< Psalms 85 >
1 Yahweh, you have been kind to [us people who live in] this land; you have enabled [us] Israeli people to become prosperous again.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 You forgave [us], your people, for the sins that we had committed; you pardoned [us] for all our sins [DOU].
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 You stopped being angry [with us] and turned away from severely punishing [us].
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Now, God, the one who saves/rescues us, (restore us/make us prosperous again) and stop being angry with us!
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 (Will you continue to be angry with us forever?/Please do not continue to be angry with us forever.) [DOU, RHQ]
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Please enable us [RHQ] to prosper again in order that [we], your people, will rejoice about what you [have done for us].
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Yahweh, by rescuing us [from our troubles/difficulties], show us that you faithfully love us.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 I want to listen to what Yahweh [our] God says, because he promises/says that he will enable [us], his people, to live peacefully, if we do not return to doing foolish things.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 He is surely ready to save/rescue those who revere him, in order that [his] glory/splendor will be seen in our land.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 [When that happens], he will both faithfully love us and faithfully [do for us what he promised to do] [PRS]; and we will act/behave righteously, and he will give us peace, which will be like a kiss that he gives us.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Here on earth, we will (be loyal to/continually believe in) God, and from heaven, God will act justly/fairly [toward us].
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Yes, Yahweh will do good things [for us], and there will be great harvests in our land.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 [Yahweh always acts] righteously [PRS, MET]; he acts righteously wherever he goes.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.