< Luke 14 >

1 One (Jewish day of rest/Sabbath day), Jesus went to eat [SYN] at the house of an important Pharisee. Some [men who studied the Jewish] laws and other Pharisees who were there were watching him carefully [to see if he would do something for which they could accuse him].
Pa tsiku lina la Sabata, Yesu atapita kukadya ku nyumba ya Mfarisi wodziwika, Afarisi anamulonda mosamalitsa.
2 Unexpectedly, there was a man in front of Jesus whose arms and legs were swollen.
Poteropo, patsogolo pake panali munthu amene anadwala matenda otupa mimba ndi miyendo.
3 Jesus said to them, “Is it permitted in [our(inc)] Jewish laws to heal [someone] (on our Jewish rest day/on the Sabbath), or not?”
Yesu anafunsa Afarisi ndi akatswiri amalamulo kuti, “Kodi ndi zololedwa kuchiritsa pa tsiku la Sabata kapena ayi?”
4 [They knew that their laws permitted it, but they thought that healing was work, which they thought was wrong to do] (on the Sabbath/on the Jewish rest day) (OR, [they knew that their laws permitted it, but they did not want to admit it]). So they did not reply. Then Jesus put his hands on the man and healed him. Then he told him to go [home].
Koma iwo sanayankhe. Tsono atamutenga munthuyo, Iye anamuchiritsa ndipo anamuwuza kuti azipita.
5 Then he said to the rest of them, “If you had a son or an ox that fell into a well on a (Sabbath/our day of rest), would you immediately [work to] pull him out, [or would you(sg) let him stay there until the next day]?”
Kenaka Iye anawafunsa kuti, “Kodi ngati mmodzi mwa inu ali ndi mwana wamwamuna kapena ngʼombe imene yagwera mʼchitsime tsiku la Sabata, kodi simungamuvuwulemo tsiku lomwelo?”
6 [They knew that they would immediately work to pull him out, even on their day of rest, so they could not justly say that Jesus did wrong by healing the man on that day. So] they said nothing in reply to Jesus.
Ndipo iwo analibe choyankha.
7 Jesus noticed that those people who had been {whom [the Pharisee] had} invited [to the meal] chose [to sit in] the places where important [people usually sit]. Then he gave [this advice] to them:
Iye ataona momwe alendo amasankhira malo aulemu pa tebulo, Iye anawawuza fanizo ili:
8 “When one of you [(sg)] is invited by someone {someone invites one of you [(sg)]} to a wedding feast, do not sit in a place where important people sit. Perhaps the man [giving the feast] has invited a man more important than you [(sg)].
“Pamene wina wakuyitanani ku phwando la ukwati, musakhale pa malo aulemu ayi, chifukwa mwina anayitananso munthu wina wolemekezeka kuposa inu.
9 [When that man comes], the man who invited both of you will come to you [(sg)] and say to you, ‘Let this man take your seat!’ Then you [(sg)] will have to take the most undesirable seat, and you will be ashamed.
Ngati zitatero, ndiye kuti munthu uja amene anakuyitani inu nonse awiri adzakuwuzani kuti, ‘Mupatseni munthu uyu malo anu.’ Pamenepo inu mudzachita manyazi, pokakhala malo wotsika.
10 Instead, when you are invited {[someone] invites one of you} [to a feast], go and sit in the most undesirable seat. Then when the man who invited everyone comes, he will say to you [(sg)], ‘Friend, sit in a better seat!’ Then all the people who are eating with you [(sg)] will see that he is honoring you.
Koma akakuyitanani, khalani pa malo otsika, kuti amene anakuyitanani uja adzakuwuzeni kuti, ‘Bwenzi, bwera udzakhale pa malo aulemu pano.’ Pamenepo inu mudzalandira ulemu pamaso pa alendo anzanu onse.
11 Also, [remember this]: [God] will humble those who exalt themselves. And [he] will exalt those who humble themselves.”
Pakuti aliyense wodzikuza adzamuchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamukweza.”
