< Psalms 25 >

1 Yahweh, my God, I give myself to you.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 I trust in you. Do not allow my enemies [to defeat me], with the result that I would be ashamed/disgraced. Do not allow my enemies to defeat/conquer me, with the result that they would rejoice.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Do not allow any of those who trust in you to be disappointed/disgraced. Cause those who (act treacherously toward/try to deceive) others to be disappointed/disgraced.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Yahweh, show me the way that I should (conduct my life/live as you want me to), teach me how to act in the manner that you want me to act/behave.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Teach me to conduct my life [by obeying] your truth because you are my God, the one who saves me. All the time I trust in you.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Yahweh, do not forget how you have acted mercifully to me and have faithfully loved me; that is the way that you have acted toward me from long ago.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Forgive me for all the sinful things I did and the ways that I rebelled against you when I was young; I ask this because you faithfully love your people and do good things for them, Yahweh, do not forget me!
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Yahweh is good and fair/just; therefore he shows sinners (how they should conduct their lives/how to live as you want them to).
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 He shows humble people what is right for them to do and teaches them what he wants [them to do].
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 He always faithfully loves and does what he has promised to those who keep his agreement with them and who do what he requires.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Yahweh, forgive me for all my sins, which are many, in order that I may honor you [MTY].
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 To all those who revere you [RHQ], you show them the (right way to conduct their lives/things that they should do).
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 They will always be prosperous, and their descendants will continue to live in [this] land.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Yahweh is a friend of those who have an awesome respect for him, and he teaches them the agreement that he [made with them].
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 I always ask [MTY] Yahweh to help me, and he rescues me from danger [MET].
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Yahweh, pay attention to me and be merciful to me, because I am alone, and I am very distressed because I am suffering/oppressed.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Help me to not worry, and rescue me from my troubles.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Note that I am distressed and troubled [DOU], and forgive [me for] all my sins.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Also note that I have many enemies, see that they hate me very much.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Protect me, and rescue me from them; do not allow [them to defeat me], [with the result that] I would be ashamed/disgraced; I have come to you to (get refuge/be safe).
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Protect me because I do what is good and honest/just [PRS], and because I trust in you.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 God, rescue [us] Israeli people from all of our troubles!
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Psalms 25 >