< Luke 8 >
1 Soon after that, Jesus went, along with his twelve [disciples], through various cities and villages. As they went, he was telling people the good message about how God wants (to have complete control/to rule) [MET] [over their lives].
Zitatha izi, Yesu anayendayenda kuchoka mzinda wina kupita wina ndiponso mudzi wina kupita wina, akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu. Ophunzira ake khumi ndi awiri aja anali naye,
2 Some women from whom he had expelled evil spirits and healed of diseases also [went with him]. These included Mary, the woman from Magdala [village], from whom [he had expelled] seven evil spirits;
komanso akazi ena amene anachiritsidwa ku mizimu yoyipa ndi matenda: Mariya, wotchedwa Magadalena, amene mwa iye munatuluka ziwanda zisanu ndi ziwiri;
3 Joanna, the wife of Chuza, who was one of [King] Herod [Antipas’] officials; Susanna; and many others. They were providing some of their own funds [to help Jesus and his disciples].
Yohana mkazi wa Kuza, woyangʼanira mʼnyumba ya Herode; Suzana; ndi ena ambiri analinso. Akazi awa ankawathandiza ndi chuma chawo.
4 A large crowd of people came to Jesus from many towns. Then he told them this parable:
Anthu ambiri ankasonkhana, ndipo pamene anthu ankabwera kwa Yesu kuchokera ku midzi, Iye anawawuza fanizo ili,
5 “A man went out [to his field] to sow [some] seeds. As he was scattering them over the soil, some [of the seeds] fell on the path. Then [people] walked on those seeds, and birds ate them.
“Mlimi anapita kukafesa mbewu zake. Akufesa mbewuzo, zina zinagwa mʼmbali mwa njira; zinapondedwa, ndipo mbalame zamlengalenga zinadya.
6 Some [of the seeds] fell on rock [on which there was a thin layer of] moist [soil]. As soon as the seeds grew, the plants dried up because they had no moisture.
Zina zinagwa pa thanthwe, ndipo pamene zinamera, zinafota chifukwa panalibe chinyezi.
7 Some [of the seeds] fell on [ground that contained roots of] thorny [weeds]. The thorny weeds grew [together] with the young plants, and [they] crowded out [those plants].
Mbewu zina zinagwera pakati pa minga, zinakulira pamodzi ndi mingazo ndipo zinalepheretsa mmerawo kukula.
8 But some of the seeds fell on good soil and grew [well]. [Each seed later] produced 100 [grains].” Then Jesus called out to them, “If you want to understand [MTY] this, you must consider [carefully what I have just said]!”
Mbewu zina zinagwera pa nthaka yabwino. Zinamera ndipo zinabala mowirikiza 100 kuposa zimene zinafesedwa zija.” Atanena izi, anafuwula kuti, “Amene ali ndi makutu, amve.”
9 Jesus’ disciples [later] asked him about the meaning of the parable [he had just told].
Ophunzira ake anamufunsa tanthauzo lake la fanizolo.
10 He said, “God is revealing to you what he did not reveal before, about [how he wants to] rule [MET] [over people’s lives]. But when I am telling other people about [these things, I tell them] only in parables. The result will be [like a prophet predicted long ago]: They will see [what I am doing], but will not perceive [what it means]. They will hear [what I am saying], but will not understand [it].
Iye anati, “Kudziwa zinsinsi za ufumu wa Mulungu kwapatsidwa kwa inu, koma kwa ena ndimawayankhula mʼmafanizo kuti, “ngakhale akuona, asapenye; ngakhale akumva, asazindikire.”
11 So this is the meaning of that parable: The seeds [represent] God’s message.
“Tanthauzo la fanizoli ndi ili: Mbewu ndi mawu a Mulungu.
12 [Some people are like] the path on which some of [the seeds fell]. When these people hear God’s message, the devil comes and causes them to forget what they have heard. As a result, they do not believe it, and will not be saved {[God] will not save them}.
