< Psalms 106 >

1 Praise Yahweh! Praise Yahweh, because he does good things [for us]; he faithfully loves [us] forever/continually!
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 [Because Yahweh has done many great things], no one can [RHQ] tell all the great things that Yahweh has done, and no one can praise him enough/sufficiently.
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 (Happy are/He is pleased with) those who act fairly/justly, with those who always do what is right.
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Yahweh, be kind to me when you help your people; help me when you rescue/save them.
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 Allow me to see it when your people become prosperous again and when [all the people of] your nation, [Israel], are happy; allow me to be happy with them! I want to praise you along with [all] those [others] who belong to you.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 We and our ancestors have sinned; we have done things that were very wicked [DOU].
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 When our ancestors were in Egypt, they did not pay attention to the wonderful things that Yahweh did; they forgot about the many times that he showed that he faithfully loved them. Instead, when they were at the Red Sea, they rebelled against God, who is greater than any other god.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 But he rescued them for the sake of his own [reputation] in order that he could show that he is very powerful.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 He rebuked the Red Sea and it became dry, and [then] while he led our ancestors across it, they walked through it as though it were as dry as a desert [SIM].
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 In that way he rescued them from the power [MTY] of their enemies who hated them [DOU].
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 [Then] their enemies were drowned in the water [of the Red Sea]; not one of them was left.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 When that happened, our ancestors believed [that Yahweh had truly done for them] what he had promised to do, and they sang to praise him.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 But they soon forgot what he had done for them; they [did things] without waiting to find out what Yahweh wanted them to do.
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 They intensely wanted [food like they formerly ate in Egypt]. They [did evil things to] find out [if they could do those things without God punishing them].
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 [So] he gave them what they requested, but he [also] caused a terrible disease to afflict them.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 [Later] when [some of] the men became jealous of Moses and [his older brother] Aaron, who was dedicated [to serve Yahweh by being a priest],
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 the ground opened up and swallowed Dathan and [also] buried Abiram and his family.
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 And [God sent] a fire down [from heaven] which burned up [all] the wicked [people who (supported them/agreed with) them].
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Then the [Israeli leaders] made a gold statue at Sinai [Mountain] and worshiped it.
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 Instead of worshiping [our] glorious God, they [started to] worship a statue of a bull that eats grass!
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 They forgot about God, who had rescued them by the great miracles that he performed in Egypt.
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 They forgot about the wonderful things that he did for them in Egypt and the amazing/awesome things that he did for them at the Red Sea.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Because of that, God said that he would get rid of the Israelis, but Moses, whom God had chosen [to serve him], pleaded with God [not to get rid of them]. And as a result God did not destroy them.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 [Later], our ancestors (refused/were afraid) to enter beautiful [Canaan] land because they did not believe [that God would enable them to take the land from the people who were living there, as] he had promised.
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 They stayed in their tents and grumbled and would not pay attention to what Yahweh said that they should do.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 So he solemnly [MTY] told them that he would cause them to die [there] in the desert,
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 and that he would scatter their descendants among the [people of other] nations/people-groups [who did not believe in him], and that he would allow them to die in those lands.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Later the Israeli people [started to] worship [the idol of] Baal [who they thought lived] at Peor [Mountain], and they ate [meat that had been] sacrificed to [Baal and those other] lifeless gods.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 Yahweh became [very] angry because of what they had done, [so again] he sent a terrible disease to attack/strike them.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 But Phinehas stood up and punished/killed [the ones who had sinned greatly], and as a result the (plague/serious disease) ended.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 People have remembered that righteous thing that Phinehas did, and in future years people will remember it.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 [Then] at Meribah Springs our ancestors caused Yahweh to become angry, and as a result Moses had trouble.
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 They caused Moses to become very angry [IDM], and he said things that were foolish.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Our ancestors did not destroy the people [who did not believe in Yahweh] like he told them to do.
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 Instead, they mingled with people from those people-groups, and they started to do the evil things that those people did.
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 Our ancestors worshiped the idols of those people, which resulted in their being destroyed/exiled/taken to another country [MET].
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 [Some of] the Israelis sacrificed their sons and daughters to the demons [that those idols represented].
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 They killed [MTY] their own children, who (were innocent/had not done things that were wrong), and offered them as sacrifices to the idols in Canaan. [As a result], Canaan land was polluted by those murders [MTY].
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 So by their deeds they caused themselves to become unacceptable to God; [because they did not faithfully worship only God], [they became like] women who sleep with other men [instead of sleeping only with their husbands] [MET].
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 So Yahweh became very angry with his people; he was completely disgusted with them.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 [As a result] he allowed people-groups [who did not believe in him] to conquer them, so those who hated our ancestors started to rule over them.
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Their enemies (oppressed them/treated them cruelly) and completely controlled them [MET].
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Many times Yahweh rescued them, but they continued to rebel against him, and they were finally destroyed because of the sins that they committed.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 However, Yahweh [always] heard them when they cried out to him; he listened to them when they were distressed.
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 For their sake, he thought about the agreement/promise that he had made [to bless] them, and because he never stopped loving them very much, he changed his mind [about punishing them more].
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 He caused all those who had taken the Israelis [to Babylonia] to (feel sorry for/pity) them.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Yahweh our God, rescue/save us and bring us back [to Israel] from among those people-groups in order that we may thank you [MTY] and joyfully praise you.
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Praise Yahweh, the God whom [we] Israelis [worship], praise him now and forever! And I want everyone to say, “Amen/May it be so!” Praise Yahweh!
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< Psalms 106 >