12 [Jesus] also said to [the Pharisee] who had invited him to the meal, “When you [(sg)] invite people to a midday or evening meal, do not invite your friends or your family or your other relatives or your rich neighbors. They can later invite you [(sg) for a meal]. In that way they will repay you.
Kenaka Yesu anati kwa mwini malo uja, “Ukakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamayitane abwenzi ako, abale ako, anthu afuko lako kapena anzako achuma; ngati iwe utero, iwo adzakuyitananso, choncho udzalandiriratu mphotho yako.
13 Instead, when you [(sg)] give a feast, invite poor [people], crippled [people], lame [people], or blind [people].
Koma ukakonza phwando, itana anthu osauka, ofa ziwalo, olumala ndi osaona.
14 They will be unable to repay you. [But God will bless you! He] will repay you [at the time] when [he causes] righteous people to become alive again.”
Pamenepo udzakhala wodala, chifukwa iwo sangakubwezere kanthu, koma Mulungu ndiye adzakubwezera pa chiukitso cha olungama.”
15 One of those who were eating with Jesus heard him say that. He said to Jesus, “God [has truly] blessed [us Jews] who will eat [with the Messiah] when he starts to rule!”
Mmodzi mwa amene amadya naye atamva izi, anati kwa Yesu, “Ndi wodala munthu amene adzadye nawo mu ufumu wa Mulungu.”
16 But [to show that many Jews whom God had invited would not accept God’s invitation] [MET], Jesus replied to him, “One time a man [decided] to prepare a large feast. He invited many people to come.
Yesu anayankha kuti, “Munthu wina ankakonza phwando lalikulu ndipo anayitana alendo ambiri.
17 When it was the day for the feast, he sent his servant to tell those who had been {whom he had} invited, ‘Come [now] because everything is ready!’
Nthawi yaphwando itakwana anatuma wantchito wake kuti akawuze onse amene anayitanidwa kuti, ‘Bwerani, pakuti zonse zakonzeka.’
18 But [when the servant did that], all of the people [whom he had invited] began to say why they did not want to come. The first [man the servant went to] said, ‘I have just bought a field, and I must go and see it. Please [ask your master to] forgive me for not coming!’
“Koma onse anayamba kupereka zifukwa mofanana. Woyamba anati, ‘Ine ndangogula kumene munda, ndipo ndikuyenera kupita kuti ndikawuone. Pepani mundikhululukire.’
19 Another person said, ‘I have just bought five pair of oxen, and I must go to examine them. Please [ask your master to] forgive me for not coming!’
“Wina anati, ‘Ndangogula kumene ngʼombe khumi zokoka ngolo ndipo kupita kukaziyesa. Pepani mundikhululukire.’
20 Another person said, ‘I have just been married. So I cannot come.’
“Wina anatinso, ‘Ine ndangokwatira kumene, choncho sinditha kubwera.’
21 So the servant returned to his master and reported what [everyone had said]. The owner of the house was angry [when he heard the reasons they gave for not] coming. He said to his servant, ‘Go out quickly to the streets and alleys of the city [and find] poor and crippled and blind and lame [people, and bring] them here into [my house]!’
“Wantchitoyo anabwera ndikudzamuwuza bwana wakeyo zimenezi. Pamenepo mphwandoyo anapsa mtima ndipo analamula wantchito wakeyo kuti, ‘Pita msangamsanga kunja mʼmisewu ndi mʼmakwalala a mu mzinda ndipo ukabweretse osauka, ofa ziwalo, osaona ndi olumala.’
22 [After the servant went and did that], he [came back and] said, ‘Sir, I have done what you [(sg)] told me to do, but there is still room [for more people].’
“Wantchitoyo anati, ‘Bwana, zimene munanena zachitika koma malo akanalipobe.’
23 [So] his master said to him, ‘Then go [outside the city]. Search for people along the highways. Search also along the narrow roads with hedges beside them [where homeless people may be staying]. Strongly urge the people in those places to come to [my house]. I want it to be full of [people]!’”
“Ndipo mbuye uja anawuza wantchito wake kuti, ‘Pita kunja ku misewu ikuluikulu ndi kunja kwa mpanda ndipo ukawawuze kuti alowe, kuti nyumba yanga idzaze.
