< Psalms 78 >

1 My friends, listen to what I am going to teach you; pay careful attention [IDM] to what I say.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 I am going to give you some sayings that wise people have said. They will be sayings about things that happened long ago, things that were difficult to understand [MET],
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 things that we have heard and known previously, things that our parents and grandparents told us.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 We will tell these things to our children [LIT], and we will also tell to our grandchildren [about] Yahweh’s power and the glorious/great things that he has done.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 He gave laws and commandments to the Israeli people, [those who are the descendants of] Jacob [DOU], and he told our ancestors to teach them to their children
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 in order that their children would [also] know them and then they would teach them to their children.
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 In that way, they also would trust in God, and not forget the things that he has done; instead, they would obey his commandments.
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 They would not be like their ancestors, who were very stubborn and kept rebelling [against God]; they did not continue firmly trusting in God, and they did not worship only him.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 [The soldiers of] the tribe of Ephraim had bows [and arrows] but they ran away [from their enemies] on the day that they fought a battle with their enemies.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 They did not do what they had agreed with God that they would do; they refused to obey his laws.
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 They forgot what he had done; they forgot about the miracles that they had seen him perform.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 While our ancestors were watching, God performed miracles in the area around Zoan [city] in Egypt.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 [Then] he caused the [Red] Sea to divide, causing the water [on each side] to pile up like a wall, with the result that [our ancestors] walked through it [on dry ground].
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 He led them by a [bright] cloud during the day and by a fiery light during the night.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 He split rocks open in the desert, giving to our ancestors plenty of water from deep inside the earth.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 He caused a stream of water to flow from the rock; the water flowed like a river [DOU].
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 But [our ancestors] continued to sin against God; in the desert they rebelled against the one who is greater than any other god.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 By demanding that God give them the food that they desired, they tried to find out if he would always do what they requested him to do.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 They insulted God by saying, “We don’t think he can supply food for us [here] in this desert!
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 [It is true that] he struck the rock, with the result that water gushed/flowed out, [but] (can he also provide bread and meat for [us], his people?/we doubt that he can also provide bread and meat for us, his people.)” [RHQ]
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 So, when Yahweh heard that, he became very angry, and he sent a fire to burn up [some of] his Israeli [people]. [MTY, DOU]
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 [He did that] because they did not trust in him, and they did not believe that he would rescue them.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 But God spoke to the sky above them; he commanded it to open [like] a door,
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 and [then food] fell down like rain, [food which they named] ‘manna’; God gave them grain from (heaven/the sky).
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 [So] the people ate the food that angels eat, [and] God gave to them all the manna that they wanted.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 [Later], he caused the wind to blow from the east, and by his power he also sent wind from the south,
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 and the wind brought birds which were as numerous as the grains of sand on the seashore.
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 God caused those birds to fall [dead] in the middle of (their camp)/the area where the people had put up their tents. [There were dead birds] all around their tents.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 [So] the people [cooked the birds and] ate the meat and their stomachs were full, because God had given them what they wanted.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 But before they had eaten all that they wanted, and while they were still eating it,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 God was [still] very angry with them, and he caused their strongest men to die; he got rid of [many of] the finest [young] Israeli men.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 In spite of all that, the people continued to sin; in spite of all the miracles that God had performed, they still did not trust that he [would take care of them].
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 So, he caused their lives to end as quickly as a puff of wind ends; they died when disasters suddenly struck them.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 When God caused [some of] them to die, [the others] turned to God; they repented and earnestly asked God [to save them].
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 They remembered that God is [like] a huge rock ledge [under which they would be safe] [MET], and that he, who was greater than any other god, is the one who protected/rescued them.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 But they [tried to] deceive God by what they said [MTY]; their words [MTY] were [all] lies.
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 They were not loyal to him; they disregarded/ignored the agreement that he had made with them.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 But God was merciful to his people. He forgave them for having sinned and did not get rid of them. Many times he refrained from becoming angry [with them] and restrained from furiously/severely [punishing them] [MTY].
