< Psalms 108 >

1 God, I am (very confident/trusting completely) [IDM] in you. I will sing to praise [you]. with all my inner being.
Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
2 I will arise before the sun rises, and I will [praise you while I play] my [big] harp and my (lyre/small harp).
Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
3 [I prayed], “Yahweh, I will thank you among [all] the people-groups; I will sing to praise you among the nations,
Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
4 because your faithful love for us reaches up to the heavens, and your faithfully doing what you promise [is as great as the distance] up to the clouds.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
5 Yahweh, [show] in the heavens that you are very great! And [show] your glory [to people] all over the earth!
Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
6 Answer our [prayers] and by your power help us [MTY] [to defeat our enemies] in order that we, the people whom you love, may be saved/rescued.”
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
7 And [Yahweh answered our prayers and] spoke from his temple, saying, “Because I have conquered [your enemies], I will joyfully [everything in] [city] and I will distribute among my people [the valuable things] in Succoth Valley.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
8 The Gilead [region] is mine; the [people of the tribe of] Manasseh are mine; [the tribe of] Ephraim is [like] my war helmet, and [the tribe of Judah] is like the (scepter/stick that I hold which shows that I am the ruler) [MET];
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
9 the Moab [region] is [like] my washbasin [MET]; I throw my sandal in the Edom [area to show that it belongs to me]; I shout triumphantly because I have defeated [the people of] the Philistia [area].”
Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
10 [Because we want to attack the people of] Edom, (who will lead my [army triumphantly] to their [capital] city that has strong walls around it?/I want someone to lead my [army triumphantly] to their [capital] city that has strong walls around it.) [RHQ]
Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
11 God, we [hope that] [RHQ] you have not abandoned us, and that you will go with us when our army marches out [to fight our enemies].
Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
12 [We need you to] help us when we fight against our enemies, because the help that humans can give us is worthless.
Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
13 [But] with you [helping us], we shall win; you will [enable us to] defeat our enemies.
Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.

< Psalms 108 >