< Joshua 3 >

1 Joshua [and all the other Israelis] got up early [the next] morning. They left [their camp at] Acacia and went [down] to the Jordan [River]. They camped there for two nights.
Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
2 Then the leaders went throughout the camp,
Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
3 telling the people, “You will see some of the priests, who are descendants of Levi, carrying the chest that contains the Ten Commandments that Yahweh our God gave us. When you see them, leave the places where you are camped and follow them.
kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
4 You have not been (here/along this road) before, [so you must follow the priests]. But do not walk close to the chest. Stay (1,000 yards/900 meters) from the chest. [The chest is sacred, so (God will punish you/you will be punished) if you come close to it].”
Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
5 Then Joshua told the people, “Perform the ceremonies needed to make yourselves acceptable to Yahweh, because tomorrow he is going to do things for you that will amaze you!”
Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
6 Then Joshua said to the priests, “Carry the chest and go in front of the [rest of the] people.” So they lifted up the chest and went ahead.
Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
7 Then Yahweh said to Joshua, “This is the day that I will begin to show all the Israeli people that you are a great leader. Then they will honor you, and know that I am with/helping you as I (was with/helped) Moses.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
8 Tell the priests who are carrying the chest that contains the Ten Commandments, ‘When you come to the edge of the Jordan [River], stand in the water.’”
Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
9 Then Joshua said to the Israeli people, “Come close to me in order that you can listen to what Yahweh, your God, is saying.”
Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
10 [When they came near], he said to them, “This is how you will know that God, who is all-powerful, is among you, and that he will expel for you the descendants of Canaan, Heth, Hiv, Periz, Girgash, Amor, and Jebus [who are now living in that land].
Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
11 Keep in mind that Yahweh is the one who rules over all the earth. The chest belongs to him, and it will be carried into the Jordan River ahead of you.
Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
12 So choose twelve men, [one from each] of the tribes of Israel, [and I will tell you later what I want them to do].
Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
13 As for the priests who are carrying the chest, as soon as they put their feet into the Jordan [River], the water will stop flowing. It will pile up because I will cause it to be blocked upstream.”
Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
14 So when the [Israeli] people packed up their tents in order to cross the river, the priests who were carrying the chest containing the Ten Commandments went in front of them.
Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
15 [It was springtime], when people harvest their crops, [and] at that time the river floods over its banks. But as soon as the priests reached the edge of the river and stepped into the water,
Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
16 the water stopped flowing. The water piled up far [upstream], at a town named Adam, near Zarethan. The water stopped flowing down to the Dead Sea. So the people were able to cross the river near Jericho.
madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
17 The priests who were carrying the chest containing the Ten Commandments that Yahweh [had given them] stood on dry ground in the middle of the Jordan [riverbed], while the rest of the Israeli people crossed the river [as though they were crossing] dry ground.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.

< Joshua 3 >