< Numbers 10 >
1 Yahweh also told Moses/me,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “[Tell someone to] make two trumpets by hammering each one from [one lump of] silver. Blow the trumpets to summon the people to come together and also to signal that they must move their tents [to a new location].
“Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
3 If both trumpets are blown, it means that everyone must gather together at the entrance of the Sacred Tent.
Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
4 If only one trumpet is blown, it means that only the [twelve] leaders of the tribes must gather together.
Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
5 If the trumpets are blown loudly, the tribes that are to the east [of the Sacred Tent] should start to travel.
Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
6 When the trumpets are blown loudly the second time, the tribes that are to the south should start to travel. The loud blasts on the trumpet will signal that they should start to travel.
Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
7 When you want only to gather the people together, blow the trumpets, but do not blow them as loudly.
Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
8 “The priests who are descended from Aaron are the ones who should blow the trumpets. That is a regulation that will never be changed.
“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
9 When you fight against enemies who attack you in your own land, tell the priests to blow the trumpets loudly. I, Yahweh, your God, will hear that, and I will rescue you from your enemies.
Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
10 Also tell the priests to blow the trumpets when the people are happy, and at the festivals [each year], and at the times when they celebrate the new moon each month. Tell them to blow the trumpets when the people bring offerings that will be completely burned, and when they bring offerings to maintain fellowship with me. If they do that, it will help you to remember that I, Yahweh your God, [will help you].”
Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
11 On the twentieth day of May in the second year [after the/we Israelis left Egypt], the cloud rose up from above the Sacred Tent.
Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
12 So we/the Israelis traveled from the Sinai Desert, and we/they continued traveling [north] until the cloud stopped in the Paran Desert.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
13 That was the first time we/they moved, obeying the instructions that Yahweh had given to Moses/me to tell them.
Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 The group that went first, carrying their flag/banner, was the group from the tribe of Judah. Nahshon, the son of Amminadab, was their leader.
Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
15 The group from the tribe of Issachar [followed them]. Nethanel, the son of Zuar, was their leader.
Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
16 The group from the tribe of Zebulun went next. Eliab, the son of Helon, was their leader.
Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
17 Then they dismantled the Sacred Tent, and the descendants of Gershon and Merari carried it, and they went next.
Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
18 The group from the tribe of Reuben went next, carrying their flag. Elizur, the son of Shedeur, was their leader.
Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
19 The group from the tribe of Simeon was next. Shelumiel, the son of Zurishaddai, was their leader.
Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
20 The group from the tribe of Gad was next. Eliasaph, the son of Deuel, was their leader.
ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
21 The group descended from Kohath was next. They carried the sacred items from the Sacred Tent. The Sacred Tent itself was set up at the new location before they arrived there.
Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
22 The group from the tribe of Ephraim was next, carrying their flag. Elishama, the son of Ammihud, was their leader.
Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
23 The group from the tribe of Manasseh went next. Gamaliel, the son of Pedahzur, was their leader.
Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
24 The group from the tribe of Benjamin, went next. Abidan, the son of Gideoni, was their leader.
Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
25 The ones who went last were the group from the tribe of Dan, carrying their flag. Ahiezer, the son of Ammishaddai, was their leader.
Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 The group from the tribe of Asher went next. Pagiel, the son of Ocran, was their leader.
Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
27 The group from the tribe of Naphtali went last. Ahira, the son of Enan, was their leader.
ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
28 That was the order in which the groups of Israeli tribes traveled.
Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
29 One day Moses/I said to his/my brother-in-law Hobab, the son of Reuel from the Midian people-group, “We are on the way to the place that Yahweh promised to give to us. Come with us, and we will take good care of you, because Yahweh has promised [to do] good things for us Israeli people.”
Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
30 But Hobab replied, “No, I will not go with you. I want to return to my own land and to my own family.”
Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
31 But Moses/I said, “Please do not leave us. You know the places where we can set up our tents in this desert, and you can guide us.
Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
32 Come with us. We will share with you all the good things that Yahweh gives to us.”
Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
33 [So Hobab agreed to go with them]. The Israelis left Sinai Mountain, [which they called] Yahweh’s Mountain, and they walked for three days. The [men carrying the] sacred chest went in front of the other people for those three days, and they kept looking for a place to set up their tents.
Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
34 The cloud sent by Yahweh was over them every day.
Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
35 Each morning when the men who were carrying the sacred chest started to walk, Moses/I said, “Yahweh, arise! Scatter your enemies! Cause those who hate you to run away from you!”
Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
36 And each time the men [stopped to] set down the sacred chest, Moses/I said, “Yahweh, stay close to the thousands of us Israelis!”
“Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”