< Proverbs 25 >

1 Here are more wise sayings/words that Solomon [wrote]. Some men who worked for Hezekiah, the king of Judah, copied them [from a scroll that Solomon had written].
Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
2 [We consider] God to be great because he (acts in mysterious ways/does things that we cannot understand); [we consider] kings to be great because they explain things.
Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
3 [It is not possible for anyone to measure] how high the sky is or how deep the earth/ocean is; likewise [SIM], it is not possible for us to know [all] that kings are thinking.
Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
4 [If workers] burn out the impure bits that are in silver, a man who makes things from silver can make something beautiful from the silver.
Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
5 [Similarly, if] wicked [advisors] are taken away from a king, his government will remain secure, because [the king will be able to] act justly.
Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
6 When you stand in front of a king, do not try to (impress him/honor yourself) and do not (act like you are important/ask to sit where important people sit; )
Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
7 it is better if someone tells you to sit closer [to the king] than for [someone to tell you], while the king is listening, to sit further away in order that someone who is more important [may sit closer to the king].
paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
8 Do not quickly go to a court [to tell the judge about] something that you have seen, because another witness may later [say something that proves that you are wrong, and as a result] you will be disgraced/ashamed. If that happens, (what will you do?/you will not know what to do.) [RHQ]
usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
9 If you and someone else think differently about some matter, settle it between yourselves, and do not tell others any secret [that he has told you].
Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
10 If others find out that you have told secrets, you will be ashamed, and from that time on, (you will have a bad reputation/people will think badly about you).
kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
11 Something that is said that is [very] appropriate is [as delightful as seeing] [SIM] gold apples/ornaments in a silver bowl.
Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
12 When a wise person rebukes/warns someone [SYN] who is willing to listen, that is [as valuable as] [SIM] a gold ring or a gold chain.
Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
13 A messenger who (is reliable/tells someone else exactly what he was told to say) refreshes [the spirits of] his bosses who sent him like [SIM] (snow/cold water) refreshes [the ground] at the time that [people] harvest crops.
Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
14 When someone promises to give a gift to us but never gives it, [that disappoints us] as much as [SIM] clouds and wind that come but do not bring any rain.
Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
15 If someone keeps requesting a ruler long enough to do something, he will [often] agree to do it; similarly, by speaking [MTY] gently we can [often] convince [others that what we say is right] [IDM].
Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
16 If you find some honey, do not eat a lot of it, because doing that may cause you to vomit.
Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 Do not go to your neighbor’s house very often [to talk with him]; if you go [very] often, he will get tired of listening to you and start to hate you.
Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
18 To falsely accuse others [in court] is like [SIM] [attacking them with] a war-club or a sword or a sharp arrow.
Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
19 Depending on unreliable people when you have troubles is [as bad] as [trying to eat when] you have a bad/hurting tooth or [trying to walk when] your foot is crippled.
Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
20 Singing to someone who is depressed [just causes him to feel worse]; it is like [SIM] taking off clothes on a very cold day or like putting vinegar on a wound.
Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
21 If your enemies are hungry, give them something to eat; if they are thirsty, give them something to drink;
Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 doing that will cause them to feel ashamed [IDM], and Yahweh will reward you for doing that.
Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
23 When wind blows from the right direction, it will rain; [similarly] [SIM], if we gossip about others, that causes them to look at us very angrily.
Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
24 It is better to live ([alone/by yourself]) in the corner of an attic/housetop than to live inside the house with a wife who is [always] nagging.
Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
25 Receiving good news from a country far away refreshes our spirits like [SIM] cold water refreshes us when we are very thirsty.
Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
26 When a righteous/good person (gives in/yields) to wicked [people], that is [as bad] as [SIM] a spring that becomes muddied or a fountain that becomes polluted.
Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
27 It is not good to eat too much honey, and trying to get people to praise you is also not good.
Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
28 People who (cannot control their tempers/quickly become very angry) [are unable to defend their behavior]; that is like [having] a city without a wall around it, [with the result that no one can defend it].
Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

< Proverbs 25 >