< Matthew 2 >

1 Jesus was born in Bethlehem [town] in Judea [province] during the time [MTY] that King Herod [the Great ruled there. Some time] after Jesus was born, some men who studied the stars and who lived in a [country] east [of Judea] came to Jerusalem.
Atabadwa Yesu mʼBetelehemu wa ku Yudeya, mʼnthawi ya mfumu Herode, Anzeru a kummawa anabwera ku Yerusalemu
2 They asked [people], “Where is the one who has been born [in order that he might be] the king of [you] Jews? [We believe that your new king] has been born, because we have seen the star [that we believe indicated that] he has been [born]. [We saw it while we were in our country] east [of here]. So we have come to worship him.”
nafunsa kuti, “Ali kuti amene wabadwa kukhala mfumu ya Ayuda? Chifukwa tinaona nyenyezi yake kummawa ndipo tabwera kudzamupembedza.”
3 When King Herod heard [what those men were asking], he became worried [that someone else might be proclaimed] {[people might proclaim someone else]} [king of the Jews to replace him]. Many [of the people] of Jerusalem [MTY, HYP] [also] became worried [because they were afraid of what King Herod might do].
Mfumu Herode atamva zimenezi, anavutika mu mtima kwambiri pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu.
4 Then Herod gathered together all the ruling priests and men who taught the people the [Jewish] laws and he asked them where [the prophets had predicted that] the Messiah was to be born.
Ndipo anayitanitsa anthu onse, akulu ansembe ndi aphunzitsi amalamulo nawafunsa kuti, “Kodi Khristu adzabadwira kuti?”
5 They said to him, “[He will be born] in Bethlehem, [here] in Judea [province], because it was written by the prophet [Micah] {the prophet [Micah] wrote} [long ago what God said]:
Ndipo anamuyankha kuti, “Ku Betelehemu wa ku Yudeya chifukwa izi ndi zimene mneneri analemba kuti,
6 ‘You [who live in] Bethlehem [APO], in Judea [province], your town is certainly very important [LIT], because a man from your [town] will become a ruler. He will guide my people [who live in] Israel.’”
“‘Koma iwe Betelehemu, chigawo cha Yudeya, sindiwe wamngʼonongʼono mwa olamulira a Yudeya; pakuti otsogolera adzachokera mwa iwe, amene adzaweta anthu anga Aisraeli.’”
7 Then [King] Herod secretly summoned those men who studied the stars. He asked them exactly when the star [first] appeared. [By what they told him, he was able to know the approximate age of the baby].
Pomwepo Herode anawayitanira mseri Anzeruwo nawafunsitsa nthawi yeniyeni yomwe nyenyeziyo inaoneka.
8 Then he [concealed what he really planned to do and] said to them, “Go to Bethlehem and inquire thoroughly [where] the infant is. When you have found him, [come back and] report to me so that I, myself, can go [there and] worship him, too.”
Ndipo anawatumiza ku Betelehemu nawawuza kuti, “Pitani mukafufuze za mwanayo mosamalitsa. Ndipo mukamupeza mudzandiwuze kuti inenso ndikamupembedze.”
9 After the men heard what the king [told them], they went [toward Bethlehem]. To their surprise, the star that they had seen while they were in the eastern [country] went ahead of them [again] until it stood above [the house] where the child was.
Atamva mawu a mfumu, ananyamuka ulendo wawo, ndipo taonani nyenyezi anayiona kummawa ija, inawatsogolera mpaka inayima pamwamba pa nyumba yomwe munali mwanayo.
10 When they saw the star, they rejoiced greatly [and followed it].
Pamene iwo anaona nyenyeziyo, anasangalala kwambiri.
11 They [found] the house and entered it and saw the child and his mother, Mary. They bowed down and worshipped him. Then they opened their treasure [boxes] [MTY] and they gave gold, [costly] frankincense, and myrrh to him.
Pofika ku nyumbayo, anaona mwanayo pamodzi ndi amayi ake Mariya, ndipo anagwada namulambira Iye. Pomwepo anamasula chuma chawo ndi kupereka mphatso zawo za ndalama zagolide, lubani ndi mure.
12 [Because] God [knew that King Herod planned to kill Jesus], in a dream the men who studied the stars were warned {he warned the men who studied the stars} that they should not return to [King] Herod. So they returned to their country, [but instead of traveling back on the same road, they] went on a different road.
