
21 Although [the non-Jews] knew what God [is like], they did not honor him as God, nor did they thank [him for what he had done]. But instead, they began to think foolish [things about him], and they became unable to understand [MET] [what he wanted them to know].
Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
22 Although they claimed that they were wise, they became foolish,
Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
23 and they refused to [admit that] God is glorious and will never die. Instead, they made and worshipped idols [that resembled people who] will some day die, and [then they made other idols that resembled] birds and four-footed animals, and [finally] they made idols that resembled reptiles.
Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
24 So God allowed [the non-Jews] do immoral sexual things that they [SYN] strongly desired, things [that their desires were compelling them to do]. As a result, they [began to] dishonor each other’s bodies [by their sexual actions].
Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
25 Also, they [chose to worship] false [gods] instead (of admitting/of choosing to believe) what is true [about] God. They worshipped and served things [that God] created instead of [worshipping and serving God himself], the one who created [everything. They did this even though] he [deserves that those he created] would forever praise him. Amen!/May it be so! (aiōn )
Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
26 So, God allowed [the non-Jews to do] shameful [sexual] things that they [strongly] desired. As a result, many women did not have natural sexual relations [with their husbands] [EUP]. Instead, they were doing sexual actions with other women [EUP].
Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
27 Similarly, [many] men stopped having/did not have natural sexual relations with women [EUP]. Instead, they strongly desired to have sexual relations with other men. They committed [homosexual] acts with other men, acts that were shameful. As a result, [God has] punished them [by sicknesses] in their bodies, which is what they deserve [because] they [thought] wrongly [that God would not punish them for doing that].
Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
28 Furthermore, because they decided that it was not [worthwhile] to know God, he allowed their own worthless thoughts [to completely control them]. As a result, they began doing [evil] things that [God says that people] should not do.
Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
29 They strongly desire to do all [kinds of] unrighteous [things]. They strongly desire to do all [kinds of] evil things [to others]. They strongly desire to possess things that [belong to others]. They strongly desire to harm [others] in various ways. [Many non-Jews] are constantly envying [other people. Many] constantly desire to murder [people. Many] constantly desire to cause strife [between people. Many] constantly desire to deceive [others. Many] constantly desire to speak hatefully [about others] (OR, [to speak harmful things about others, things that are not true]). [Many] gossip [about others].
Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
30 [Many] slander [others. Many] act especially hatefully toward God. [Many] speak or act in an insulting way [toward others. Many] treat others contemptuously. [Many] boast [about themselves to others. Many] invent new ways to do evil things. [Many non-Jewish children] disobey their parents.
osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
31 [Many non-Jews] act in other morally foolish ways. [Many] do not do what they promised [others that they would do. Many] do not [even] love [their own family members. And many] do not act mercifully [toward other people].
alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
32 Although they know that God has declared that those who do such things deserve to be killed, they not only habitually do these [kinds of evil] things, but they also approve of others who habitually do them.
Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.