< Mark 11 >

1 When they came near to Jerusalem, they came to Bethphage and Bethany [villages] near Olive [Tree] Hill. Then Jesus [summoned] two of his disciples.
Atayandikira ku Yerusalemu, anafika ku Betifage ndi Betaniya ku phiri la Olivi. Yesu anatuma awiri a ophunzira ake
2 He said to them, “Go to that village just ahead of you. As soon as you enter it, you will see a donkey that no one has ever ridden, that has been tied {people have tied} up. Untie it, and then bring it [to me].
nati kwa iwo, “Pitani ku mudzi uli patsogolo panu, ndipo mukamakalowa, mukapeza mwana wabulu atamangiriridwa pamenepo, amene wina aliyense sanakwerepo. Kamumasuleni ndi kubwera naye kuno.
3 If anyone says to you, ‘Why are you doing that?’, say, [‘Jesus], our Lord, needs [to use] it. He will send it back here [with someone] as soon as [he no longer needs it].’”
Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Mukuchita zimenezi chifukwa chiyani?’ Kamuwuzeni kuti, ‘Ambuye akumufuna ndipo akamutumiza kuno msanga.’”
4 So [the two disciples] went and they found the young donkey. It was tied close to the door [of a house], which was beside the street. Then they untied it.
Anapita ndipo anakapeza mwana wabulu ali kunja mu msewu waukulu atamumangirira pa chipata. Pamene anamumasula,
5 Some of the [people who were there] said to them, “Why are you untying the donkey?”
anthu ena amene anayima pomwepo anafunsa kuti, “Mukuchita chiyani, kumasula mwana wabuluyo?”
6 They told them what Jesus had said. So the people permitted them [to take the donkey].
Iwo anayankha monga mmene Yesu anawawuzira, ndipo anthu aja anawalola kuti apite.
7 They brought the donkey to Jesus. [The disciples] put some of their clothes on it [in order to make something for him to sit on].
Atafika naye mwana wabulu kwa Yesu, nayika mikanjo yawo pa buluyo, Iye anakwerapo.
8 Many people spread their cloaks on the road [to honor him as a king]. Others, [in order to honor him], spread along the road branches that they cut from [palm trees] in the fields [beside the road].
Anthu ambiri anayala mikanjo yawo pa msewu, pamene ena anayala nthambi zomwe anadula mʼminda.
9 The people who were going in front of him and behind him were all shouting [things like], “Praise God!” “May God bless this one who comes (with his authority/as his representative) [MTY].”
Amene anatsogola ndi iwo amene ankatsatira ankafuwula kuti, “Hosana! “Odala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye!”
10 “May you be blessed {May [God] bless you} when you rule [like] our ancestor [King] David ruled!” “Praise God who is in the highest heaven!”
“Odala ndi ufumu umene ukubwera wa abambo athu Davide!” “Hosana Mmwambamwamba!”
11 He entered Jerusalem [with them], and then he went into the Temple [courtyard]. After he looked around at everything [there], he left [the city] because it was already late [in the afternoon]. He returned to Bethany with the twelve [disciples and slept there].
Yesu analowa mu Yerusalemu napita ku Nyumba ya Mulungu. Anayangʼana zonse, koma popeza kuti nthawi inali itapita, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.
12 The next day, as Jesus and his disciples were leaving Bethany, Jesus was hungry.
Mmawa mwake pamene amachoka ku Betaniya, Yesu anamva njala.
13 He saw from a distance a fig tree with all its leaves, so he went [to it] to see if he could find any [figs] on it. But when he came to it, he found only leaves on it. This was because it was not yet time when [normal fig trees have ripe] figs.
Ataonera patali mtengo wamkuyu uli ndi masamba, anapita kuti akaone ngati unali ndi chipatso chilichonse. Atafika, sanapezemo kanthu koma masamba, chifukwa sinali nthawi ya nkhuyu.
14 [But to illustrate how God would punish the nation of Israel, ] he said to the tree, “No one shall ever eat from you again [because you will no longer bear figs].” The disciples heard what he said. (aiōn g165)
Ndipo Iye anati kwa mtengo, “Palibe amene adzadyenso chipatso kuchokera kwa iwe.” Ndipo ophunzira ake anamva Iye akunena izi. (aiōn g165)
15 Jesus and his disciples went [back] to Jerusalem. He entered the Temple [courtyard. He saw people] who were selling and buying [animals for sacrifices. They were spoiling the place of worship]. He chased those people [from the Temple courtyard.] He also overturned the tables of those who were giving Temple tax money in exchange for Roman coins. He overturned the seats of the men who were selling doves [for sacrifices],
Atafika ku Yerusalemu, Yesu analowa mʼbwalo lakunja la Nyumba ya Mulungu ndipo anayamba kupirikitsa anthu amene amagula ndi kugulitsa mʼmenemo. Anagubuduza matebulo a osintha ndalama ndi mipando ya ogulitsa nkhunda,
16 and he would not allow anyone who was carrying anything [to sell] to go through the Temple [area].
ndipo Iye sanalole aliyense kugulitsa malonda mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu.
