< Psalms 66 >

1 [Tell] everyone on the earth that they should sing joyfully to praise God!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 They should sing songs that say that God [MTY] is very great, and they should tell everyone that he is very glorious!
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 They should say to God, “The things that you do are awesome! You are very powerful, with the result that your enemies (cringe/bow down) in front of you.”
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 Everyone on the earth [should] worship God and sing to praise him and honor him [MTY].
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Come and think about what God has done! Think about the awesome things that he has done.
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 He caused the [Red] Sea to become dry land, [with the result that our] ancestors were able to walk right through it. There we rejoiced because of what he [had done].
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 By his great power he rules forever, and he keeps watching all the nations [to see what things they do], [so] those nations that want to rebel [against him] should not be proud.
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 You people [of all nations], praise our God! Praise him loudly in order that people will hear you as you praise him.
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 He has kept us alive, and he has not allowed us to (stumble/be defeated).
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 God, you have tested us; you have allowed us to experience great difficulties [to make our lives become pure] as [people] put precious metals in a hot fire [to burn out what is impure] [MET].
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 [It is as if] you allowed us to fall into traps [MET], and you [forced us to endure difficult things which were like] putting heavy loads on our backs [MET].
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 You allowed [our] enemies to trample on us; we [experienced difficulties/troubles that were like] [MET] walking through fires and floods, but now you have brought us into a place where we have plenty.
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 [Yahweh], I will bring to your temple offerings that are to be completely burned [on the altar]; I will offer to you what I promised.
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 When I was experiencing [much] trouble, I said that I would bring offerings to you [if you rescued me]; [and you did rescue me, so] I will bring to you what I promised.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 I will bring sheep to be burned on the altar, and I will [also] sacrifice bulls and goats, and when they are burning, [you will be pleased when] the smoke [rises up] ([to you/to the sky]).
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 All you [people] who revere God, come and listen, and I will tell you what he has done for me.
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 I called out to him to help me, and I praised him while I was speaking to him [MTY].
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 If I had ignored the sins that I had committed, the Lord would not have paid any attention to me.
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 But because [I confessed my sins], God has listened to me and he paid attention to my prayers.
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 I praise God because he has not ignored my prayers or stopped faithfully loving me.
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< Psalms 66 >