Ndipo atachenjezedwa mʼmaloto kuti asapitenso kwa Herode, anabwerera ku dziko la kwawo podzera njira ina.
13 After the men who studied the stars left [Bethlehem], an angel [from] the Lord appeared to Joseph in a dream. He said, “Get up, take the child and his mother, and flee to Egypt. Stay there until I tell you [(sg) that you should leave], because [King] Herod is about [to send soldiers] to look for the child so that they can kill him.”
Atachoka, taonani mngelo wa Ambuye anaonekera kwa Yosefe mʼmaloto nati, “Tadzuka, tenga mwanayo pamodzi ndi amayi ake ndipo muthawire ku Igupto. Mukakhale kumeneko mpaka nditakuwuza pakuti Herode adzafunafuna mwanayo kuti amuphe.”
14 So Joseph got up, he took the child and his mother [that] night, and they fled to Egypt.
Atadzuka, Yosefe anatenga mwanayo ndi amayi ake usiku omwewo napita ku Igupto,
15 They stayed there until [King] Herod died, [and then they left Egypt]. By doing that, it was {they} fulfilled what the prophet [Hosea] wrote, which had been said by the Lord {which the Lord had said}, I have told my son to come out of Egypt.
nakhala kumeneko mpaka Herode atamwalira. Ndipo zinakwaniritsidwa zomwe ananena Ambuye mwa mneneri kuti, “Ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.”
16 [While King] Herod [was still living], because he realized that he had been tricked by the men who studied the stars {the men who studied the stars had tricked him}, he became furious. Then, [assuming that Jesus was still in Bethlehem or the surrounding regions], Herod sent [soldiers there] to kill all the boy babies two years old and younger. [Herod calculated how old the baby was], according to what the men who studied the stars told him [about when the star first appeared].
Herode atazindikira kuti Anzeruwo anamupusitsa, anakwiya kwambiri. Ndipo anatumiza anthu kukapha ana onse aamuna a mʼBetelehemu ndi midzi yozungulira amene anali a zaka ziwiri kapena zocheperapo, molingana ndi nthawi imene Anzeruwo anamuwuza.
17 [Because Bethlehem and Ramah towns were in the area where the descendants of Jacob’s wife Rachel lived, when soldiers killed the infant boys], they fulfilled what Jeremiah the prophet wrote,
Pamenepo, zimene ananena mneneri Yeremiya zinakwaniritsidwa:
18 [Women] in Ramah were weeping and wailing loudly. [Women who were the descendants] of Rachel, [the ancestor of the women there] [SYN], were grieving for [what happened to] their children. [Even though people tried to comfort them], they would not be comforted {stop mourning}, because their children were dead.
“Kulira kukumveka ku Rama, kubuma ndi kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake; sakutonthozeka, chifukwa ana akewo palibe.”
19 After Herod died [and while Joseph and his family were still in Egypt], an angel that the Lord [had sent] appeared to Joseph in Egypt in a dream.
Atamwalira Herode, mngelo wa Ambuye anaonekera kwa Yosefe mʼmaloto ku Igupto
20 He said to Joseph, “Take the child and his mother and go back to Israel [to live], because the people who were looking for the child [in order to kill him] have died.”
nanena kuti, “Nyamuka, tenga mwanayo ndi amayi ake ndipo mupite ku dziko la Israeli, popeza amene anafuna moyo wa mwanayo anamwalira.”
21 So Joseph took the child and his mother, and they went back to Israel.
Tsono Yosefe atadzuka anatenga mwanayo ndi amayi ake kupita ku dziko la Israeli.
22 When Joseph heard that Archaelaus now ruled in Judea [district] instead of his father, [King] Herod [the Great], he was afraid to go there. Because he was warned {[God] warned Joseph} in a dream [that it was still dangerous for them to live in Judea], he [and Mary and Jesus] went to Galilee [District]
Koma atamva kuti Arikelao akulamulira mu Yudeya mʼmalo mwa abambo ake, Herode, anaopa kupitako. Atachenjezedwa mʼmaloto, anapita ku Galileya,
23 to Nazareth [to live there]. The result was that what had been said by the ancient prophets {what the ancient prophets had said} [about the Messiah], that he would be called {people would call him} a Nazareth-man, was fulfilled {came true}.
ndipo anakakhazikika mu mzinda wa Nazareti. Pamenepo zinakwaniritsidwa zonenedwa ndi aneneri kuti, “Adzatchedwa Mnazareti.”

< Matthew 2 >