< Matthew 20 >
1 “[In order to illustrate how God rewards people], I will compare [the way] God [MTY/EUP] rules his people with what the owner of an estate [did]. Early in the morning the owner of the estate went to [the market] where [people who wanted work gathered]. He went there to hire laborers to work in his vineyard.
“Ufumu wakumwamba uli ngati mwini munda amene anapita mmawa kukalemba anthu aganyu kuti akagwire ntchito mʼmunda wake wa mpesa.
2 He promised the men whom he hired that he would pay them the standard wage [for working] one day. Then he sent them to his vineyards.
Anagwirizana kuwalipira dinari monga malipiro a tsiku limodzi ndipo anawatumiza mʼmunda wake wamphesa.
3 At nine o’clock [that same morning] he went back [to the market]. There he saw more men who did not have work.
“Nthawi 9 koloko mmawa, anatulukanso naona ena atayimirira pa msika akungokhala.
4 He said to them, ‘Go to my vineyard as other men have done, [and work there]. I will pay you whatever is a just [wage].’ [So they also went to his vineyard and began to work].
Anawawuza kuti, ‘Inunso pitani mukagwire ntchito mʼmunda wanga wa mpesa, ndipo ndidzakulipirani malipiro oyenera.’
5 At noon and at three o’clock he again went [to the market] and found [other laborers whom he promised to pay a fair wage].
Ndipo anapita. “Anatulukanso nthawi ya 12 koloko masana, ndi nthawi ya 3 koloko masananso nachita chimodzimodzi.
6 At five o’clock he went [to the market again] and saw other [men] standing [there who were not working]. He said to them, ‘Why are you standing here all day and not working?’
Nthawi ya 5 koloko madzulo anatulukanso ndipo anapeza enanso atangoyimirira. Anawafunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mukungoyimirira pano tsiku lonse osagwira ntchito?’
7 They said to him, ‘Because no one has hired us.’ He said to them, ‘[I will hire you]. Go to my vineyard as other men have done, [and work there.’ So they went].
“Iwo anayankha kuti, ‘Chifukwa palibe munthu amene watilemba ganyu.’ “Iye anawawuza kuti, ‘Inunso pitani mukagwire ntchito mʼmunda wanga wa mpesa.’
8 When evening came, the owner of the vineyard said to his manager, ‘Tell the men to come so that you can give them their wages. First, pay the men who started working last, and pay the men last who started working first.’
“Ndipo pofika madzulo, mwini munda wamphesa anayitana kapitawo wake nati, ‘Itana antchito ndipo uwapatse malipiro awo, kuyambira omalizira aja mpaka oyamba.’
9 The [manager] paid the standard daily wage to each of the men who did not start working until five o’clock [in the afternoon].
“Antchito amene anawalemba ganyu pa 5 koloko masana anafika ndipo aliyense analandira dinari.
10 When the men who had begun working early [in the morning] went [to get their wages], they thought that they would receive more than the standard wage. But they also received only the standard wage.
Ndipo atabwera kwa amene analembedwa poyamba anayembekezera kuti alandira zambiri. Koma aliyense wa iwo analandira dinari.
11 So they complained to the owner of the vineyard [because they thought their payment was unfair].
Atalandira, anayamba kuderera kwa mwini mundayo.
12 They said [to him], ‘[You are not being fair!] The men who started working after [all of the rest of us started] worked for [only] one hour! You have [paid] them the same [wage] as [you paid] us! But we worked hard [all] day [IDM], [including working in the] hottest part of the day!’
Iwo anati, ‘Anthu amene munawalemba pomalizira agwira ntchito ora limodzi, ndipo mwawafananitsa ndi ife amene tathyoka nayo ntchito ndi kutentha kwa dzuwa tsiku lonse.’
13 The owner of the vineyard said to one of those [who complained], ‘Friend, I did not treat you unfairly. You agreed with me [to work the whole day] for the standard wage [RHQ].
“Koma iye anamuyankha mmodzi wa iwo nati, ‘Bwenzi, ine sikuti sindinachite chilungamo. Kodi sunavomereze kuti ugwira ntchito ndi kulandira dinari?
14 [Stop complaining to me]! Take your wage and go! I desire to give the same wage that I gave you to the men who began working after all of you [had begun working].
Tenga malipiro ako pita. Ndikufuna kumupatsa munthu amene ndinamulemba pomaliza mofanana ndi mmene ndakupatsira iwe.
15 I certainly have a right to [spend my money] as I desire [RHQ], [including paying those laborers what I desire to pay them]. (You should not be envious about my being generous!/Are you angry [MET] because I am generous?) [RHQ]’”
Kodi ndilibe ufulu wochita zimene ndikufuna ndi ndalama zanga? Kapena ukuyipidwa chifukwa ndine wopereka mowolowamanja?’
16 [Then Jesus said to us], “Similarly, [God will reward] well [some] people who [seem to be] less important now, and he will not reward [some] people who [seem to be] more important [now].”
“Momwemo omalizira adzakhala oyamba ndipo oyamba adzakhala omalizira.”
