< Judges 14 >

1 One day when Samson was in Timnah [town], he saw a young Philistine woman there.
Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
2 When he returned home, he told his mother and father, “I saw a young Philistine woman in Timnah, and I want you to get her for me so I can marry her.”
Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
3 His mother and father objected very strongly. They said, “Is there no woman from our tribe, or from the other Israeli tribes, that you could marry? Why must you go to the heathen Philistines to get a wife?” But Samson told his father, “Get her for me! She is the one I want!”
Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
4 His mother and father did not realize that Yahweh was arranging this. He was preparing a way for [Samson to defeat] the Philistines, who were ruling over Israel at that time.
(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
5 So, as Samson was going down to Timnah, followed by his mother and father, a young lion attacked Samson near the vineyards close to Timnah.
Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
6 Then Yahweh’s Spirit came upon Samson powerfully, with the result that he tore the lion apart with his hands. He did it [as easily] as if it were a young goat. But he did not tell his mother and father about it.
Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
7 When they arrived in Timnah, Samson talked with the young woman, and he liked her very much. [And his father made arrangements for the wedding].
Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
8 Later, when Samson returned to Timnah for the wedding, he turned off the path to see the carcass of the lion. He discovered that [after other creatures had eaten all the flesh], a swarm of bees [had made a hive in the skeleton and] had made some honey.
Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
9 So he scooped some of the honey into his hands and ate some of it as he was walking along. He also gave some of it to his mother and father, but he did not tell them that he had taken the honey from the skeleton of the lion, [because anyone dedicated to God was not to touch any corpse].
Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
10 As his father was making the final arrangements for the marriage, Samson gave a party [for the young men in that area]. That was the custom for men to do when they were about to be married.
Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
11 Thirty young man were invited to the party.
Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
12 Samson said to them, “Allow me to tell you a riddle. If you tel me the meaning of my riddle during these seven days of the celebration, I will give each of you a linen robe and an extra set of clothes.
Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
13 But if you cannot tell me the meaning, you must each give me a linen robe and an extra set of clothes.” They replied, “All right. Tell us your riddle.”
Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
14 So he said, “From the thing that eats came something to eat; out of something strong came something sweet.” But for three days they could not tell him the meaning of the riddle.
Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
15 On the fourth day, they said to Samson’s bride, “Ask your husband to tell you the meaning of the riddle. If you do not do that, we will burn down your father’s house, with you inside it! Did you invite us here only to make us poor [by forcing us to buy a lot of clothes for your husband]?”
Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
16 So Samson’s wife came to him, crying, and said to him, “You do not really love me. You hate me! You have told a riddle to my friends, but you have not told me the meaning of the riddle!” He replied, “I have not told the meaning of the riddle even to my mother and father, so why should I tell it to you?”
Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
17 She continued to cry every time she was with him, all during the rest of the celebration. Finally, on the seventh day, because she continued to nag him, he told her the meaning of the riddle. Then she told it to the young men.
Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
18 So, before sunset on the seventh day, the young men came to Samson and said to him, “What/Nothing is sweeter than honey [RHQ]. What/Nothing is stronger than a lion [RHQ]!” Samson replied, “[You should not force a heifer to] plow a field [MET]. Similarly, if you had not forced my bride to ask me about the riddle [MET], you would not have known the answer to my riddle!”
Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
19 Then Yahweh’s Spirit powerfully took control of Samson. He went down to [the coast at] Ashkelon [town], and killed 30 men. He took their clothes [and went back to Timnah] and gave them to the men who had told him the meaning of the riddle. But he was very angry about what had happened, so he went back home to live with his mother and father.
Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
20 So (Samson’s wife was given/the bride’s father gave Samson’s wife) to the man who who had been Samson’s best man at the wedding, [but Samson did not know that].
Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.

< Judges 14 >