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 He remembered/considered that they were only humans who die; they [disappear quickly] [SIM], like a wind that blows by and then is gone.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 Many times our ancestors rebelled against God in the desert and caused him to become very sad.
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Many times they did evil things, to find out [if they could do those things without God punishing them]. They frequently caused the holy God of Israel to become disgusted/sad.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 They forgot about his [great] power, and they (forgot/did not think) about the time when he rescued them from their enemies.
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 They forgot about when he performed many miracles in the area near Zoan [city] in Egypt.
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 He caused the [Nile] River (OR, their sources of water) to become [red like] blood, with the result that the people of Egypt had no water to drink.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 He sent among the people of Egypt swarms of flies that bit them, and he sent frogs that ate up everything.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 He sent locusts to eat their crops and the other things that grew in their fields.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 He sent hail that destroyed the grapevines, and sent frost that ruined the figs.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 He sent hail that killed their cattle and sent lightning that killed their sheep and cows.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Because God was fiercely angry with the people of Egypt, he caused them to be very distressed. The disasters that struck them were like a group of angels that destroyed [everything].
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 He did not lessen his being angry [with them], and he did not (spare their lives/prevent them from dying); he sent a (plague/serious illness) that killed [many of] them.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 He also caused all the firstborn sons of the people of Egypt to die.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 Then he led his people out [of Egypt] like [a shepherd leads] his sheep [SIM], and he guided them [while they walked] through the desert.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 He led them safely, and they were not afraid, but their enemies were drowned in the sea.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 [Later] he brought them to [Canaan], his sacred land, to [Zion] Hill (OR, the hilly area) and by his power [MTY] he enabled them to conquer [the people who were living there].
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 He expelled the people-groups while his people were advancing; he allotted part of the land for [each tribe] to possess, and he gave to the Israeli people the houses of those people who had been expelled.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 However, the Israeli people rebelled against God, who is greater than any other god, and they did many evil things to see if they could do those things without God punishing them, and they did not obey his commandments.
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Instead, like their ancestors did, they rebelled against God and (were not loyal to/did not faithfully [obey]) him; they were as [unreliable as] a crooked arrow [that does not go straight] [SIM].
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 Because they [worshiped] carved images of their gods on the tops of hills, they caused God to become angry [DOU].
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 He saw what they were doing and became very angry, so he rejected the Israeli people.
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 He no longer appeared to them at Shiloh in the tent where he had lived among them.
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 He allowed their enemies to capture [the sacred chest], [which was the symbol of] his power and his glory.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 Because he was angry with his people, he allowed them to be killed [MTY] [by their enemies].
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Young men were killed in battles, with the result that the young women had no one to marry.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 [Many] priests were killed by [their enemies’] swords, and (the people did not allow the priests’ widows/the priests’ widows were not allowed) to mourn.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Later, [it was as though] the Lord awoke from sleeping; he was like a strong man who (became stimulated/felt that he was strong) by (OR, became sober after) [drinking] a lot of wine [SIM].
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 He pushed their enemies back and caused them to be [very] ashamed for a long time [HYP] [because they had been defeated].
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 [But] he did not set up his tent where [the people of] the tribe of Ephraim lived; he did not choose their area [to do that].
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Instead he chose [the area where] the tribe of Judah [lived]; he chose Zion Hill, which he loves.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 He [decided to have] his temple built [there], high up, like [his home in] heaven; he caused it to be firm, [and intended that] his temple would last forever, like the earth.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 He chose David, who served him [faithfully], and took him from the pastures
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 where he was taking care of his [father’s] sheep, and appointed him to be the leader [MET] of the Israeli people, the people who belong to God.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 David took care of the Israeli people sincerely and wholeheartedly, and guided them skillfully/wisely.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< Psalms 78 >