< Psalms 146 >

1 Praise Yahweh! With my whole inner being I will praise Yahweh.
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 I will praise Yahweh as long as I am alive; I will sing to praise my God for [the rest of] my life.
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 [You people], do not trust in your leaders; do not trust humans because they cannot save/rescue you [from your difficulties/problems].
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 And when they die, their corpses [decay and] become soil again. After they die, they can no longer do the things that they planned to do.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 But those whose helper is the God whom Jacob [worshiped] are happy. The one whom they confidently expect [to help them] is Yahweh, their God.
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 He is the one who created heaven and the earth and the oceans and all [the creatures] that are in them. He always does what he has promised to do.
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 He decides matters fairly for those who are (treated unfairly/oppressed), and he provides food for those who are hungry. He frees those who are in prison.
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 Yahweh enables those who are blind to see again. He lifts up those who have fallen down. He loves righteous [people].
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 Yahweh takes care of those from other countries who live in our land, and he helps widows and orphans. But he gets rid of wicked [people].
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 Yahweh will [continue to] be our king forever; you people of Israel, your God will rule forever! Praise Yahweh!
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.

< Psalms 146 >