17 When Jesus was walking [on the road] up to Jerusalem, [along with us] twelve [disciples], he took us to a place by ourselves [in order that he could talk to us privately]. Then he said to us,
Tsopano pamene Yesu ankapita ku Yerusalemu, anatengera pambali ophunzira ake khumi ndi awiriwo nati kwa iwo,
18 “Listen carefully! We are [now] going up to Jerusalem. [While we are there, someone] will enable the chief priests and the men who teach the [Jewish] laws to seize [me], the one who came from heaven, [and they will put me on trial]. They will condemn me [and say] that I should be killed {the authorities should kill me}.
“Tikupita ku Yerusalemu, ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo adzamuweruza kuti aphedwe,
19 [Then they] will put me in the hands of non-Jews so that they can make fun of me, whip me, [and kill me by] nailing me to a cross. But on the third day [after that], [God] will cause me to live again.”
ndipo adzamupereka kwa anthu a mitundu ina kuti amunyoze ndi kumukwapula ndi kumupachika. Pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa!”
20 Then the mother of James and John brought her two sons to Jesus. She bowed down before Jesus and asked him to do her a favor.
Amayi a ana a Zebedayo anabwera ndi ana ake kwa Yesu, nagwada pansi namupempha Iye.
21 Jesus said to her, “What do you want [me to do for you]?” She said to him, “Permit these two sons of mine to sit next to you (OR, Permit these two sons of mine to sit next to you at your right side and at your left side) [and rule with you] [MTY] when you become king.”
Yesu anawafunsa kuti, “Mukufuna chiyani?” Amayiwo anati, “Lolani kuti ana anga awiriwa adzakhale mmodzi ku dzanja lanu lamanja ndi wina ku dzanja lanu lamazere mu ufumu wanu.”
22 Jesus said to [her and her sons], “You do not understand what you are asking for. Can you suffer like I am about to suffer [IDM]?” [James and John] answered him, “Yes, we are able [to do that].”
Yesu anawawuza kuti, “Simukudziwa chimene mukupempha. Kodi mungathe kumwera chikho chimene ndidzamwera Ine?” Iwo anayankha nati, “Inde tingathe.”
23 Then Jesus said to them, “Yes, you will suffer as I will suffer [IDM]. But I am not the one who chooses the ones who [will] sit next to me [and rule with me]. [God], my Father, will give those places [MTY] to the ones whom he appoints.”
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi mudzamwera chikho changa, koma kuti mudzakhale ku dzanja langa lamanja kapena lamazere si kwa Ine kupereka. Malo awa ndi a iwo amene anakonzeredweratu ndi Atate anga.”
24 When we ten [other disciples] heard [what James and John had requested], we became angry with them [because we also wanted to rule with Jesus in the highest positions].
Ophunzira khumi aja, anawapsera mtima abale awiriwo.
25 [So] Jesus called all of us together and said [to us], “You know that those who rule the non-Jews [enjoy] showing them that they are powerful. Their chief rulers [enjoy] commanding the people under them.
Yesu anawayitana onse pamodzi nati, “Mukudziwa kuti olamulira a mitundu ina ali ndi mphamvu pa iwo, ndipo akuluakulu awo amawalamulira.
26 You [should] not be like them. On the contrary, everyone among you who wants [God to consider] him great must become [like] a servant for [the rest of] you.
Siziyenera kutero ndi inu. Mʼmalo mwake, aliyense amene akufuna kukhala wamkulu pakati panu akhale wotumikira wanu.
27 And everyone among you who wants [God to consider him] to be the most important must become [like] a slave for [the rest of] you.
Ndipo aliyense amene akufuna kukhala woyamba akhale kapolo wanu.
28 [You should imitate me]. [Even though I am] the one who came from heaven, I did not come to be served {in order that people would serve me}. On the contrary, I [came in order] to serve [others] and to [IDM] allow myself to be killed {other people to kill me}, so that [my dying would be like] a payment to rescue many [people from being punished for their sins].” [MTY]
Momwenso Mwana wa Munthu sanabwere kudzatumikiridwa, koma kudzatumikira, ndi kupereka moyo wake kukhala dipo la anthu ambiri.”
29 As we were leaving Jericho [city], a large crowd of people followed [us].
Pamene Yesu ndi ophunzira ake ankachoka ku Yeriko, gulu lalikulu la anthu linawatsata.
30 [As we walked along, we saw] two blind men sitting alongside the road. When they heard that Jesus was passing by, they yelled [to him], “Lord, Descendant of [King] David, [you are the Messiah] Take pity on us!”
Amuna awiri osaona anakhala mʼmbali mwa msewu, ndipo pamene anamva kuti Yesu akudutsa anafuwula kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”
31 [People in] the crowd scolded them [and] told them to be quiet. But the blind men yelled even louder, “Lord, Descendant of [King] David, [you are the Messiah] Have pity on us!”
Gulu la anthulo linawadzudzula iwo ndi kuwawuza kuti akhale chete, koma anafuwulitsabe kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”
32 Jesus stopped and called them [to come to him]. [Then] he said [to them], “What do you want me to do for you?”
Yesu anayima ndi kuwayitana ndipo anawafunsa kuti, “Mukufuna ndikuchitireni chiyani?”
33 They said to him, “Lord, heal our eyes [IDM] [so that we can see]!”
Anamuyankha nati, “Ambuye, tikufuna tione!”
34 Jesus [felt] sorry [for them and] touched their eyes. Immediately they were able to see, and they went with Jesus.
Yesu anamva nawo chifundo ndipo anakhudza maso awo. Nthawi yomweyo anaona namutsata Iye.