< Leviticus 27 >

1 Yahweh also said to Moses/me,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Tell the Israeli people [that this is what I am saying to them]: If anyone solemnly promises to dedicate another person to [work solely] for me, the person who is dedicated to me is allowed to be free from having to do that by someone paying [to the priest] a fixed amount of money. The money that is given must be calculated by comparing it with the official pieces of silver in the Sacred Tent.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole,
3 [These are the amounts that must be paid]: 50 pieces of silver for men who are between 20 and 60 years old,
mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60.
4 30 pieces of silver for adult women [who are between 20 and 60 years old],
Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu.
5 20 pieces of silver for young men who are between five and 20 years old, ten pieces of silver for young women who are between five and 20 years old,
Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi.
6 five pieces of silver for boys who are between one month and five years old, three pieces of silver for girls who are between one month and five years old,
Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva.
7 15 pieces of silver for men who are more than 60 years old, ten pieces of silver for women who are more than 60 years old.
Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi.
8 ‘If anyone who has made such a solemn promise is very poor and unable to pay, to free that person from doing what he had promised, he must take that person to the priest. The priest will set the price [for freeing him] to be what the person who made that solemn promise is able to pay.
Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.
9 ‘If someone solemnly promises to give an animal that is acceptable to be an offering to me, that animal becomes sacred [and belongs to me].
“‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika.
10 The person who promised to give it must not give another animal instead of the one that he promised; he must not substitute a bad animal for a good one or even a better one than the one offered. If he would substitute one animal for the other, both animals would belong to me.
Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika.
11 If the animal that he wishes to dedicate to me is a kind that is unacceptable to be an offering to me, he must take that animal to the priest.
Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe,
12 The priest will then decide what its value is, according to the animal’s good and bad points. Whatever value the priests sets will be the value of the animal, [and that is the price that the priest must pay for the animal].
ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
13 If the man who gave the animal later decides that he wants to buy it back, he must pay [to the priest] that price plus an additional 20 percent.
Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.
14 ‘[Similarly], if someone dedicates his house to be a sacred gift to belong to me, the priest will decide how much it is worth, which will depend on whether the house is in good condition. Whatever the priest says that it is worth, that will be its value [and that is the price that the priest must pay for it].
“‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
15 If the man who dedicated his house to me later wants to buy it back, he must pay that price plus an additional 20 percent, and then the house will belong to him again.
Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.
16 ‘If someone dedicates to me some of the property that belongs to him and his family, its value will be determined by the number of bushels of seed that will be needed to plant seeds on that land: Its value will be ten pieces of silver for each bushel of seed.
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu.
17 If he dedicates the land during the Year of Celebration, its full value will be that amount.
Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa.
18 But if he dedicates the field after the Year of Celebration, the priest will count the number of years until the next Year of Celebration, and if there are not many years that remain, the price will be much lower [than the full price].
Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo.
19 If the person who dedicated the field later wants to buy it back, he must pay [to the priest] the price that the priest says it is worth, plus an added one-fifth, and then the field will belong to that man again.
Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake.
20 However, if he does not buy it back, or if it has been sold (OR, the priest has sold it) to someone else, that person will never be permitted to buy it back again.
Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso.
21 In the Year of Celebration, it will become sacred again, and it will be given to the priest.
Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.
22 ‘If someone dedicates to me some land that he has bought, land which is not part of the land that his family has always owned,
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake,
23 the priest will count the number of years until the next Year of Celebration to determine how much it is worth, and the man must pay that amount to the priest on that day, [and then that land will belong to that man again].
wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova.
24 But in the Year of Celebration, the land will again be owned by the person from whom he bought it, the person whose family had always owned that land.
Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake.
25 All the silver that is paid must be compared with the official pieces of silver in the Sacred Tent.
Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.
26 ‘No one is permitted to dedicate to me the firstborn of any cow or sheep, because the firstborn already belongs to me [DOU].
“‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova.
27 If someone gives to me a kind of animal that is not acceptable to me, that person may later buy it back by paying what it is worth plus an additional 20 percent of its value. If he does not buy it back, it must be sold (OR, the priest must sell it) for its standard price.
Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.
28 ‘However, no slave or animal or family land that someone owns can be sold or bought back after it has been dedicated to me [and no price has been paid for it]. That kind of gift belongs to me permanently/forever.
“‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.
29 ‘No person who has [done something that I consider to be very wicked] is permitted to be freed [from being punished]; that person must surely be executed.
“‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.
30 ‘One tenth of all the crops and grain or fruit that is produced on anyone’s land is sacred and belongs to me.
“‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova.
31 If anyone wants to buy back any of that tenth, he must pay [to the priest] what it is worth plus an additional 20 percent.
Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo.
32 One of every ten domestic animals belongs to me. When a shepherd counts his animals [MTY] [to decide which ones he will give to me], he must mark every tenth one as belonging to me.
Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova.
33 When he does that, he must not pick out the good ones for himself or leave the bad ones, or substitute bad ones for good ones. If he substitutes one animal for another, both animals will belong to me, and he will not be permitted to buy them back (OR, the shepherd cannot buy them back).’”
Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’”
34 Those are the commands that Yahweh gave to Moses/me on Sinai Mountain [to tell to the people].
Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.

< Leviticus 27 >