< Judges 15 >
1 During the time that they harvested wheat, Samson took a young goat to Timnah as a present for his wife. He planned to sleep with [EUP] his wife, but her father would not let him go into [her room].
Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.
2 He said to Samson, “I really thought that you hated her. So I gave her to the man who had been your best man at the wedding, and she married him. But look, her younger sister is [RHQ] more beautiful than she is. You can marry her!”
Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”
3 Samson replied, “No! And this time I have a right to get revenge on you Philistines!”
Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.”
4 Then he went out [into the fields] and caught 300 foxes. He tied their tails together, two-by-two. He fastened torches to each pair of tails.
Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali.
5 Then he lit the torches and let the foxes run through the fields of the Philistines. The fire [from the torches] burned all the grain to the ground, including the grain that had been cut and piled in bundles. The fire also burned down their grapevines and their olive trees.
Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.
6 The Philistines asked, “Who did this?” Someone told them, “Samson did it. He married a woman from Timnah, but then his father-in-law gave her to the man who was Samson’s best man at the wedding, and she married him.” So the Philistines went [to Timnah] and got the woman and her father, and burned them to death.
Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.” Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake.
7 Samson [found out about that, and he] said to them, “Because you have done this, I will not stop until I get revenge on you!”
Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.”
8 So he attacked the Philistines furiously, and killed many of them. Then he went [to hide] in a cave in the large rock at a place called Etam.
Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.
9 The Philistines [did not know where he was, so they] went up to where the descendants of Judah lived, set up their tents near Lehi [town and then raided the town].
Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi.
10 The men there asked the Philistines, “Why have you attacked us?” The Philistines replied, “We have come to capture Samson. We have come to get revenge on him for what he did to us.”
Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?” Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”
11 [Someone there knew where Samson was hiding]. So 3,000 men from Judah went down to get Samson at the cave in the rock where he was hiding. They said to Samson, “Do you not realize that the people of Philistia are ruling over us? Do you not realize what they will do to us?” Samson replied, “The only thing I did was that I got revenge on them for what they did to me.”
Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?” Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”
12 But the men from Judah said to him, “We have come to tie you up and put you in the hands of the Philistines.” Samson said, “All right, but promise me that you yourselves will not kill me!”
Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.” Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”
13 They replied, “We will just tie you up and take you to the Philistines. We will not kill you.” So they tied him with two new ropes, and led him away from the cave.
Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja.
14 When they arrived at Lehi, the Philistines came toward him, shouting [triumphantly]. But Yahweh’s Spirit came upon Samson powerfully. He snapped the ropes on his arms as easily as if they were stalks of burned flax, and the ropes fell off his wrists.
Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake.
15 Then he saw a donkey’s jawbone lying on the ground. It was fresh, [so it was hard]. He picked it up and killed about 1,000 Philistine men with it.
Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.
16 Then Samson wrote this poem: “With the jawbone of a donkey I have made them like a heap of [dead] donkeys. With the jawbone of a donkey I killed 1,000 men.”
Ndipo Samsoni anati, “Ndi chibwano cha bulu, milu ndi milu ya anthu. Ndi chibwano cha bulu, ndapha anthu 1,000.”
17 When he finished killing those men, he threw the jawbone away, and later that place was called Jawbone Hill.
Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.
18 Then Samson was very thirsty, so he called out to Yahweh, “You have given me strength to win a great victory. So now must I die because of being thirsty, with the result that those heathen Philistines will take away my body [and mutilate it]?”
Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?”
19 So God caused water to gush out of a depression in the ground at Lehi. Samson drank from it and soon felt strong again. He named that place ‘The spring of the one who called out’. That spring is still there at Lehi.
Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.
20 Samson was the leader of the Israeli people for 20 years, but during that time the Philistines [were the ones who really ruled over the land].
Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.