< Psalms 143 >

1 Yahweh, hear me while I pray to you! Because you are righteous and because you faithfully do what you have promised, listen to what I am pleading that you [do for me].
Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
2 I am one who serves you; do not judge me, because you know that everyone has done things that are wrong).
Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
3 [My] enemies have pursued me; they have completely defeated me. [It is as though] they have put me in a dark [prison], where I [have nothing good to] ([hope for/expect]), like those who died long ago [SIM].
Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
4 So I am very discouraged; I am very dismayed/worried.
Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
5 I remember what has happened previously: I (meditate on/think about) all the things that you have done; I consider [all] the [great] deeds that you [SYN] have performed.
Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
6 I lift up my hands/arms to you while I pray; I [SYN] need you, like very dry ground [needs rain] [SIM].
Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
7 Yahweh, I am very discouraged, [so] please answer me right now! Do not hide from me, because if you do that, I will [soon] be [SIM] among those who descend to where the dead people are.
Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
8 [Every] morning cause me to remember that you faithfully love [me], because I trust in you. I (pray/send my prayers up [IDM]) to you; show me what I should do.
Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
9 Yahweh, I have gone/run to you to be protected, [so] rescue me from my enemies.
Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
10 You are my God; teach me to do what you want me to do. I want your good Spirit to lead me on a path that is not difficult to walk on.
Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
11 Yahweh, restore me when I am close to dying, as you promised to do. Because you are righteous/good, rescue me from my troubles/difficulties!
Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
12 I am one who serves you; so because you faithfully love [me], kill my enemies and get rid of all those who (oppress/cause trouble for) me.
Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.

< Psalms 143 >