< Matthew 18 >
1 About that time we disciples approached Jesus and said, “Who [among us will be] the most important when God [MTY/EUP] [makes you] king?”
Pa nthawi imeneyo ophunzira anabwera kwa Yesu ndipo anamufunsa kuti, “Wamkulu woposa onse ndani mu ufumu wakumwamba?”
2 Jesus called a child to come, and he placed that child in our midst.
Iye anayitana kamwana kakangʼono ndi kukayimiritsa pakati pawo.
3 He said, “Think about this: If you [(pl)] do not change [the way you(pl) think] and become [as humble] as little children, you [(pl)] will surely not go to the place where God [MTY/EUP] rules.
Ndipo Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati simusintha ndi kukhala ngati tiana tatingʼono, simudzalowa konse mu ufumu wakumwamba.
4 The people who become as humble as this child [or any child] is, will be the most important people among those over whom God rules.
Chifukwa chake, aliyense amene adzichepetsa yekha ngati kamwana aka, ameneyo ndiye wamkulu koposa onse mu ufumu wakumwamba.
5 Also, when those who, [because they love] me, welcome [a] child like this one, [God considers] that they are welcoming me.”
Ndipo aliyense amene alandira kamwana kakangʼono ngati aka mu dzina langa, alandira Ine.
6 “If you cause someone who believes in me to sin, [even if it is someone who is socially unimportant like] this little child, [God will severely punish you]. If a heavy stone were fastened around your neck and you were thrown into the deep waters of the sea, [people would consider that you had been severely punished. But God will punish] you more severely [than that if you cause someone to sin]
“Koma ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana awa, amene akhulupirira Ine, kuti achimwe, kukanakhala bwino kuti iye amangiriridwe chimwala chachikulu mʼkhosi mwake ndi kumizidwa pansi pa nyanja.
7 It will be terrible for those [MTY] who cause others to stop believing in me. [God will punish them eternally]. It is inevitable that there will be [those who] cause others to stop believing in me. But it will be horrible for everyone who does that.
Tsoka dziko lapansi chifukwa cha zinthu zimene ziyenera kubwera, koma tsoka kwa munthu amene abweretsa zotere!
8 So, if you [are wanting to use] one of your hands or feet to sin, [stop using that hand or foot! Even if you have to] cut it off [to avoid sinning, do it] [MET]! It is good [that you not sin and] go where you will live [with God eternally, even though while you are still here on earth] you are maimed or lame and do not have a hand or a foot. But it is not good that you continue to have your two hands and two feet [and do] [MTY] [the sinful things you want to, and as a result], you are thrown into [hell], where there is eternal fire burning. (aiōnios , questioned)
Ngati dzanja lako kapena phazi lako likuchimwitsa, lidule ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kulowa mʼmoyo wosatha wolumala kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri kapena mapazi awiri ndi kukaponyedwa ku moto wosatha. (aiōnios )
9 If what you see you [makes you want] to sin, [stop looking at those things! Even if you have to] gouge out one of your eyes and throw it away [to avoid sinning, do it] [HYP]! It is good [that you not sin and] go where you will live [with God eternally, even though while you are still here on earth] you have only one eye. But it is not good that you continue to have your two eyes [and do the sinful things you want to, and as a result], you are thrown {God throws you} into hell where there is eternal fire burning.” (Geenna )
Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kuti ukalowe ku moyo wosatha ndi diso limodzi kuposa ndi kukhala ndi maso awiri ndi kukaponyedwa ku moto wa gehena.” (Geenna )
10 “Make an effort that you [(pl)] do not despise [even] one of these children. I tell you [(pl)] truly that [since] the angels [live] in heaven [in the presence of] my Father, [they will report to him if you mistreat the children].
“Onetsetsani kuti musanyoze mmodzi wa anawa. Pakuti ndikuwuzani kuti angelo awo kumwamba amakhala pamaso pa Atate anga akumwamba nthawi zonse.”
(Mwana wa Munthu anabwera kudzapulumutsa chimene chinatayika).
