< Joshua 4 >

1 After all the people of the Israeli nation had finished crossing the Jordan [River], Yahweh said to Joshua,
Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
2 “When you choose the twelve men, one from each tribe, whom I mentioned previously, tell them to pick up [large] stones from the middle of the Jordan riverbed, where the priests are [still] standing.
“Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
3 Tell them to carry the stones with you and put them down at the place where you will stay tonight.”
Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
4 So Joshua chose twelve men, one from each tribe. He called them together, and said to them,
Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
5 “Go into the middle of the Jordan riverbed, to [where the priests are standing, holding] the chest that Yahweh, your God, gave you. Each of you must pick up a [large] stone, one for each tribe, [and carry it] on your shoulder [to our camp].
ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
6 [Then pile them up] to be a memorial for you. In the future, when your children ask, ‘What do these stones mean?’,
kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
7 tell them that the water in the Jordan River was blocked off when the priests were carrying the chest [that contained] the Ten Commandments that Yahweh [gave us]. When the chest was carried into the Jordan [River], the water was blocked off [so that we could cross the riverbed]. These stones will be a memorial for the descendants of us Israeli people forever.”
Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
8 So those Israeli men did what Joshua told them to do. They went and picked up twelve [large] stones from the middle of the Jordan [riverbed], one stone for each of the tribes, just as Yahweh had told Joshua. They carried the stones to their camp and put them down.
Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
9 Then Joshua set up twelve [other large] stones [in a pile], in the middle of the Jordan [riverbed], where the priests who carried the chest containing the Ten Commandments were standing. And those stones are still there.
Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
10 The priests who carried the chest remained standing in the middle of the Jordan [riverbed] until the people had finished doing everything that Yahweh had commanded Joshua to tell them to do. Those were the same instructions that Moses had given to Joshua. The Israeli people crossed [the riverbed] quickly.
Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
11 As soon as all of them had crossed, as the people watched, the priests carried the chest [the rest of the way across the river].
Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
12 The soldiers of the tribes of Reuben, Gad, and of half of the soldiers of the tribe of Manasseh, crossed over ahead of the rest of the Israeli people, carrying their weapons, as Moses had commanded.
Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
13 As Yahweh was watching, there were about 40,000 of those soldiers, carrying weapons ready for battle, who crossed the riverbed to the plains near Jericho, [ready] to fight.
Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
14 On that day, all the people of Israel saw that Yahweh had caused Joshua to be a great leader. And they honored Joshua for the rest of his life, just as they had honored Moses.
Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
15 Yahweh said to Joshua,
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
16 “[Now] tell the priests who are carrying the chest containing the Ten Commandments to come up from the Jordan [riverbed].”
“Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
17 So Joshua commanded the priests to do that.
Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
18 Then the priests, carrying the chest containing the Ten Commandments that Yahweh [had given to Moses], came up out of the riverbed. And as soon as they walked up out of the riverbed onto the riverbank, the water of the Jordan [River] flowed again, and flooded [over the river banks] as it had done before.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
19 It was on the tenth day of the first month [of that year] that the people crossed over the Jordan [River] and camped at [a place called] Gilgal, on the east side of [the land near] Jericho [city].
Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
20 The men [who were carrying] the twelve [large] stones from the Jordan [riverbed brought them to] Joshua, [and he] set them up at Gilgal
Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
21 Joshua said to the Israeli people, “In the future, when your children and grandchildren ask, ‘(What do these stones [mean/Why are these stones here)]?’,
Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
22 tell them, ‘We Israeli people crossed the Jordan [River as though we were crossing] on dry ground.
Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
23 As we were watching, Yahweh, your God, dried up the river until we had all crossed over. Yahweh, the God whom we worship, did to the Jordan [River] just like he did to the Red Sea, when he caused it to become dry as [our parents] were watching, until they all crossed over it.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
24 Yahweh did that in order that all the people-groups of the earth may know that he [MTY] is very powerful, and in order that you may always (be in awe of/revere) Yahweh, your God.’”
Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”

< Joshua 4 >