Mbewu za mʼmbali mwa njira ndi anthu amene amamva mawu, ndipo kenaka mdierekezi amabwera ndi kuchotsa mawuwo mʼmitima mwawo kuti asakhulupirire ndi kupulumutsidwa.
13 [Some people are like] the [soil with] rock [underneath]. When they hear [God’s] message, they accept it joyfully. [But because it does not penetrate deeply] [MET] [into their inner beings], they believe it for [only] a [short] time. [They are like the plants that] did not have [deep] roots. When difficult things happen to them, they stop believing [God’s message].
Mbewu za pa thanthwe ndi anthu amene amalandira mawu mwachimwemwe pamene akumva, koma mawuwo sazika mizu. Iwo amakhulupirira kwa kanthawi, koma pa nthawi ya mayesero, amagwa.
14 [Some people are like] the [soil that had roots of] thorny [weeds] in it. They are people who accept [God’s message], but later on they worry about things, and try to become rich, and enjoy [things that give them] a lot of pleasure. So they do not become [spiritually] mature.
Mbewu zimene zinagwa pakati pa minga zikuyimira anthu amene amamva mawu, koma akamayenda mʼnjira zawo amatsamwitsidwa ndi zodandaulitsa za moyo uno, chuma ndi zosangalatsa, ndipo iwo samakhwima.
15 But [some people are like] the good soil. They hear [God’s] message and accept it. They [become] good, honest people, and they continue doing things [that please God] [MET].”
Koma mbewu za pa nthaka yabwino zikuyimira anthu amene ali ndi mtima woona ndi wabwino, amene amamva mawu nawasunga, ndipo amalimbikira mpaka amabala zipatso.
16 “After people light a lamp, they do not cover it with a basket or put it under a bed. Instead, they put it on a lampstand, so that those who enter [their house] can see [things from] its light [MET]. [Similarly, you must tell God’s truth to others so that they can know what I can do for them].
“Palibe amayatsa nyale ndi kuyibisa mu mtsuko kapena kuyika pansi pa bedi. Koma mʼmalo mwake, amayika pa choyikapo chake, kuti anthu olowamo aone kuwala.
17 [God wants to] make clear all [of his truth] that was not evident previously. [He intends] that all of [the truth] that [he] had not revealed before be told openly {that [his people] openly tell [others] all [of the truth] that [he] has not revealed before}.
Pakuti palibe kanthu kobisika kamene sikadzawululika, ndipo palibe kanthu kophimbika kamene sikadzadziwika kapena kuonetsedwa poyera.
18 So listen carefully [to what I tell you], because [God] will enable those who accept [my truth] to [understand even] more. But [God] will cause those who do not accept [my truth] to not understand even [the little] that they think they have [understood].”
Choncho ganizirani mozama. Iye amene ali nazo adzapatsidwa zambiri, iye amene alibe, ngakhale chimene akuganiza kuti ali nacho adzalandidwa.”
19 [One day Jesus’] mother and his [younger] brothers came to see him, but they could not get near him because there was a large crowd [around him in the house].
Tsopano amayi ndi abale a Yesu anabwera kudzamuona Iye, koma analephera kuti afike pafupi ndi Iye chifukwa cha gulu la anthu.
20 Someone told him, “Your mother and your [younger] brothers are standing outside, wanting to see you.”
Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunja, akufuna kukuonani.”
21 He replied, “Those who hear God’s message and obey it are [as dear to me] [MET] as my mother and my brothers.”
Yesu anayankha kuti, “Amayi ndi abale anga ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kumachita zimene mawuwo akunena.”
22 One day Jesus got into a boat with his disciples. He said to them, “Let’s go [around to] the other side of the lake.” So they started to go.
Tsiku lina Yesu anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tiwolokere tsidya lina la nyanja.” Ndipo analowa mʼbwato nanyamuka.
23 As they were sailing, he fell asleep. A big windstorm struck the lake. Soon the boat was filling with water, and they were in danger.
