< Micah 5 >

1 “But now, [you people of Jerusalem, gather your troops together, ] [because even though] you have a wall [around your city to protect it], [enemy soldiers] are surrounding the city. And [soon] they will strike your leader on his face, with a rod.”
Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
2 But you [people of] [APO] Bethlehem in Ephrathah [district need to know that] even though your [town] is a very small one among all the towns in Judah, someone who will rule Israel will be born in your town. [He will be] someone whose family has existed a very long time ago [DOU].
“Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
3 [But now] you people of Israel will be conquered by your enemies; [but it will be for only a short time], like [MET] [the short time that] women have great pain while their babies are being born. After that, your fellow-countrymen who were (exiled/forced to go to other countries) will return to their own country.
Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
4 And that man who will be ruling [there in Jerusalem] will stand and lead his people well, because Yahweh, his God, will cause him to be strong and greatly honored. Then the people whom he rules will live [in Jerusalem] safely; he will be greatly honored by people all over the earth, [so no one will dare to attack Jerusalem].
Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
5 And he will cause things to go well [for his people]. When [the army of] Assyria attacks our country and breaks though our fortresses, we will appoint (seven or eight/several) leaders [to lead our army] to fight against them.
Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
6 With their swords [our army] will defeat the [army of] Assyria, [whose capital was founded by] Nimrod [long ago]. So our army will rescue us from the Assyrian [army] when they invade our country [DOU].
Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
7 The (descendants of Jacob/Israelis) who survive will be [a blessing] to the people of other nations, like [SIM] dew and rain sent by Yahweh do good to the grass. The Israelis will not trust in humans [to help them]; instead, they will rely on Yahweh.
Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
8 In the midst of [their enemies in] many people-groups [DOU], the descendants of Jacob who remain alive will be like [SIM] a lion among the [other] wild beasts of the forest, like [SIM] a young lion who goes among a flock of sheep and pounces [on one] and (mauls it/tears it to pieces), and no one will be able to rescue [that sheep].
Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
9 You Israelis will defeat [MTY] all your enemies and completely destroy them.
Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
10 Yahweh says, “At that time, I will destroy [you Israeli people’s] horses [that your soldiers use in war] and your chariots.
Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
11 I will tear down your city [walls] and destroy all your fortified cities.
Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
12 I will get rid of all those among you who practice magic and the (fortune-tellers/those who say that they can predict what will happen in the future).
Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
13 I will destroy [all] your idols and [sacred stone] pillars, and then you will no longer bow down [and worship] things that you yourselves [SYN] have made.
Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
14 I will get rid of your poles [that represent the goddess] Asherah, and [I will also] destroy all your idols.
Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
15 And because I will be very angry, I will [also] punish [the people of] all the nations who have not obeyed [me].”
Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”

< Micah 5 >