< Psalms 90 >

1 Lord, you have always (been [like] a home for us/protected us) [MET].
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
2 Before you created the mountains, before you formed the earth and everything that is in it, you were eternally God, and you will be God forever.
Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
3 [When people die], you cause their corpses to become soil again; you change their corpses to become dirt like [the first man] was created from.
Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
4 When you (consider/think about) time, 1,000 years are [as short as] [SIM] one day which passes; [you consider that] [HYP] they are as short as a few hours in the night.
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
5 You cause people suddenly to die [MET]; they [live only a short time], like a dream lasts only a short time. They are like grass/weeds [SIM] that grow up.
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
6 In the morning [DOU] the grass sprouts and grows well, but in the evening it dries up and (completely withers/dies).
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
7 [Similarly], [because of the sins that we have committed], you become angry with us; you terrify us and then you destroy us.
Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
8 [It is as though] you place our sins in front of you, you spread out even our secret sins where you can see them.
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
9 Because you are angry with us, you cause our lives to end; the years that we live pass as quickly as a sigh does.
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
10 People live for only 70 years; but if they are strong, some of them live for 80 years. But even during good years we have much pain and troubles; our lives soon end, and we die [EUP].
Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
11 No one [RHQ] has fully experienced the powerful things you can do to them when you are angry with them, and people are not afraid that you will greatly punish them because of your being angry with them.
Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
12 So teach/help us to realize that we live for only a short time in order that we may [use our time] wisely.
Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
13 Yahweh, how long [will you be angry with us]? Pity us who serve you.
Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
14 Each morning show us that your faithfully loving us is enough for us in order that we may shout joyfully and be happy for the rest of our lives.
Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 Cause us to now be as happy for as many years as you (afflicted us/caused us to be sad) and we experienced troubles.
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Enable us to see the [great] things that you do and enable our descendants to [also] see your glorious power.
Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
17 Lord, our God, give us your blessings and enable us to be successful; yes, cause us to be successful in [everything] that we do [DOU]!
Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

< Psalms 90 >