< Psalms 44 >

1 God, we ourselves have heard what our parents and grandparents told us. They told us about the miracles that you performed long ago.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 [They told us] how you expelled the ungodly people and enabled us to live in their land. [They told us] that you punished those ungodly people and enabled your own people to prosper [IDM].
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 It was not by using their own swords that they conquered the people that lived in that land, and it was not by their own power that they were victorious; it was only by your power [MTY, DOU] [that they did those things]; and they were sure that you were with them, and that showed that you were pleased with them.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 You are my King and my God; it is you who enable us, your people [MTY], to defeat our enemies.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 It is by your power that we knock our enemies down and tramp on them.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 I do not trust that I will be saved by using my bow [and arrows] and my sword.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 No, it is you who have rescued us from our enemies, it is you who have caused those who hate us to become ashamed [because they were defeated].
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 We have continually boasted about what God [has done for us], and we will thank him [MTY] forever.
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 But [now] you have rejected us and caused us to be disgraced; when our armies march out [to fight a battle], you no [longer] go with them.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 You have caused us to run away from our enemies, with the result that they captured the things that belonged to us.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 You have allowed us to become like [MET] sheep that were ready to be slaughtered; you scattered us [far away] among [other].
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 [It is as though] [MET] you sold us, your people, [to our enemies] for a very small price, and you did not gain much profit from selling us!
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 People who live in nations near us make fun of us; they laugh at us and deride/belittle us.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 They make jokes using the name of [our country], they shake their heads [to indicate that they despise us].
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 All day I feel disgraced; from seeing my face, people know that I am ashamed.
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 I hear what those who sneer at me and revile me say; I am ashamed in front of my enemies and those who want to harm me.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 All these things have happened to us [even] though we have not forgotten you, and we are not the ones who disobeyed the agreement you made with [our ancestors].
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 We have not stopped being loyal to you, and we have not stopped doing what you want us to do [IDM].
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 But [it is as though] you have allowed us to be helpless among wild animals, and abandoned us in a deep dark [ravine].
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 If we had forgotten to worship [MTY] our God, or if we had spread out our hands to [worship] a foreign god,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 you certainly would have known that, because you know [even] what we secretly think.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 But it is because we belong to you, [that our enemies] are constantly killing us. They act toward us as though we were only sheep to be slaughtered.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 [So], Yahweh, arise! Why are you asleep [RHQ]? Get up! Do not reject us forever!
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Why are you not looking at us? Why are you forgetting that we are suffering and being oppressed [by our enemies]?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 We are pushed down to the ground and we cannot get up.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Arise, and come and help us! Rescue us because you faithfully love us!
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

< Psalms 44 >