Akuwoloka, Iye anagona tulo. Namondwe wamkulu anayamba pa nyanja, ndipo bwatolo linayamba kudzaza ndi madzi ndipo anali pa chiopsezo chachikulu.
24 Jesus’ disciples woke him up. They said [to him], “Master! Master! We [(inc)] are going to drown!” He got up and rebuked the wind and told the waves to be calm. The wind [immediately] stopped blowing and the waves calmed down. [The lake] became calm.
Ophunzira anapita ndi kukamudzutsa Iye, nati, “Ambuye, Ambuye, ife tikumira!” Anadzuka ndipo anadzudzula mphepo ndi madzi owindukawo. Namondwe anasiya, ndipo panali bata.
25 He said to them, “(I [am disappointed that] you did not trust me [to help you]!/Why did you not trust me [to help you]?)” [RHQ] They were afraid. They were also amazed. They said to each other, “(What kind of man is this?/This man is not like ordinary men!) [RHQ] He [not only commands people, but] when he commands the wind and the water, they also obey him!”
Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Chikhulupiriro chanu chili kuti?” Koma pogwidwa ndi mantha ndi kudabwa anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Uyu ndi ndani? Iye alamulira ngakhale mphepo ndi madzi, ndipo zimumvera Iye.”
26 Jesus and his disciples arrived at the region near Gerasa, a [town] which [was on the eastern] side of Lake [Galilee].
Iwo anawolokera ku chigawo cha Gerasa chimene chili tsidya lina la nyanja kuchokera ku Galileya.
27 [There was] a man [in that region] in whom demons lived. [He was] from the town [of Gerasa]. (OR, [In that area there was] a man [from that town] whom demons controlled.) For a long time he had not worn clothes. He did not live in a house. Instead, he lived in burial caves.
Yesu ataponda pa mtunda, anakumana ndi munthu wogwidwa ndi ziwanda wochokera mu mzindawo. Kwa nthawi yayitali munthuyu sanavale zovala kapena kukhala mʼnyumba, koma amakhala ku manda.
28 Many times [demons] attacked him. He was guarded {[People] tried to guard him} [so that he would not injure others]. Chains were fastened {They fastened chains} on his hands and shackles on his feet, but he would break the chains and shackles. Then he would be sent away by the demons {the demons would send him away} to some desolate area. When Jesus stepped out of the boat onto the shore, the man saw him. He [ran to Jesus] and prostrated himself before him. Then Jesus commanded, “You evil spirit, come out of that man!” But it [did not leave immediately. Instead, it] caused the man to shout very loudly, “Jesus, Son of the great God in heaven, since we [(inc)] have nothing in common, [leave me alone] [RHQ]! I beg you, do not torture me [now]!”
Iye ataona Yesu, anakuwa nagwa pa mapazi ake akufuwula kwambiri kuti, “Mukufuna chiyani ndi ine, Yesu Mwana wa Mulungu Wammwambamwamba? Ndikupemphani Inu, musandizunze ine!”
Pakuti Yesu analamula mzimu woyipawo kuti utuluke mwa munthuyo. Kawirikawiri umamugwira iye, ndipo ngakhale anali womangidwa ndi unyolo dzanja ndi mwendo ndi kuti ankamuyangʼanira, koma amadula maunyolo akewo ndipo ziwanda zimamutengera kumalo a yekha.
30 [In order to expel the demon more easily], Jesus asked [the demon], “What is your [(sg)] name?” He replied, “My name is Crowd/Mob.” [He said that] because many demons had entered that man.
Yesu anamufunsa kuti, “Dzina lako ndani?” Iye anayankha kuti, “Legiyo,” chifukwa ziwanda zambiri zinalowa mwa iye.
31 [The demons] kept begging [Jesus] that he would not command them to go into the deep place [where God punishes demons]. (Abyssos )
Ndipo ziwandazo zimamupempha mobwerezabwereza kuti asazitumize ku dzenje la mdima. (Abyssos )
32 There was a large herd of pigs (grazing/rooting for food) on the hillside. The demons begged Jesus that he allow them to enter the pigs. So he did.
