< Nehemiah 8 >

1 Ezra, who taught people the laws of Moses, [had a scroll on which] the laws of Moses were written. Those were the laws that Yahweh had commanded the Israeli people [to obey]. On October 8 of that year, all the people gathered together in the plaza/square that was close to the Water Gate. Men and women and [children] who [were old enough to] understand gathered together. Someone told Ezra to bring out that scroll.
Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
2
Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
3 So he brought it out and read it to the people. He started reading it early in the morning and continued reading it until noontime. All the people listened carefully to the laws that were written on the scroll.
Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
4 Ezra stood on top of a high wooden platform that had been built just for that event. At his right side stood Mattithiah, Shema, Anaiah, Uriah, Hilkiah, and Maaseiah. At his left side stood Pedaiah, Mishael, Malkijah, Hashum, Hashbaddanah, Zechariah, and Meshullam.
Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
5 Ezra stood on the platform above the people, where they could all see him. He opened the scroll; and as he did that, all the people stood up, [and they continued to stand, to show respect for God’s word].
Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
6 Then Ezra praised Yahweh, the great God, and all the people lifted up their hands and said, “Amen! Amen!” Then they all bowed down with their foreheads touching the ground, and they worshiped Yahweh.
Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
7 Jeshua, Bani, Sherebiah, Jamin, Akkub, Shabbethai, Hodiah, Maaseiah, Kelita, Azariah, Jozabad, Hanan, and Pelaiah, were all (Levites/men who worked in the temple). They explained the meaning of the laws of Moses to the people who were standing there.
Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
8 They also read from scrolls that contained the laws that God [gave to Moses], and they interpreted [into the Aramaic language] what they read, making the meaning clear so that the people could understand the meaning.
Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
9 Then I, Nehemiah the governor, and Ezra, and the Levites who were interpreting what was being read to the people, said to them, “Yahweh your God considers that this day is very holy/sacred. So do not be sad or cry!” They said that because all the people were crying as they were listening to the laws of Moses.
Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
10 Then I said to them, “Now go home and enjoy [some] good food and drink [some] sweet wine. And send some of it to people who do not have anything [to eat or drink]. This is a day that Yahweh considers sacred. Do not be sad! Yahweh will cause you to be joyful and make you strong.”
Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
11 The Levites also caused the people to be quiet, saying “Be quiet [and do not cry], because this is a sacred day! Do not be sad!”
Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
12 So the people went away, and they ate and drank, and they sent portions of food [to those who did not have any]. They celebrated very joyfully, because they had heard and understood what had been read to them.
Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
13 The next day, the leaders of the families and the priests and [other] descendants of Levi met with Ezra to study carefully the laws that Yahweh had given to Moses.
Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
14 While they were doing that, they realized that Yahweh had told Moses to command the Israeli people to live in shelters during that month, [to remember that their ancestors lived in shelters when they left Egypt].
Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
15 They also learned that they should proclaim in Jerusalem and in all the towns that the people should go to the hills and cut branches from olive trees [that they have planted] and from wild olive trees and from myrtle trees and palm trees and fig trees. They should make shelters from these branches, and live in those shelters during the festival, just as Moses wrote [that they should do].
Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
16 So the people went out [of the city] and cut branches and used them to build shelters. They built shelters on the [flat] roofs [of their houses], in their courtyards, in the courtyards of the temple, and in the plazas/squares close to the Water Gate and the Ephraim Gate.
Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
17 All of the Israeli people who had returned from Babylon built shelters and lived in them [for one week]. The Israeli people had not celebrated that festival like that since the time that Joshua lived. And they were very joyful.
Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
18 Every day during that week Ezra read to the people from the scroll that contained the laws that God [gave Moses]. Then on the eighth day, just as one of the laws of God said that they should do, they gathered together to end the celebration.
Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.

< Nehemiah 8 >