< Proverbs 30 >

1 These are sayings/messages that God gave to Agur, the son of Jakeh. [Agur wrote them] for Ithiel and Ucal.
Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
2 It seems that I am very stupid; I do not deserve to be considered to be a human; I do not have the good sense that humans should have.
“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
3 I have not learned [how to become] wise and I do not know [much] about God.
Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
4 [But let me say this]: No one [RHQ] has ascended to heaven [to find out what God is like] and returned [to tell us]. No one [RHQ] has gathered/held the wind in his hand. No one [RHQ] has wrapped the water [in the ocean] in [a piece of] cloth, and no one [RHQ] has established the boundaries of the earth. [If you know who has done those things, tell me] [RHQ] his name, and the names of his children [SAR]! [But you do not know who has done those things, so you cannot speak with authority about what God is like].
Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
5 Everything that God has said is true; he is [like] a shield [MET] for all those who request him to protect them.
“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
6 Do not add to (OR, change) what God has said; if you do that, he will rebuke you and show that you are lying.
Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
7 [God], I ask you to do two things for me; [please] do them before I die:
“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
8 Help me never to lie or deceive [people] and do not cause me to become poor or to become rich. [Just] give me the food that I need;
Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
9 because if I become rich, I might say that I do not [RHQ] know you and that I do not need you; and if I become poor, I might dishonor you by stealing things.
kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
10 Do not (slander/say bad things about) a worker to his boss; if you do that, the worker will curse you, and cause you to have trouble.
“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
11 [I will list four kinds of evil things that people do]: Some people curse their fathers and do not [ask God to] bless their mothers.
“Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
12 Some people think that they are perfect, but [really] they have never been cleansed from their guilt for committing disgusting sins.
Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
13 Some people are very proud; they think that they are very good and they despise others.
Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
14 Some people [act very cruelly toward others]; [it is as though] [MET] they have teeth that are [like] sharp knives; they severely oppress poor [people] and try to cause them to disappear from the land.
Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
15 Leeches [are always wanting more blood to suck]; [similarly, greedy people are always] saying “Give [me some]!” or “Give [me more]!” [MET] There are four things that are never (satisfied/content with what they have); they always want more [LIT]:
“Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
16 The place where the dead people are; women who do not have any children; ground that needs water/rain; and a fire that always needs more wood. (Sheol h7585)
Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
17 Those who [SYN] make fun of their fathers or refuse to obey their mothers (OR, despise their aged mothers) should [die and] have their eyes pecked out by crows, and the [rest of their corpses should be] fed to the vultures.
Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
18 There are four things that are wonderful to me, [but] I do not understand any of them:
Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
19 How eagles fly in the sky, how snakes [are able to] move/crawl across a big rock, how ships sail on the seas, and how a man falls in love with a woman.
Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
20 This is what a woman who (is not faithful to/does not have sex only with) her husband does: She commits adultery [EUP], and [then] bathes and says, “I have not done anything that is wrong!”
Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
21 There are four things that no [one in] the world can tolerate:
Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
22 [What] a slave [does who] becomes a king, a foolish person eating [too much] food,
Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
23 [what] a woman who is hated [does when she] gets married, and [what] a female servant [does when she] becomes the boss instead of her mistress.
mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
24 [There are] four animals on the earth that are small, but they are very wise:
Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
25 Ants are not strong, but they store up food during the summer [in order to have it during the winter].
Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
26 Rock badgers [also] are not strong, but they make their homes among the rocks [where they will be safe].
mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
27 Locusts do not have a king, but they march like [the soldiers in] an army.
dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
28 Lizards/Geckos [are very small and] you can hold them in your hand, but they are [cleverly able to get] inside kings’ palaces.
Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
29 [There are] four animals that strut around and look very impressive while they walk [DOU]:
“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
30 Lions, which are stronger than all other animals and are not afraid of any of them;
Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
31 male goats, strutting roosters, and kings who (parade/walk proudly back and forth) in front of the people whom they rule.
Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
32 If you have acted foolishly, exalting yourself, or if you been planning [to do something] evil, stop it immediately [IDM]!
“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
33 If you churn milk, it produces butter/curds, and if you hit [someone hard on his] nose, [his nose] bleeds; similarly, if you do something to cause [people to become] angry, strife [usually] results.
Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

< Proverbs 30 >