< Judges 18 >

1 At that time the Israelis had no king. Also at that time, the tribe of Dan was still searching for some land where they could live. The other Israeli tribes had [been able to] ([capture/take possession of]) [the] land that had been allotted to them, but the tribe of Dan had not been able to do that.
Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli. Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli.
2 So they chose five soldiers from their clans, men who lived in Zorah and Eshtaol [cities], to go through the land and explore it [and try to find some land where their tribe could live]. They came to Micah’s house in the hilly area where the tribe of Ephraim lived, and they stayed there that night.
Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.” Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona.
3 While they were in his house and they heard the young man who had become Micah’s priest talking, they recognized from (his accent/the way that he talked) [that he was from the southern part of Israel]. So they went to him and asked him, “Who brought you here? What are you doing here? Why did you come here?”
Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”
4 He told them the things that Micah had done for him. And he said, “Micah (has hired me/is paying me to work for him), and I have become his priest.”
Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”
5 So they said to him, “Please ask God if we will succeed [in what we are trying to do] on this journey.”
Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”
6 The young man replied, “Things will go well for you. Yahweh will go with you on this journey.”
Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”
7 [The next day] the five men left. When they came to Laish [city], they saw that the people there lived safely, like the people in Sidon [city] did. The people there thought that they were safe/protected [from any enemies], and they had plenty of [good fertile] land. They lived very far from the people of Sidon, [so the people of Sidon would not be able to help defend/protect them]. They had no other (allies/groups nearby that would help them in battles).
Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.
8 When those five men returned to Zorah and Eshtaol, their relatives asked them “What did you find out?”
Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”
9 They replied, “We have found some land, and it is very good. We should go and attack the people [who live there]. Why are you staying here and doing nothing [RHQ]? Do not wait any longer! We should go immediately and take possession of that land!
“Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda.
10 When you go there, you will see that there is plenty of land, and it has everything [that we will need]. The people there are not expecting anyone to attack them. Surely God is giving that land to us.”
Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”
11 So 600 men from the tribe of Dan left Zorah and Eshtaol, carrying their weapons.
Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo.
12 On their way they set up their tents near Kiriath-Jearim [city] in [the area where the tribe of] Judah [lives]. That is why the area west of Kiriath-Jearim was named ‘Camp of Dan’, and that is still its name.
Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero.
13 From there, they went to the hilly area where the tribe of Ephraim lives. And they arrived at Micah’s house.
Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.
14 The five men who had explored the land near Laish said to their fellow Israelis, “Do you know that in one of these houses there is a sacred vest, several idols, and a statue? [We think that] you know what you should do.” [RHQ]
Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.”
15 So they went to the house where the man from the tribe of Levi lived, which was the house where Micah lived, and they greeted the young man from the tribe of Levi [who had become Micah’s priest].
Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili.
16 The 600 men of the tribe of Dan stood outside the gate of the house, carrying their weapons.
Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo.
17 The five men who had explored the land went into Micah’s house, and took all the idols, the sacred vest, and the statue. While they did that, the 600 men stood outside the gate, [talking] with the priest.
Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.
18 When the priest saw them bringing out the idols and the sacred vest and the statue, he said to them, “What are you doing?”
Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
19 They replied, “Be quiet! Do not say anything! You come with us and be [like] a father to us and a priest for us. Is it better for you to [stay here and] be a priest for the people in the house of one man, or to be a priest for a clan, and a priest for a whole tribe of Israelis?” [RHQ]
Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?”
20 The priest liked what they were suggesting. So he took the sacred vest and the idols, and he [prepared to] go with the men from the tribe of Dan.
Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo.
21 They all put their little children and their animals and everything else that they owned in front of them.
Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.
22 After they had gone a little distance from Micah’s house, Micah [saw what was happening. He] quickly summoned the men who lived near him, and they ran and caught up with the men from the tribe of Dan.
Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza.
23 They shouted at them. The men of the tribe of Dan turned around and said to Micah, “What is the problem? Why have you gathered these men [to pursue us]?”
Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”
24 Micah shouted, “You took the silver idols that were made for me! You also took my priest! I do not have anything left [RHQ]! So why do you ask me, ‘What is the problem?’”
Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”
25 The men from the tribe of Dan replied, “You should not shout loudly like that! One of our angry men might attack you and kill you and your family!”
Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.”
26 Then the men from the tribe of Dan continued walking. Micah realized that there was a very large group of them, [so that it would be useless for him to try to fight them]. So he turned around and went home.
Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.
27 The men of the tribe of Dan were carrying the things that had been made for Micah, and they also took his priest, and they continued traveling to Laish. They attacked the people who were peacefully living there, and killed them with their swords, and then they burned everything in the city.
Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto.
28 Laish was far from [the city of] Sidon, [so the people of Sidon could not rescue the people of Laish]. And the people of Laish had no other allies. Laish was in a valley near Beth-Rehob [town]. The people of the tribe of Dan rebuilt the city and started to live there.
Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu. Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo.
29 They gave to the city a [new] name, Dan, in honor of their ancestor Dan, who was one of the sons of Jacob.
Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi.
30 The people of the tribe of Dan set up [in the city] the idols [that had been made for Micah]. Jonathan, who was the son of Gershom and the grandson of Moses, was appointed to be their priest. His descendants continued to be priests until the Israelis were captured and taken [to Assyria].
Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.
31 After the people of the tribe of Dan set up the idols that had been made for Micah, [they worshiped those idols, even though] the Sacred Tent [where they had been commanded to worship] God, was at Shiloh.
Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.

< Judges 18 >