Gulu lalikulu la nkhumba limadya pamenepo mʼmbali mwa phiri. Ziwandazo zinamupempha Yesu kuti azilole kuti zikalowe mu nkhumbazo ndipo Iye anazilola.
33 The demons left the man and entered the pigs. Then the herd [of pigs] rushed down the steep bank into the lake and drowned.
Ziwanda zija zitatuluka mwa munthuyo, zinakalowa mwa nkhumbazo, ndipo gulu lonselo linathamangira ku mtsetse ndi kukalowa mʼnyanja ndi kumira.
34 When the men who were taking care of the pigs saw what happened, they ran! They told people inside the town and outside the town what had happened.
Oweta nkhumbazo ataona zimene zinachitikazo, anathamanga ndi kukanena izi mu mzinda ndi ku madera a ku midzi.
35 So people went out to see what had happened. When they came to where Jesus was, they saw that the man from whom Jesus had [expelled] the demons was sitting at the feet of Jesus, [listening to him]. He had clothes on, and his mind was normal again. Then those people became afraid [because they thought that Jesus would destroy more of their property] (OR, [because they realized that he must be very powerful]).
Ndipo anthu anapita kukaona zimene zinachitika. Atafika kwa Yesu, anapeza munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja atakhala pa mapazi a Yesu, atavala ndipo ali ndi nzeru zake; ndipo iwo anachita mantha.
36 The people who had seen what happened told those [who had just arrived] how [Jesus] had healed the man whom demons were controlling [before].
Amene anaona izi anawuza anthu mmene munthu wogwidwa ndi ziwandayo anachiritsidwira.
37 Then [those people and] many other people [HYP] from the area near Gerasa asked Jesus to leave their area. They were very afraid of [what else Jesus would do to them]. So [Jesus and the disciples] got into the boat to go back across the lake.
Kenaka anthu onse a ku chigawo cha Gerasa anamupempha Yesu kuti achoke kwa iwo, chifukwa anadzazidwa ndi mantha. Choncho Iye analowa mʼbwato nachoka.
38 The man from whom he had [expelled] the demons begged him saying, “[Please], let me go with you!” But [Jesus refused. Instead], he said to him,
Munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja, anapempha Yesu kuti apite nawo, koma Yesu anamubweza nati,
39 “[No], go home and tell people how much God has done for you!” Then he sent him away. So the man went away and told people throughout the nearby town how much Jesus had done for him.
“Bwerera kwanu kafotokoze zimene Mulungu wakuchitira.” Ndipo munthuyo anachoka ndi kukanena ku mzinda wonsewo zimene Yesu anamuchitira iye.
40 When [Jesus and the disciples] returned [to Capernaum], a crowd of people who had been waiting for him welcomed him.
Yesu atabwerera, gulu lalikulu la anthu linamulandira, chifukwa onse ankamuyembekezera.
41 Just then a man named Jairus, who was one of the leaders (of the synagogue/of the Jewish meeting place) [there], came near and prostrated himself at Jesus’ feet. He pleaded with Jesus, “Please come to my house [and heal my daughter],
Nthawi yomweyo munthu wotchedwa Yairo, woweruza wa mu sunagoge, anabwera ndi kugwa pa mapazi a Yesu, namupempha Iye kuti apite ku nyumba kwake,
42 my only daughter, who is about twelve years old, because she is dying!” As Jesus went with him, many people crowded close to Jesus.
chifukwa mwana wake yekhayo wamkazi, kamtsikana ka zaka khumi ndi ziwiri, kanali pafupi kufa. Pamene Yesu ankapita gulu la anthu linkamupanikiza.
43 Then a woman came near. She had been suffering from constant [vaginal] [EUP] bleeding for twelve years, but she could not be healed by anyone {no one could heal her}.
Ndipo pomwepo panali mayi wina amene ankataya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri, koma panalibe wina akanamuchiritsa.
