< Luke 4 >
1 As Jesus left the Jordan [River valley], the Holy Spirit was completely controlling him.
Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu,
2 For 40 days the Spirit led him around in the desolate area. During that time Jesus was being tempted by the devil {the devil was tempting him}, and Jesus did not eat anything. When that time ended, he was [very] hungry.
kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.
3 Then the devil said to Jesus, “Because you [claim that you] ([have a relationship with] God as a son [has with his father] [MET]/are the man who is both God and man), [prove it by] telling these stones to become bread [so that you can eat them]!”
Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”
4 Jesus replied, “[No, I will not change stones into bread, because it is written] {[Moses] wrote} [in the Scriptures] that [eating] food sustains people physically, but it does not [sustain them spiritually. They also need food for their spirits].”
Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’”
5 Then the devil took him on top of [a high mountain] and showed him in an instant all the nations in the world.
Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi.
6 Then he said to [Jesus], “I will give you the authority [to rule] all these areas and will make you famous. [I can do this] because [God] has permitted me [to control these areas], and I can allow anyone I desire to rule them!
Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna.
7 So if you worship me, I will [let] you [rule] them all!”
Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”
8 But Jesus replied, “[No, I] will not [worship you, because] it is written {[the Psalmist] wrote} [in the Scriptures], ‘It is the Lord, your God, whom you must worship, and you must serve only him!’”
Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’”
9 Then the devil took [Jesus] to Jerusalem. He set him on the highest part of the Temple and said to him, “Because you [claim that you] ([have a relationship with God as a son has with his father] [MET]/are the man who is both God and man), [prove it by] jumping down from here.
Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano.
10 [You will not be hurt], because it is written {the [Psalmist] wrote} [in the Scriptures], ‘God will command his angels to protect you [(sg)].
Pakuti kwalembedwa, “Adzalamulira angelo ake za iwe kuti akutchinjirize mosamala;
11 They will lift you up with their hands [when you are falling], so that [you will not get hurt]. You will not [even] strike your foot on a stone.’”
ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”
12 But Jesus replied, “[No, I] will not [do that, because] it is written {[Moses] wrote} [in the Scriptures]: ‘Do not try to test the Lord your God [to see if he will prevent something bad from happening to you when you do something foolish]’.”
Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’”
13 Then, after the devil had finished trying to tempt [Jesus] in many ways, he left him. He wanted to try to tempt him later at an appropriate time.
Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.
14 As the Spirit empowered him, Jesus returned to Galilee [district. People] throughout all that region heard about what he [was doing].
Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi.
15 He taught [people] in their (synagogues/meeting places). [As a result], he was praised by everyone {everyone praised him}.
Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.
16 Then [Jesus] went to Nazareth, [the town] where he grew up. (On the Sabbath/On the Jewish rest day) he went (to the synagogue/to the Jewish meeting place), as he usually did. He stood up [to indicate that he wanted] to read [Scriptures] to them.
Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba.
17 A scroll containing [the words] that the prophet Isaiah [had written] was given to him {[Someone] gave to him a scroll containing [the words] that the prophet Isaiah [had written]}. He opened the scroll and found the place from which he [wanted to] read. [He read these words]:
Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,
18 The Spirit (of the Lord/of God) is upon me. He has appointed [MTY] me to declare God’s good news to the poor. He has sent me [here] to proclaim that God will deliver those whom [Satan] has captured, and he will [enable me to] enable those who are blind to see. He will enable me to free people who have been oppressed {whom [others] have oppressed}.
“Mzimu wa Ambuye ali pa Ine; chifukwa wandidzoza kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka. Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe ndi kwa osaona kuti apenyenso, kumasulidwa kwa osautsidwa,
19 And he sent me to declare that now is the time when (the Lord/God) will [act] favorably [toward people].
ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”
20 Then he rolled up the scroll and gave it back to the attendant, and sat down [to teach the people]. Everyone in the synagogue was looking intently [MTY] at him.
Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye,
21 He said to them, “Today as you have been hearing [MTY] [me speak], [I am beginning] to fulfill this Scripture passage.”
ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”
22 [At first] everyone there spoke well about him, and they were amazed at the charming words that he spoke. [But then some of] them said, “(He is [only] Joseph’s son!/Isn’t he [only] Joseph’s son?) [RHQ] [So] ([it is useless for us(exc) to listen to what he says!/why should we(exc) listen to what he says]?) [RHQ]”
Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”
23 He said to them, “Surely [some of] you will quote to me the proverb that says, ‘Doctor, heal yourself!’ [What you will mean is], ‘People told us that you did miracles in Capernaum [town, but we(exc) do not know if those reports are true. So] do miracles here in your own hometown, too!’”
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”
24 Then he said, “It is certainly true that [people] do not accept [the message of] a prophet when he speaks in his hometown, [just like you(pl) are not accepting my message now].
Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo.
25 But think about this: There were many widows in Israel during the time when [the prophet] Elijah [lived. During that time], because of there being no rain [MTY] for three years and six months, there was a great famine throughout the country.
Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo.
26 But [God] did not send Elijah to [help] any of those [Jewish] widows. [God sent him] to Zarepath [town] near Sidon [city], to [help] a [non-Jewish] widow.
Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni.
27 There were also many [Jewish] lepers in Israel during the time when the prophet Elisha [lived]. But [Elisha] did not heal any of them. He healed only Naaman, a [non-Jewish] man from Syria.”
Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”
28 When all the people in the synagogue heard him say that, they were very angry, [because they realized that he was inferring that he similarly would help non-Jewish people instead of helping Jews] (OR, [that they also were not worthy of receiving God’s help]).
Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi.
29 So they all got up and shoved him out of the town. They took him to the top of the hill outside their town in order to throw him off the cliff [and kill him].
Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho.
30 But he [simply] walked through their midst and went away.
Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.
31 [One day] Jesus went [with his disciples] down to Capernaum, a town in Galilee [district]. On the next (Sabbath/Jewish day of rest) (OR, Each (Sabbath/Jewish day of rest)), he taught the people ([in the synagogue/in the Jewish meeting place]).
Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu.
32 They were continually amazed at what he was teaching, because [he spoke] ([with authority/as people speak who have] the right to command others what to do).
Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.
33 [That day], (OR, On one of those Jewish days of rest, ) there was a man in the synagogue who was controlled by an evil spirit. That man shouted very loudly,
Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti
34 “Hey! Jesus, from Nazareth! [We(exc) evil spirits] have nothing in common with you, so ([do not interfere with us now!/why should you interfere with us now]?) [RHQ] (Do not destroy us [now!]/Have you come to destroy us [now]?) [RHQ] I know who you are. You are the Holy One [who has come] from God!”
“Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
35 Jesus rebuked [the evil spirit], saying, “Be quiet! And come out [of the man]!” The demon threw the man down on the ground in the midst of the people. But without harming the man, the demon left him.
Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.
36 The people were all amazed. They said to each other, “(What he says to the demons [has great power!/] [kind of] teaching is this?) [RHQ] He speaks to them like he knows that they must obey him, and as a result they leave people!”
Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!”
37 The people were telling everyone in [every village] in the surrounding region what Jesus [had done].
Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.
38 Jesus [and his disciples] left (the synagogue/the Jewish meeting place) and entered Simon’s house. Simon’s mother-in-law was sick and had a high fever. So [others in Simon’s family] (OR, [the disciples]) asked Jesus to [heal] her.
Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize.
39 So he bent over her and commanded the fever to leave her. At once she became well! She got up and served them [some food].
Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.
40 When the sun was setting [that day, and the restriction about not traveling] (on [the Sabbath/on the Jewish rest day]) [was ended], many people [HYP] whose [friends or relatives] were sick or who had various diseases brought them to Jesus. He put his hands on them and healed [all of] them.
Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa.
41 He also was [expelling demons] from many people. As the demons left those people, they shouted to Jesus, “You are (the Son of God/the one who is God and man)!” But he rebuked those demons and would not allow them to tell [people about him], because they knew that he was the Messiah, and [for various reasons he did not want everyone to know that yet].
Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.
42 [Early] the next morning [Jesus] left that house and went to an uninhabited place [to pray]. Many people searched for him, and when they found him they kept urging him not to leave them.
Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere.
43 But he said to them, “I must tell [people] in other towns also the good message about how God wants to rule [MET] their lives, because that is what I was sent {[God] sent me} to do.”
Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.”
44 So he kept preaching in (the synagogues/Jewish worship places) [in various towns] in Judea [province].
Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.