< Psalms 33 >
1 You righteous people should sing joyfully to Yahweh because that is what he deserves.
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 Praise Yahweh as you play songs on the lyre/harp. Praise him as you play [other] instruments that have many strings.
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 Sing a new song to him; Play those instruments well, and shout joyfully as you play them!
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 Yahweh always does what he says that he will do; we can trust that everything that he does is right.
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 He loves everything that we do that is just and right. People all over the earth can know that Yahweh faithfully loves us.
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 Yahweh created everything in the sky by commanding it. By what he said [MTY] he created all the stars.
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 He gathered all the water into one huge mass like [someone scoops liquid] into a container.
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 Everyone on the earth should revere Yahweh [DOU].
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
9 When he spoke, the world (was created/started to exist). Everything started to exist as a result of him commanding it.
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 Yahweh frustrates the things that the [pagan] nations decide to do. He prevents them from doing the [evil] things that they plan to do.
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 But what Yahweh decides to do will last forever. What he plans to do will never be changed.
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 Yahweh blesses those nations who choose him to be their God; He is pleased with those whom he has chosen to receive what he has promised.
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 Yahweh looks down from heaven and sees all us people;
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
14 from where he rules [MTY], he looks down on all the people who live on the earth.
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 He formed our inner beings, and he sees everything that we do.
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
16 It is not because a king has a great army that he is able to win [battles], and it is not because a soldier is very strong that he is able to defeat [his enemy].
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 It is foolish to trust that because horses are very strong that they will able to win a battle and save their riders.
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Do not forget that Yahweh watches over those who revere him, those who confidently expect him to faithfully love them.
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 He saves them [SYN] from dying [before they should die] and preserves them when there is a famine.
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 We trust that Yahweh will help us; he protects us like a shield protects a soldier [MET].
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 We rejoice because of what he [has done for us]; we trust in him because he [MTY] is holy.
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Yahweh, we pray that you will always faithfully love us while we confidently expect you [to do great things for us].
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.