< Judges 2 >

1 Yahweh [appeared in the form of] an angel [and] went up from Gilgal to [a place that was later called] Bokim. He said [to the Israeli people], “I brought your [ancestors] up here from Egypt. I led them into this land that I solemnly promised to give to your ancestors. I said to them, ‘The agreement that I made with you, as for me, I will never (break it/say that it is ended).
Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
2 But as for you, you must never make a peace agreement with the people who live in this land. You must tear down the altars [where they make sacrifices to idols].’ But you have not obeyed me.
ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
3 So now, I am telling you that I will not expel [your enemies] as you advance. They will be like thorns in your sides. And [they] will try to trap you [by making you worship] their idols.”
Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
4 After he told that to all the Israelis, the people cried loudly.
Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
5 They called that place Bokim, [which means ‘weeping’]. There they offered sacrifices to Yahweh.
ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
6 After Joshua sent the Israeli people away, each group went to possess the land that had been allotted to them.
Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
7 They served Yahweh as long as Joshua was alive, and as long as the elders, those who had seen all the great things that Yahweh had done for Israel, were alive.
Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
8 Then Yahweh’s servant Joshua died. He was 110 years old when he died.
Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
9 They buried his body in the area he had received [from Moses], at Timnath-Serah, in the area where the descendants of Ephraim lived, north of Gaash Mountain.
Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
10 After all the people died who lived at the same time as Joshua [EUP], a group of people grew up who did not know Yahweh, and did not know what great things he had done for the Israeli people.
Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
11 They did things that Yahweh said were very evil. They worshiped [idols that represented the god] Baal and the goddess Astarte. They worshiped [DOU] the various gods that the people-groups around them worshiped. They stopped worshiping Yahweh, the God their ancestors worshiped, the one who had brought their ancestors out of Egypt. That caused Yahweh to be very angry.
Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
14 So he allowed people from other groups to raid them and steal their crops and animals. They were no longer able to resist their enemies, and Yahweh allowed all their enemies around them to defeat them.
Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
15 Whenever the Israelis went to fight [their enemies], Yahweh [MTY] was opposing them, and allowed their enemies to defeat them, just as he had promised he would do. So the Israelis were greatly distressed.
Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
16 Then Yahweh gave leaders to them. These leaders rescued the Israelis from the people who were raiding them.
Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
17 But the Israelis still would not pay attention to their leaders. Instead, they went to the idols, [acting like] prostitutes [who gave themselves to men who were not their husbands] [MET], and they worshiped those idols. They were not like their ancestors. Their ancestors obeyed what Yahweh commanded, but their descendants quickly stopped behaving as their ancestors had behaved.
Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
18 Whenever Yahweh gave a leader to them, he helped that leader and enabled him to rescue the people from their enemies. He helped them like that as long as that leader was alive. Yahweh pitied them as they groaned because they were being oppressed and caused to suffer.
Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
19 But after that leader died, the people went back to behaving in ways even more evil than their ancestors had behaved. They worshiped other gods and bowed down to them and did all [LIT] the things that they thought those gods wanted them to do.
Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
20 So Yahweh was very angry with the Israeli people. He said, “These people have disobeyed the agreement I made with their ancestors. They have not done what I told them to do.
Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
21 So I will no longer expel the people-groups that Joshua left in this land when he died.
Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
22 I will use them to test the Israeli people to see whether they will do what I want them to do, as their ancestors did.”
Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
23 Yahweh had allowed those people-groups to stay in that land. He did not expel them by allowing Joshua [and his men] to defeat them.
Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.

< Judges 2 >