24 [Then Jesus said], “I tell you [(pl)] this: Very few of you [Jewish] people will enjoy my feast, even though [I] invited you [first to eat it with me when I become king].”
Ine ndikukuwuzani inu kuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anayitanidwa adzalawa phwandolo.’”
25 Large groups of people were traveling with [Jesus]. He turned and said to them,
Gulu lalikulu la anthu linkayenda naye Yesu ndipo atatembenukira kwa iwo anati,
26 “If anyone comes to me who loves his father and mother and wife and children and brothers and sisters [more than] [HYP] [he loves me], he cannot be my disciple. He must even love me more than he loves his own life!
“Ngati wina aliyense abwera kwa Ine ndipo sadana ndi abambo ndi amayi ake, mkazi wake ndi ana, abale ake ndi alongo ake, inde ngakhale moyo wake omwe, iye sangakhale ophunzira wanga.
27 [People who are ready to execute a prisoner make] him carry his cross [MET] [to the place where others will nail him] on it. Only those who are willing [to allow others to hurt them and disgrace them] like that because of being my disciples, and who are willing to obey what I teach, can be my disciples.
Ndipo aliyense amene sasenza mtanda wake ndi kunditsata Ine sangakhale ophunzira wanga.
28 [I will illustrate] [MET]. If one of you desired to build a (tower/big house), (you would surely first sit down and determine how much it would cost!/would you not first sit down and determine how much it would cost?) [RHQ] Then you would determine whether you had enough money to complete it.
“Taganizani, ngati wina mwa inu akufuna kumanga nsanja, kodi iye sayamba wakhala pansi ndi kuganizira za mtengo wake kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanira kuti atsirizire?
29 [If you did not do that], if you laid the foundation and were not able to finish [the rest of the tower], everyone who saw it would make fun of you.
Pakuti ngati ayika maziko ndi kulephera kutsiriza, aliyense amene adzayiona adzamuseka,
30 They would say, ‘This man started to build [a tower], but he was not able to finish it!’
nanena kuti, ‘Munthu uyu anayamba kumanga koma sanathe kutsiriza.’
31 Or, if a king decided to [send his army to] war against another king, (he would surely first sit down [with those who] advised [him]./would he not first sit down [with those who] advised [him]?) [RHQ] They would determine whether [his army], which had only 10,000 soldiers, could defeat the [other army], which had 20,000 soldiers, and was about to attack his [army].
“Kapena mfumu imene ikupita ku nkhondo kukamenyana ndi mfumu ina, kodi siyamba yakhala pansi ndi kulingalira ngati ingathe ndi anthu 10,000 kulimbana ndi amene akubwera ndi 20,000?
32 If he [decided] that his army could not [defeat that army], he would send messengers to [the other king] while the other army was still far away. He would tell the messengers to say to that king, ‘What things must I do to have peace with your country?’
Ngati singathe, idzatuma nthumwi pomwe winayo ali kutali ndi kukapempha mgwirizano wamtendere.
33 So, similarly, if any one of you does not first decide that you [(sg)] are [willing to] give up all that you have, you cannot be my disciple.”
Mʼnjira yomweyo, wina aliyense wa inu amene sasiya zonse ali nazo sangakhale ophunzira wanga.
34 [Jesus also said, “You are like] [MET] salt, which is useful [to put on food]. But (salt certainly cannot be made {[you] certainly cannot make salt} to taste salty again if it stops tasting salty!/can salt be made {can [you] make salt} to taste salty again if it quits tasting salty?) [RHQ]
“Mchere ndi wabwino, koma ngati usukuluka adzawukoleretsanso ndi chiyani?
35 [If salt does not taste salty any more], it is not good for the soil or even for the manure heap. [People] throw it away. [The same thing will happen to you if you become useless to God]. If you want to understand what I just said [IDM], you must consider [carefully] what you have heard!”
Suyeneranso ngakhale mʼnthaka kapena kudzala la manyowa; umatayidwa kunja. “Amene ali ndi makutu akumva, amve.”

< Luke 14 >