17 Then as he taught those people, he said to them, “It is written {[One of the prophets] wrote} [in the Scriptures that God said], ‘[I want] my house to be called {[people] to call my house} a house where [people from] all nations may pray’, but you bandits have made it [like] a cave where you can hide! ([You know that!/Do you not know that]?) [RHQ]”
Ndipo pamene ankawaphunzitsa, Iye anati, “Kodi sikunalembedwe kuti, ‘Nyumba yanga idzatchedwa Nyumba ya mapemphero kwa anthu a mitundu yonse?’ Koma inu mwayisandutsa ‘phanga la achifwamba.’”
18 The chief priests and the men who taught the [Jewish] laws [later] heard [about what he had done]. So they planned how they might kill him, [but they knew that it would be difficult], because they realized that the crowd was amazed at what he was teaching and they feared [that the people would soon decide that Jesus had more authority over the Temple than they did] (OR, [feared what the people would do if they tried to arrest Jesus]).
Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo anamva izi ndipo anayamba kufuna njira yoti amuphere Iye, pakuti amamuopa, chifukwa gulu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.
19 That evening, [Jesus and his disciples] left the city [and again slept in Bethany].
Pofika madzulo, iwo anatuluka mu mzindamo.
20 [The next] morning, while they were going along [the road toward Jerusalem, they saw that the fig tree that Jesus had cursed] had withered completely.
Mmamawa, pamene ankayenda, anaona mtengo wamkuyu uja utafota kuyambira ku mizu.
21 Peter remembered [what Jesus had said to the fig tree] and he exclaimed to Jesus, “Teacher, look! The fig tree that you cursed has withered!”
Petro anakumbukira nati kwa Yesu, “Aphunzitsi, taonani! Mtengo wamkuyu munawutemberera uja wafota!”
22 Jesus replied, “[You should not be surprised that God did what I asked]! You must trust that God [will do whatever you ask him to do]!
Yesu anayankha kuti, “Khalani ndi chikhulupiriro mwa Mulungu.
23 [Also] note this: If anyone says to this hill, ‘Be raised up {Rise up} and then be thrown {throw yourself} into the lake!’ and if he does not doubt [that what he asks for will happen], that is, if he believes that what he asks for will happen, [God] will do it for him.
Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati wina aliyense angalamule phiri ili kuti, ‘Pita, kadziponye mʼnyanja,’ ndipo wosakayika mu mtima mwake koma kukhulupirira kuti chimene akunena chidzachitika, chidzachitikadi kwa iyeyo.
24 So I tell you, whenever you ask [God] for something when you pray, believe that you will receive it, and, [if you do, God] will do it [for you].
Nʼchifukwa chake ndikukuwuzani kuti chilichonse chimene mupempha mʼpemphero, khulupirirani kuti mwalandira, ndipo chidzakhala chanu.
25 Now, I [tell you this also]: Whenever you are praying, if you have a grudge against people [because they have harmed you], forgive them, in order that your Father in heaven will [likewise] forgive your sins.”
Pamene muyimirira kupemphera, ngati muli ndi chifukwa ndi wina, mukhululukireni, kuti Atate anu akumwamba akukhululukireni machimo anu.”
(Koma ngati simukhululukirana, ngakhale Atate anu akumwamba sadzakhululukira machimo anu).
27 Jesus and his disciples arrived in the Temple [courtyard] in Jerusalem again. While Jesus was walking [there, a group consisting of] chief priests, [some] men who taught the [Jewish] laws, and elders came to him and they said to him,
Iwo anafikanso ku Yerusalemu, ndipo pamene Yesu amayenda mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
28 “By what authority are you doing these things? Who authorized you to do things [like those you did here yesterday]?”
Iwo anafunsa kuti, “Mukuchita izi ndi ulamuliro wanji? Ndipo anakupatsani ulamuliro umenewu ndi ndani?”
29 Jesus said to them, “I will ask you one question. If you answer me, I will tell you who authorized me to do those things.
Yesu anayankha kuti, “Ndikufunsani funso limodzi. Mundiyankhe, ndipo ndikuwuzani ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira izi.
30 Did God [MTY] or people [authorize] John to baptize [those who came to him]?”
Ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena kwa anthu? Ndiwuzeni.”
31 They debated among themselves [as to what they should answer]. They [said to each other], “If we say that it was God [who authorized] him, he will say to us, ‘Therefore, (you should have believed what John said!/why did you not believe what John said?) [RHQ]’
Iwo anakambirana pakati pawo ndipo anati, “Tikati, ‘Wochokera kumwamba,’ atifunsa kuti, ‘Nanga nʼchifukwa chiyani simunamukhulupirire?’
32 On the other hand, if we say that it was people [who authorized John, then what will happen to us]?” They were afraid [to say that about where John got his authority, because they knew that] the people [would be very angry with them. They knew that] all the people truly believed that John was a prophet [whom God had sent].
Koma ife tikati, ‘Wochokera kwa anthu.’” (Amaopa anthu, pakuti aliyense amakhulupirira kuti Yohane analidi mneneri).
33 So they answered Jesus, “We do not know [where John got his authority].” Then Jesus said to them, “[Because you did not answer my question, I] will not tell you who authorized me to do those things [here yesterday].”
Ndipo anamuyankha Yesu kuti, “Sitikudziwa.” Yesu anati, “Nanenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji ndichitira zimenezi.”

< Mark 11 >