< Matthew 16 >

1 [Some] Pharisees and Sadducees came to [Jesus] and asked him [to perform] a miracle that would prove [that] [had sent him].
Afarisi ndi Asaduki anabwera kwa Yesu ndi kumuyesa pomufunsa kuti awaonetse chizindikiro chochokera kumwamba.
2 He answered them, “[In this country], in the evening you say, ‘[It will be] good weather [tomorrow], because the sky is red.’
Iye anayankha kuti, “Kunja kukamada, inu mumati, kudzakhala nyengo yabwino popeza thambo ndi lofiira.
3 [Early] in the morning [you say], ‘It will be stormy weather today, because the sky is red, and dark clouds have formed.’ You understand how to predict [the weather by looking at the sky], but you cannot [seem to look at what is happening] now, [and by that] understand [what God is doing].
Ndipo mmawa mumati, ‘Lero kudzakhala mvula yamphepo popeza thambo ndi lofiira ndi mitambo ya mvula.’ Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a thambo koma simungathe kutanthauzira zizindikiro za nthawi.
4 [You] evil people have seen me [perform miracles] but you do not faithfully worship God [MET]. You want to see [me perform] a miracle [that would prove that God has sent me]. But [God] will [enable you to see] only one miracle. It will be [like] what happened [MET] to Jonah, [the prophet, who was inside a huge fish for three days and then came out of it to live again].” Then Jesus left them and sailed away, [along with us disciples].
Mʼbado woyipa ndi wachigololo umafuna chizindikiro chodabwitsa koma palibe ngakhale chimodzi chidzapatsidwa kupatula chizindikiro cha Yona.” Pamenepo Yesu anawasiya nachoka.
5 [We] forgot to take bread when [we] sailed to another edge of [the lake].
Koma atawoloka nyanja, ophunzira anayiwala kutenga buledi.
6 [Then] Jesus said to us, “Beware [that you do not accept] the yeast [MET] that the Pharisees and Sadducees [distribute].”
Yesu anawawuza kuti, “Chenjerani, khalani tcheru ndi yisiti wa Afarisi ndi Asaduki.”
7 Then, [not realizing that he was speaking figuratively], [we] said to one another, “[He must have said that] because we forgot to bring any bread!”
Iwo anakambirana pakati pawo za izi ndipo anati, “Ichi nʼchifukwa chakuti sitinatenge buledi aliyense.”
8 Because Jesus knew what [we were saying], he said [to us], “(I am disappointed that you are discussing among yourselves, [thinking] that [it was because] you did not bring any bread [that I talked about the yeast of the Pharisees and Sadducees]./Why are you discussing among yourselves thinking that it was because you did not bring any bread [that I talked about the yeast of the Pharisees and Sadducees]?) [RHQ] You believe only a little [what I am able to do for you].
Yesu atadziwa zokambirana zawo, anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukukambirana zakuti, ‘mulibe buledi?’ Inu achikhulupiriro chochepa.
9 (You should understand [that I can continue to do miracles to provide for what you need./] you not yet understand [that I can provide miraculously for you if you need food]?) [RHQ] Do you not remember that 5,000 [people ate when I multiplied the] five small loaves [and the two fish? And after everyone had enough to eat], you collected [twelve] baskets [of left-over pieces] [RHQ]!
Kodi inu simukumvetsetsabe? Kodi simukukumbukira za buledi musanu amene anadya anthu 5,000 ndi madengu amene munadzaza?
10 [Do you not remember] [RHQ] [that] 4,000 [people ate when I multiplied the] seven small loaves [and a few fish]? And [after everyone had enough to eat], you collected [seven] large baskets [of left-over pieces]
Kapena buledi musanu ndi muwiri amene anadya anthu 4,000, nanga ndi madengu angati amene munadzaza?
11 (You should have understood that I was not speaking about [real] bread [that contains yeast]./Why have you not understood that I was not speaking about [real] bread [that contains yeast?]) [RHQ] What I [was saying] was that you should [not accept what] the Pharisees and Sadducees [say, because it would affect you like] yeast [affects] [MET] [dough].”
Zitheka bwanji kuti inu simukumvetsetsa kuti Ine sindinkayankhula nanu za buledi? Koma inu chenjerani ndi yisiti wa Afarisi ndi Asaduki.”
12 Then we understood that he was not talking about the yeast that is [in] bread. Instead, [he was talking] about the [wrong] teaching of the Pharisees and Sadducees.
Kenaka iwo anazindikira kuti Iye samawawuza kuti achenjere ndi yisiti wa buledi koma ndi chiphunzitso cha Afarisi ndi Asaduki.
13 When Jesus came with [us] disciples to the region near Caesarea Philippi [town], he asked us, “Who do people say that I, the one who came from heaven, [really] am?”
Yesu atafika ku chigawo cha Kaisareya Filipo, Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Kodi anthu amati Mwana wa Munthu ndi ndani?”
14 We answered, “Some [people say that you are] John the Baptizer, [who has come back to life again]. Others say [that you are the prophet] Elijah, [who has returned from heaven as God promised]. [Still] others [say that you are the prophet] Jeremiah or one of the [other] prophets [who lived long ago, who has come back to life again].”
Iwo anayankha kuti, “Ena amati ndi Yohane Mʼbatizi; ena amati ndi Eliya; komanso ena amati Yeremiya kapena mmodzi wa aneneri.”