12 What do you [(pl)] think [you would do in the following situation]? If you had 100 sheep and one of them got lost, you would surely leave the 99 sheep [that are] on the hill and go and search for the lost one [RHQ], would you not?
“Kodi mukuganiza bwanji? Ngati munthu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi nʼkusowa, kodi sasiya 99 zija mʼmapiri ndi kupita kukafuna imodzi yosocherayo?
13 If you found it, I affirm to you [(pl)] that you would rejoice very much. You would be happy that 99 sheep did not stray away, but you would rejoice even more [because you had found] the sheep that had strayed away.
Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti akayipeza amasangalala kwambiri chifukwa cha nkhosa imodziyo kuposa nkhosa 99 zimene sizinasochere.
14 In the same way [that shepherds do not want one of] their [sheep to stray away], so [God], your Father in heaven, does not want [even] one of these children to go to hell.” ()
Chimodzimodzinso Atate anu akumwamba safuna kuti mmodzi wa anawa atayike.
15 “If a fellow believer sins [against you], go [to him], and when you two are alone, reprove him [for sinning against you]. If that person listens to you [and feels sorry that he has sinned against you], you will have restored [your friendship with] that person.
“Ngati mʼbale wako akuchimwira, pita kamuwuze cholakwa chake pa awiri. Ngati akumvera, wamubweza mʼbale wakoyo.
16 If that person will not listen to you [nor feel sorry that he has sinned against you], go get one or two other people [who will listen to what you both have to say]. Have them go with you so that [what is written] {[Moses wrote]} [in the Scriptures might happen: ] ‘[When one person accuses another in some matter], it should be confirmed by [at least] two or three people {[at least] two or three people should confirm it} [before that person can be declared] guilty {[before they declare that person guilty]}.’
Koma ngati sakumvera, katenge wina mmodzi kapena ena awiri, ‘kuti nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.’
17 If the one who has sinned against you will not listen to them [or does not feel sorry that he has sinned against you], tell that to the congregation [so that they can rebuke him]. If that person will not listen to the congregation [or feel sorry that he has sinned against you, exclude him from being a member of your congregation, just like] you [would exclude] pagans, tax collectors, [and others who do not believe in God and sin greatly].
Ngati iye akana kuwamvera iwo, kaneneni ku mpingo; ndipo ngati sakamvera ngakhale mpingo, muchite naye monga mukanachitira ndi wakunja kapena wolandira msonkho.
18 Keep this in mind: Whatever you decide on earth [about punishing] or [not punishing a member of your congregation] is what has also been decided by [God] in heaven {what [God] in heaven has also decided}.
“Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti chilichonse chimene muchimanga pa dziko lapansi, chidzamangidwanso kumwamba, ndipo chilichonse chimene muchimasula pa dziko chidzamasulidwanso kumwamba.
19 Also note this: If [at least] two of you [who live] here on earth agree together about something you ask [God] for [DOU], [God], my Father [who is] in heaven, will give you what you ask for.
“Komanso ndikukuwuzani inu kuti ngati awiri a inu pa dziko lapansi avomerezana kanthu kalikonse kamene mukapempha, Atate anga akumwamba adzakuchitirani.
20 [This is true], because wherever [at least] two or three of you assemble because you believe in me [MTY], I am [spiritually] present with you. I [will hear what you ask for and I will ask God to do it for you].”
Pakuti pamene awiri kapena atatu asonkhana pamodzi mʼdzina langa, Ine ndili nawo pomwepo.”
21 Then Peter approached [Jesus] and said to him, “How many times must I forgive a fellow believer who [keeps on] sinning against me? [If he keeps asking me to forgive him, must I forgive him] as many as seven times?”
Kenaka Petro anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti, “Ambuye, kodi mʼbale wanga akandichimwira ndimukhululukire kokwanira kangati? Mpaka kasanu nʼkawiri?”
22 Jesus said to him, “I tell you [that the number of] times [you must forgive someone is] not just up to seven, but [you must] ([forgive him] 77 times/never stop forgiving him).
Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuza iwe kuti osati kasanu nʼkawiri, koma ka 70 kuchulukitsa ndi kasanu nʼkawiri.
