< Psalms 125 >
1 Those/We who trust in Yahweh are [as secure/steadfast] [SIM] as Zion Hill, which cannot be shaken and can never be moved.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2 Like the hills that surround Jerusalem [protect the city], Yahweh protects [us], his people, and he will protect us forever.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Wicked people [MTY] should not [be allowed to] rule over the land where righteous [people] live. If they did that, those righteous [people] might [(be encouraged to imitate them and]) do things that are wrong.
Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
4 Yahweh, do good things to those who do good things to others and to those who sincerely obey your commands [IDM].
Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
5 But when you punish the wicked people [who are not Israelis], also punish those [Israelis] who turn away from walking on the good roads [MET] that you have shown them! I wish that things will go well for [people in] Israel!
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.