< Revelation 6 >

1 I saw that [Jesus, the one who is like a] lamb, opened the first of the seven seals [of the scroll]. Then I heard one of the four living [creatures] say in a voice [as loud] as [SIM] thunder, “Come!”
Ndinaona pamene Mwana Wankhosa anatsekula chomatira choyamba cha zomatira zisanu ndi ziwiri zija. Ndipo ndinamva chimodzi mwa zamoyo zinayi zija chikunena liwu lomveka ngati bingu kuti, “Bwera!”
2 Then I saw a white horse [come out]. The one who sat on it had a bow [and arrows]. [God] gave him a crown [to show that he was the king]. Then the one who conquers [people] went out to continue to conquer [people].
Nditayangʼana patsogolo pake ndinaona kavalo woyera! Wokwerapo wake anali ndi uta ndipo anapatsidwa chipewa chaufumu, ndipo anatuluka kupita kukagonjetsa anthu ena.
3 When the [one who was like a] lamb opened the second seal, I heard the second living [creature] say, “Come!”
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachiwiri, ndinamva chamoyo chachiwiri chija chikuti, “Bwera!”
4 Then a red horse came out. The one sitting on it was allowed {[God] allowed the one sitting on it} to cause [people] to no longer [live] peacefully, but instead to be killing each other. [For this purpose] he was given {[God’s agent] gave to him} a large sword.
Pamenepo kavalo wina wofiira anatulukira. Wokwerapo wake anapatsidwa mphamvu yochotsa mtendere pa dziko lapansi ndi kuchititsa anthu kuti aziphana wina ndi mnzake. Iyeyu anapatsidwa lupanga lalikulu.
5 When [the one who is like a] lamb opened the third seal, I heard the third living [creature] say, “Come!” This time, I saw a black horse [come out]. The one who sat on it had a pair of scales in his hand.
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachitatu, ndinamva chamoyo chachitatu chikuti, “Bwera!” Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wakuda! Wokwerapo wake anali ndi masikelo awiri mʼmanja mwake.
6 I heard a voice [that sounded] like [it was coming from] among the four living [creatures]. It was saying ([to the horseman/to the man who was sitting on the black horse]), “A quart of wheat [will cost so much that] a man must work a whole day to earn enough money to buy it, and three quarts of barley will sell for the same price. But do not cut off [the supply of] olive oil or the wine [MTY]!”
Ndinamva ngati liwu kuchokera pakati pa zamoyo zinayi zija likuti, “Kilogalamu imodzi ya tirigu mtengo ndi malipiro a tsiku limodzi ndipo makilogalamu atatu a barele mtengo wake ndi malipiro a tsiku limodzi koma usawononge mafuta ndi vinyo!”
7 When the [one who is like a] lamb opened the fourth seal, I heard the fourth living [creature] say, “Come!”
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachinayi, ndinamva chamoyo chachinayi chija chikunena kuti, “Bwera!”
8 This time I saw a pale horse [come out]. The one who sat on it is named ‘[The one who causes] death [PRS]’, and [the one that is named ‘The place where dead people go’] accompanied him. [God] gave them authority over one quarter of the people on earth to incite them to kill each other with weapons [SYN], and also authority to kill them (by [causing them to] starve, by [their causing them to become] sick from epidemics, and by [their causing them to be attacked by] wild animals. (Hadēs g86)
Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wotuwa! Wokwerapo wake dzina lake linali Imfa ndipo Hade inali kumutsatira pambuyo pake. Anapatsidwa ulamuliro pa gawo limodzi la magawo anayi a dziko lapansi kuti aphe ndi lupanga, njala, mliri, ndi zirombo zakuthengo za mʼdziko lapansi. (Hadēs g86)
9 When the [one who is like a] lamb opened the fifth seal, I saw under (OR, at the base of) the altar [in heaven] the souls of [God’s servants] who had been killed {whom [people had] killed} because of [their believing] God’s message, and because they told others [the message about Jesus].
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachisanu, ndinaona kunsi kwa guwa lansembe kunali mizimu ya anthu amene anaphedwa chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi chifukwa chochitira umboni.
10 They spoke loudly [to God] saying, “Sovereign/Almighty Lord, you are holy and faithful. How long [will it be] before you judge [and punish] the people on earth who murdered [us(exc)]?”
Iwo anafuwula kuti, “Mudzawaleka mpaka liti, Inu Ambuye wamkulu, woyera ndi woona, osawaweruza anthu okhala mʼdziko lapansi ndi kulipsira magazi athu?”
11 [God] gave to each of them a long white robe, and [he] told them to rest a little longer until [people] killed all the believers who served [the Lord] with them. They were believers whom [God wanted to die in just the same way] that these others had been killed.
Pamenepo aliyense wa anthuwo anapatsidwa mwinjiro woyera ndipo anawuzidwa kuti adikire pangʼono kufikira chiwerengero cha anzawo ndi abale awo amene anayeneranso kuphedwa ngati iwo, chitakwanira.
12 I saw that when [the one who is like a] lamb opened the sixth seal, the earth shook violently. The sun became as black as cloth made (of [black] wool/of pitch). The whole moon became [red] [SIM] like blood.
Ndinayangʼanitsitsa pamene ankatsekula chomatira chachisanu ndi chimodzi. Ndipo panachitika chivomerezi champhamvu. Dzuwa linada ngati chiguduli chopanga ndi bweya wambuzi wakuda. Mwezi wonse unafiira ngati magazi,
13 The stars fell to the earth [in great numbers], just [SIM] like immature figs fall when a fig tree is shaken by a strong wind {when a strong wind shakes a fig tree}.
ndipo nyenyezi zakuthambo zinagwa pa dziko lapansi ngati muja zimagwera nkhuyu zotsalira mu mtengo mphepo yamphamvu ikawomba.
14 The sky split open and [rolled up on either side] just [SIM] like an [old] scroll rolls up [when it is split in two]. Every mountain and island moved out of its place.
Thambo linachoka ngati amayalulira mphasa ndipo phiri lililonse ndi chilumba chilichonse zinachotsedwa pa malo pake.
15 [As a result, all the rebellious people] of the earth, [including] kings, high-ranking people, generals, the rich people, the powerful people, along with everyone [else], both slave and free, hid themselves in caves and between the mountain rocks.
Kenaka, mafumu a pa dziko lapansi, ana a mafumu, atsogoleri a ankhondo, olemera, amphamvu, kapolo aliyense, ndi mfulu aliyense anakabisala kumapanga ndi pakati pa matanthwe a ku mapiri.
16 They shouted to the mountains and to the rocks, “Fall on us [(exc)] and hide us [(exc)] in order that the one who sits upon the throne will not be able to see us [(exc)] [MTY], and [in order that] the [one who is like a] lamb will not be able to punish [MTY] us [(exc)].
Iwo anafuwulira mapiri ndi matanthwe kuti, “Tigwereni ndi kutivundikira kuti asatione wokhala pa mpando waufumuyo ndi kupulumuka ku mkwiyo wa Mwana Wankhosa!
17 This is the terrible day on which they will punish [MTY] us [(exc)], and [when that happens], no one will be able to survive! [RHQ]”
Pakuti tsiku lalikulu la mkwiyo wawo lafika ndipo ndi ndani angathe kulimbapo?”

< Revelation 6 >