< Psalms 94 >

1 Yahweh, you are able to get revenge [on your enemies]. [So] show them that you are going to punish them!
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 You are the one who judges all [people on] the earth; [so] arise, and give/punish the proud [leaders of our] people like they deserve.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Yahweh, how long will those wicked [people] be glad/happy? It is not right that [RHQ] they continue being glad!
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 They do evil things, and they boast about doing them; how long will they [be allowed to] continue doing that?
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Yahweh, [it is as though] those wicked people crush [us], your people; they (oppress/treat cruelly) those who belong to you [DOU].
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 They murder widows and orphans and people from other countries who [think it is safe to] live in our land.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 Those wicked people say, “Yahweh does not see anything; [so] the God whom those Israelis [worship] does not see [the evil things that we do].”
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 You evil people [who rule Israel], you are foolish and stupid; when will you become wise [RHQ]?
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 God made our ears; so [do you think that] he cannot hear [what you say] [RHQ]? He created our eyes; so do you think that he cannot see [the evil things that you do] [RHQ]?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 He also scolds [the leaders of other] nations; so do you think that he will not punish [you] [RHQ]? He is the one who knows everything; [so why do you think that he does not know what you do] [RHQ]?
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 Yahweh knows [everything] that people are thinking; he knows that what they think ([is useless/vanishes as quickly as]) smoke [MET].
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Yahweh, you are pleased with people who [want you to] discipline/correct them, those who [want you to] teach them your laws.
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 When those people have had troubles, you cause those troubles to cease, and some day [it will be as though] you will dig pits for wicked people, and they will fall into those pits [and die].
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 Yahweh will not abandon his people; he will not desert like that those who belong to him [DOU].
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 [Some day] judges will decide matters fairly for people, and all honest/righteous people will be pleased about that.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 But when wicked [people] ([oppressed me/treated me cruelly]), (who defended me?/no one defended me.) [RHQ] No one stood up to testify for me against those evil people [RHQ].
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 If Yahweh had not helped me [at that time], [I would have been executed], [and] my soul/spirit would have gone to the place where [dead people] say nothing.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 I said/thought [to myself], “I am about to die,” but Yahweh, you held me up by faithfully loving me.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Whenever I am very worried, you comfort/encourage me and cause me to be happy.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 You have nothing to do with wicked judges, who establish laws that allow people to do what is not legal.
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 They plan to get rid of righteous [people], and they declare that (innocent people/people who have not done what is wrong) must be executed.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 But Yahweh (has become [like] my fortress/protects me) [MET]; my God is [like a huge] rock under which I am protected/safe [MET].
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 He will punish those wicked leaders in return for the wicked things that they have done, and will get rid of them for the sins that they have committed; [yes], Yahweh our God will (wipe them out/destroy them completely).
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Psalms 94 >