< Proverbs 10 >
1 These [are more] proverbs/wise sayings from Solomon: If children are wise, they cause their parents to be happy; but if children are foolish, they cause their parents to be very sad.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Money that you get by doing dishonest/wicked things will really not benefit you; but by living righteously you will live for (a long time/many years).
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 Yahweh does not allow righteous [people] to starve, but he will prevent wicked [people] from getting what they want.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 Lazy people [soon] become poor; it is those who work hard who become rich.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 Those who are wise, harvest the crops when they are ripe; it is shameful/disgraceful to sleep [and not work] during harvest time.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Righteous [people will] be blessed [by God]; [the nice things] that wicked [people] say [MTY] [sometimes] conceal the fact that they [are planning to] act violently.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 After righteous [people die], other people are blessed as they remember [what those people did before they died]; but we will soon forget wicked people [MTY] after they die.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Wise people heed good instruction/advice, but people who talk foolishly will ruin themselves.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Honest people will be safe, but [others] (OR, God) will find out those who are dishonest.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Those who signal with their eyes [that they are about to do something that is wrong] cause trouble, but those who rebuke others truthfully cause them to be peaceful.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 What righteous [people] say [MTY] is [like] a fountain that (gives life/enables people to live many years) [MET], but what wicked [people] say [MTY] hides [the fact] that they intend to act violently.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 When we hate others, it causes quarrels, but if we love others, we forgive them [for the wrong things that they do].
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 Those who have good sense say [MTY] what is wise, but people who do not have good sense must be punished.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Wise people continue to learn all that they can, but when foolish people speak, they soon cause trouble.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 The wealth that rich people have [protects them like a city is protected by a] strong wall around it [MET], but people who are poor suffer much [because they have no one to help them].
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 If you are righteous, your reward will be a good life, [but] all that sinful people gain is to sin more.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 Those who pay attention when others try to (correct them/teach them what they are doing that is wrong) will live (happily/for many years); but those who reject being rebuked will not find the road to life (OR, cause others to go astray).
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Those who will not admit that they hate [others] are liars, and those who slander [others] are foolish.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 When people talk a lot, that will lead them to sin a lot [by what they say]; if you are wise, you will refuse to say very much.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 What righteous/good [people] say [MTY] is [as valuable as] pure silver [MET]; what wicked [people] think is worthless.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 What righteous [people] say [MTY] benefits many [people], but foolish people die because of the stupid [things that they do].
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 Yahweh blesses [some people] by enabling them to become rich, and working hard will not make them to become richer (OR, and he will not also cause them to become sad).
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 Foolish people (have fun/enjoy) doing what is wrong, but wise/sensible people enjoy doing what is wise.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 Righteous [people] will get the good things that they want/desire, but what wicked [people] are afraid of is what will happen to them.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 When storms come, the wicked will (be blown away/never be safe), but righteous [people will] be safe forever.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 We do not like a lazy person who refuses to do the job that he is given to do, [just] like we do not like vinegar in our mouths or smoke in our eyes.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 If you revere Yahweh, you will live for a long time; but wicked [people] die before they become old.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 Righteous [people] confidently expect [that good things will happen to them], and that causes them to be happy/joyful; but when wicked [people] confidently expect something good to happen, it does not happen.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 Yahweh protects [MET] those who live righteously, but he destroys those who do what is evil.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 Righteous [people] will always be secure [LIT], but wicked people will be removed from their land (OR, from this earth).
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 Righteous people [MTY] say things that are wise, but [God] will shut the mouths of people [MTY] who say what is not true.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Righteous people [MTY] know what to say that is acceptable, but wicked [people] [MTY] are [constantly] saying things that are not true.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.