44 She came behind [Jesus] and touched the edge of his robe [in order to be healed]. At once her bleeding stopped.
Iye anafika kumbuyo kwake ndi kukhudza mothera mwa chovala chake, ndipo nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka.
45 Jesus said, “Who touched me?” When everyone said that they had not touched him, Peter said, “Lord, there is a large crowd of people around you [(sg)] and crowding against you, [so any one of them might have touched you]!”
Yesu anafunsa kuti, “Wandikhudza ndani?” Onse atakana, Petro anati, “Anthu akukupanikizani ndi kukukankhani.”
46 But Jesus said, “[I know that] someone [deliberately] touched me, [because] my power has healed someone [who touched me].”
Koma Yesu anati, “Wina wandikhudza; ndikudziwa chifukwa mphamvu yachoka mwa Ine.”
47 When the woman realized that she could not prevent [Jesus] (OR, [people]) from knowing that [she was healed], her body began to shake. [She was afraid that because she had disobeyed the law that a woman with such a condition should not touch others, Jesus might scold her for doing that]. She prostrated herself before Jesus. As the other people were listening, she told why she had touched him and how she had been healed immediately.
Ndipo mayiyo podziwa kuti sanathe kuchoka wosadziwika, anabwera akunjenjemera ndipo anagwa pa mapazi a Yesu. Pamaso pa anthu onse, anafotokoza chifukwa chimene anamukhudzira Iye ndi mmene iye anachiritsidwira nthawi yomweyo.
48 [Jesus] said to her, “(Ma’am/My dear woman), because you believed [PRS] [that I could heal you, I] have healed you. Go [from here, and may you experience God’s] peace [within you].”
Kenaka anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere.”
49 While he was still talking [to her], a man from Jairus’ house came and said to Jairus, “Your daughter has died. So (it is useless that you bother the teacher any longer [by urging him to go to your house]!/why do you bother the teacher any longer [by urging him to go to your house]?) [RHQ]”
Pamene Yesu ankayankhulabe, munthu wina anabwera kuchokera ku nyumba ya Yairo, woweruza wa ku sunagoge uja. Iye anati, “Mwana wanu wa mkazi wamwalira, musawavutitsenso Aphunzitsiwa.”
50 But when Jesus heard that, he said to Jairus, “Do not think that there is nothing more that can be done. Just believe that [I can help her. If you(sg) do that], she will live again.”
Atamva zimenezi, Yesu anati kwa Yairo, “Usachite mantha, ingokhulupirira basi ndipo adzachiritsidwa.”
51 When they arrived outside Jairus’ house, Jesus allowed only Peter, John, James, and the girl’s mother and father to go in Jairus’ house with him.
Iye atafika ku nyumba ya Yairo, sanalole wina aliyense kulowa kupatula Petro, Yohane, ndi Yakobo ndi abambo ndi amayi a mwanayo.
52 All the people [there] were crying and beating their chests [to show that they were sad]. But, [knowing that he would cause the girl to live again], he said to them, “Stop crying! She is not dead! She is [just] sleeping [MET]!”
Pa nthawiyi nʼkuti anthu onse akubuma ndi kumulirira iye. Yesu anati, “Lekani kulira, sanafe koma wagona tulo.”
53 The people laughed at him, because they knew that [the girl] was dead.
Iwo anamuseka podziwa kuti anali atamwalira.
54 But [Jesus] took hold of her hand and called to her, saying, “Child, get up!”
Koma Iye anamugwira dzanja lake ndipo anati, “Mwana wanga, dzuka!”
55 At once her spirit returned [to her body] and she got up. Jesus immediately said, “Give her something to eat!”
Mzimu wake unabwerera, ndipo nthawi yomweyo anayimirira. Kenaka Yesu anawawuza kuti amupatse chakudya.
56 Her parents were amazed, but Jesus told them not to tell anyone [else yet] what had happened.
Makolo ake anadabwa, koma Iye anawalamulira kuti asawuze wina aliyense zimene zinachitikazo.