< Joshua 13 >

1 When Joshua was very old, Yahweh said to him, “Joshua, you are now an old man, but there is still a lot of land [for your army] to capture.
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 Here is a list of the land that remains: The Geshur region and all the area where the Philistia people-group live;
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 the area where the Canaan people-group live, from the Shihor River [in the south] at the [eastern] border of Egypt, to Ekron [city] in the north; the rulers of the five [cities] of Gaza, Ashdod, Ashkelon, Gath, and Ekron; the area where the Avva people-group live,
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 which is south of the area where the Canaan people-group live;
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 the area where the Gebal people-group live; and all the Lebanon area east of Baal-Gad [city] at the bottom of Hermon Mountain, as far as Lebo-Hamath.
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 All the people of the Sidon people-group live in the hilly area from Lebanon to Misrephoth-Maim, but I will force them to leave that area before you Israelis arrive there. Be sure to give that area to the Israeli people when you divide the land among them, like I told you to do.
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 Divide all that land among the nine Israeli tribes and half of the tribe of Manasseh, [the tribes that do not have land on the east side of the Jordan River].”
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 Half of the tribe of Manasseh and the tribes of Reuben and Gad had already been told what land they would receive, because Moses, the man who served Yahweh [well], had already assigned to them the land on the east side of the Jordan [River].
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 Their land extended from Aroer [town] at the Arnon River gorge to the town in the middle of the gorge. It included the whole plain from Medeba [town south] to Dibon [town].
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 All the towns ruled by King Sihon were in that area. The land extended to where the Ammon people-group lived.
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 The Gilead area was also there, and the regions where the people of the Geshur and Maacah people-groups lived, and all of Hermon Mountain and all the Bashan region [south] to Salecah.
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 All the land ruled by Og, the king who ruled the Bashan [region], was in that land. Og was one of the last descendants of Repha; previously he had ruled in Ashtaroth and Edrei [cities], but [the armies of] Moses had defeated their armies and had taken their land from them.
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 But the Israelis did not force the people of the Geshur and Maacah [people-groups] to leave their land, so they still live among the Israeli people.
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 The tribe of Levi was the only tribe that did not get any land. Instead, just like Yahweh promised, they continued to receive [food from] the sacrifices that were given to Yahweh, the God whom the Israelis [worship], the sacrifices that were burned [on the sacred altar].
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 Moses had allotted land to each clan in the tribe of Reuben.
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 Their land extended from Aroer [town] near the Arnon River gorge to Medeba [town]. That included all of the plain [that is near Medeba] and the town in the middle of the gorge.
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 It also included Heshbon [city] and all the nearby towns on the plain—Dibon, Bamioth-Baal, Beth-Baal-Meon,
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
18 Jahaz, Kedemoth, Mephaath,
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 Kiriathaim, Sibmah, Zereth-Shahar on the hill overlooking the valley,
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
20 Beth-Peor, the hills in the Pisgah area, and Beth-Jeshimoth.
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 That land included all the towns on the plain and all the area that King Sihon had previously ruled. But [the army of] Moses had defeated him and the rulers of the Midian people-group: Evi, Rekem, Zur, Hur, and Reba. The armies of all those rulers fought battles along with the army of Sihon, and they lived in that country.
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 The Israeli army killed many people during those battles, including Balaam, [the prophet] from Beor, who tried to use magic to predict/tell what would happen in the future.
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 The [western] boundary of the land that was allotted to the clans of the tribe of Reuben was the Jordan [River].
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 Moses also allotted some land to each clan in the tribe of Gad.
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 Their land included the Jazer [area] and all the towns of the Gilead [area]; half of the land where the Ammon people-group lived, as far as Aroer [town which is] near Rabbah [town];
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 the area from Heshbon [city] to Ramath-Mizpah and Betonim [towns; the area] from Mahanaim [town] to the Debir region;
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 Beth-Haram, Beth-Nimrah, Succoth, and Zaphon [cities] in the valley; and the other area that King Sihon had ruled on the east side of the Jordan River. That area extended [north] to the southern end of Galilee Lake.
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 All this land, including the towns and villages, was allotted to the tribe of Gad.
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 Moses also had allotted some of the land [on the east side of the Jordan River] to half of the tribe of Manasseh.
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 Their land extended [north] from Mahanaim [city]. It included all the Bashan region, all the land that King Og had ruled, and all the towns in the Jair area in Bashan. Altogether that area included 60 towns.
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 Their area also included half of the Gilead region, and the cities of Ashtaroth and Edrei where King Og had ruled. All that area was allotted to the clans descended from Manasseh’s son Makir.
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 Moses had allotted to those tribes the land that was on the plain of the Moab [region], on the east side of the Jordan [River], across from Jericho.
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 But Moses did not allot any land to the tribe of Levi because Yahweh, the God whom we Israelis worship, promised that he himself would always provide for them.
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

< Joshua 13 >