23 [In order to illustrate] why [you should do this], I [will tell you a story in which] God [MTY/EUP], [who cares for] the people whose lives he rules over, is compared {I compare God, [who cares for] the people whose lives he rules over} to a king [and his officials]. That king told [some of his servants that he wanted] his officials to pay what they owed him.
“Nʼchifukwa chake, ufumu wakumwamba ukufanana ndi mfumu imene inafuna kuti antchito ake abweze ngongole.
24 [So those officials were brought to the king to] settle [their accounts with him]. [One of the officials who were brought] owed the king several million dollars.
Atangoyamba kulandira, anamubweretsa munthu kwa iye amene anakongola ndalama 10,000.
25 But because he did not have [enough money] to pay [what he owed], the king demanded that he, his wife, his children and all he possessed be sold [to someone else, and that the king] be repaid [with] {receive} [the money that was paid for them].
Popeza sakanatha kubweza, bwanayo analamula kuti iye, mkazi wake, ana ake ndi zonse anali nazo zigulitsidwe kuti zibweze ngongoleyo.
26 Then that official, [knowing that he did not have the money to pay that huge debt], fell on his knees [in front of the king] and begged him saying, ‘Be patient with me, and I will pay you all of it, [eventually].’
“Wantchitoyo anagwada pamaso pake namupempha iye kuti, ‘Lezereni mtima ndipo ndidzabweza zonse.’
27 The king, [knowing that the official could never pay all that huge debt], felt sorry for him. So he canceled his debt and released him.
Bwana wakeyo anamuchitira chifundo, namukhululukira ngongoleyo ndipo anamulola apite.
28 Then this official went to another one of the king’s officials who owed him a bit less than a year’s wages. He grabbed him [by the throat], started choking him, and said to him, ‘Pay back what you owe [me]!’
“Koma wantchito uja atatuluka, anakumana ndi wantchito mnzake amene anakongola kwa iye madinari 100. Anamugwira, nayamba kumukanyanga pa khosi, namuwumiriza nati, ‘Bwezere zimene unakongola kwa ine!’
29 That official fell on his knees and begged him saying, ‘Be patient with me, and I will pay you all of it, [eventually].’
“Wantchito mnzakeyo anagwada namupempha iye kuti, ‘Lezere mtima ine, ndipo ndidzakubwezera.’
30 But this official kept refusing [to cancel that small debt that the man owed him]. Instead, he [caused that official to be] put in prison [and to stay there] until he could pay back all the money that he owed him.
“Koma iye anakana. Mʼmalo mwake, anachoka nakamumangitsa kufikira atabweza ngongoleyo.
31 When the other officials [of the king] learned that this had happened, they felt very distressed. So they went to the king and reported in detail what had happened.
Pamene antchito ena anaona zomwe zinachitikazo, anamva chisoni kwambiri ndipo anapita nakawuza bwana wawo zonse zimene zinachitika.
32 Then the king summoned the official [who had owed him several million dollars]. He said to him, ‘You wicked servant! I canceled that huge debt [that you owed me] because you begged me [to do so]
“Pamenepo bwanayo anayitana wantchitoyo nati, ‘Iwe wantchito woyipa mtima, ndinakukhululukira ngongole yako yonse chifukwa unandipempha.
33 You should have been merciful [and canceled your fellow official’s debt], just like I was merciful to you [and canceled your debt] [RHQ]!’
Kodi iwe sukanamuchitira chifundo wantchito mnzako monga momwe ine ndinakuchitira iwe?’
34 The king was very angry. He handed this official over to some jailers who would torture him severely until he paid all of the debt that he owed.”
Ndi mkwiyo, bwana wakeyo anamupereka kwa oyangʼanira ndende kuti amuzuze mpaka atabweza zonse zimene anakongola.
35 [Then Jesus continued by saying], “That is what my Father in heaven will do to you if you do not [feel merciful and] sincerely forgive a fellow believer [who sins against you].”
“Umu ndi mmene Atate anga akumwamba adzachitira ndi aliyense wa inu ngati simukhululukira mʼbale wanu ndi mtima wonse.”