15 Jesus said to us, “[What about] you? Who do you say that I am?”
Iye anafunsa kuti, “Nanga inuyo mumati ndine yani?”
16 Simon Peter said to him, “You are the Messiah! You are the Son of the all-powerful God.”
Simoni Petro anayankha kuti, “Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.”
17 Then Jesus said to him, “Simon, son of Jonah, [God] is pleased with you. What you just said was not [SYN] revealed to you by any human. Instead, [it was] my Father [who lives] in heaven [who revealed this to you].
Yesu anati kwa iye, “Ndiwe wodala Simoni mwana wa Yona, popeza si munthu amene anakuwululira izi koma Atate anga akumwamba.
18 I will also tell you this: You are Peter, [which means rock]. [You are like] a rock. What you [and your fellow apostles teach] (OR, [what] you [do]) [will be like a foundation on which I] will create congregations of people who [believe in] me. And the demons [PRS], [who live] where the dead people who lived evil lives are, will not be able to [come and] prevent [MET] [me from doing] that.” (Hadēs g86)
Ndipo Ine ndikuwuza iwe kuti ndiwe Petro ndipo pa thanthwe ili Ine ndidzamangapo mpingo wanga ndipo makomo a ku gehena sadzawugonjetsa. (Hadēs g86)
19 [Then, speaking to all of us, he said], “I will enable you [(pl)] to have authority [MTY] over the groups of people over whose lives [God] rules. Whatever you forbid regarding those people [MTY], it will have been forbidden by God. Whatever you permit [MET] regarding them, it will have been permitted by God.”
Ine ndidzakupatsa makiyi a Ufumu wakumwamba, ndipo chilichonse chimene iwe udzachimanga pansi pano chidzamangidwanso kumwamba.”
20 Then Jesus warned [us] disciples strongly not to tell anyone [at that time] that he is the Messiah.
Pamenepo Iye anachenjeza ophunzira ake kuti asawuze wina aliyense kuti ndi Khristu.
21 From that time Jesus began to teach [us] disciples that it was necessary for him to go to Jerusalem [city]. There the ruling elders, the chief priests, and the men who taught the [Jewish] laws would cause him to suffer and (be killed/die). Then on the third day [after that], he would become alive again.
Kuyambira nthawi imeneyo Yesu anayamba kuwafotokozera ophunzira ake kuti Iye ayenera kupita ku Yerusalemu ndi kukazunzidwa kwambiri mʼmanja mwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo kuti ayenera kuphedwa, ndi kuti tsiku lachitatu adzaukitsidwa.
22 [Because Peter assumed that the Messiah would not suffer and die], he took Jesus aside and began to rebuke him [for talking about suffering and dying]. He said, “Lord, may [God] never permit that to happen to you! That must certainly not happen!”
Petro anamutengera Iye pambali nayamba kumudzudzula kuti, “Dzichitireni chifundo Ambuye, sizingachitike kwa Inu ayi.”
23 Then Jesus turned [to look at] Peter, and he said to him, “Stop talking to me [like that] [MTY]! [Stop saying what] Satan [MET] [would say, and stop] trying to prevent [from happening what God has planned]! You are a hindrance to me, because you are not thinking like God thinks. Instead, [you are thinking] like people [think]!”
Yesu anatembenuka nati kwa Petro, “Choka pamaso panga Satana! Iwe ndi chokhumudwitsa kwa Ine; iwe suganizira zinthu za Mulungu koma zinthu za anthu.”
24 Then Jesus said to [us] disciples, “If any one [of you] wants to be my disciple, you must not do [only] what you yourself want [to do]. [You] must be willing to [let people hurt you and disgrace you. That is like what they do to criminals whom they force to] carry a cross [MET] [to the place where the criminals will be executed. That is what anyone who wants to] be my disciple [must do].
Pamenepo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Ngati wina aliyense abwera pambuyo panga ayenera kudzikana ndi kutenga mtanda wake ndi kunditsata Ine.
25 [You must do that], because those who try to save their lives [by denying that they belong to me when people want to kill them for believing in me] will not live [eternally], but those who are killed [because of being my disciples] will live [with God eternally].
Pakuti aliyense amene afuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya koma aliyense amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupeza.
26 People [might] get everything [they want] in this world, but ([if they do not become my disciples], they would really be gaining nothing [because] they would not get eternal life!/what would they gain [if they do not become my disciples and thus] do not get eternal life?) [RHQ] (There is absolutely nothing that people can give [to God] that would enable them to gain eternal life./What can people give [to God] that could enable them to gain eternal life?) [MTY, RHQ]
Kodi munthu adzapindula chiyani ngati atapeza zonse za dziko lapansi nataya moyo wake? Kapena munthu angapereke chiyani chosinthana ndi moyo wake?
27 [Listen carefully: I], the one who came from heaven, [will leave this earth, but] I will return, and the angels of heaven will accompany me. At that time I will have the glorious [radiance] that my Father has, and I will reward everyone according to what they did [when they were living on earth].
Pakuti Mwana wa Munthu adzabwera mu ulemerero wa Atate ake ndi angelo ake ndipo pamenepo Iye adzapereka mphotho kwa munthu mofanana ndi zimene anachita.
28 Listen carefully! Some of you who are here now will see [me], the one who came from heaven, when I return to rule. You will see this before you die!”
“Ine ndikuwuzani inu choonadi, ena amene akuyimirira pano sadzalawa imfa asanaone Mwana wa Munthu akudza mu ufumu.”

< Matthew 16 >