< Jonah 4 >
1 But Jonah was very distressed [that God had not destroyed Nineveh]. He became very angry. [The people of Nineveh were non-Jews, and Jonah did not think that God should act mercifully toward anyone who was not a Jew].
Koma Yona anakhumudwa kwambiri ndipo anakwiya.
2 He prayed to Yahweh, “O Yahweh, what you have done is what I thought that you would do, before I left home [RHQ]. That is why I [decided] immediately to run away, and go to Tarshish [city], because I knew that you, O God, act very kindly and compassionately [toward all people]. You do not quickly become angry with people who do evil things. You love people very much, and you change your mind about punishing [people who sin].
Iye anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, kodi izi si zimene ndinanena ndikanali kwathu? Nʼchifukwa chaketu ine ndinafulumira kuthawa kupita ku Tarisisi. Ine ndinadziwa kuti ndinu Mulungu wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wa chikondi chopanda malire, Mulungu amene mumaleka kubweretsa tsoka.
3 [So] now, O Yahweh, [since you will not destroy Nineveh city as you said you would], allow me to die, because it would be better for me to die than to [continue to] live.”
Ndipo tsopano, Inu Yehova, ingondiphani basi, pakuti ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”
4 Yahweh replied, “(Why is it right for you to be angry [about my not destroying the city]?/It is not right for you to be angry [about my not destroying the city]!) [RHQ]”
Koma Yehova anayankha kuti, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye?”
5 Jonah [did not reply]. He went out of the city to the east [side of it]. He made a small shelter in order that he could sit under it and be protected from the sun. He sat under the shelter and waited to see what would happen to the city.
Yona anatuluka mu mzindamo nakakhala pansi cha kummawa kwa mzindawo. Kumeneko anadzimangira chithando nakhala mʼmenemo mu mthunzi, kudikira kuti aone zimene zichitikire mzindawo.
6 Then Yahweh God caused a vine to grow up [immediately] to shade Jonah’s head from the sun and make him [feel] more comfortable. Jonah was very happy about [having] the vine [over his head].
Tsono Yehova Mulungu anameretsa msatsi ndi kuyikulitsa kuti ipereke mthunzi kwa Yona kuchotsa mavuto ake; ndipo Yona anasangalala kwambiri chifukwa cha msatsiyo.
7 But before dawn the next day, God sent a worm that chewed the vine, with the result that the vine withered.
Koma tsiku linalo mmawa, Mulungu anabweretsa mbozi imene inadya msatsiyo ndipo inafota.
8 Then, when the sun rose [high in the sky], God sent a very hot wind from the east, and the sun shone very strongly on Jonah’s head, with the result that he felt faint. He wanted to die, and he said, “It would be better for me to die than to [continue to] live!”
Dzuwa litatuluka, Yehova anabweretsa mphepo yotentha yochokera kummawa, ndipo dzuwa linatentha pamutu pa Yona kotero analenguka nalo. Iye anangofuna atafa, ndipo anati, “Ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”
9 But God asked Jonah, “Is it right for you to be angry about [what happened to] the vine?” Jonah replied, “[Yes], it is right! [Now] I am very angry and I want to die!”
Koma Mulungu anati kwa Yona, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye chifukwa cha msatsi?” Iye anayankha kuti, “Inde nʼkoyenera. Kukwiya kwanga nʼkofuna kufa nako.”
10 But Yahweh said [to him], “You have been concerned about my [causing] that vine [to wither], even though you did not take care of it, and you did not make it grow. It just grew up during one night, and it completely withered [at the end of] the next night.
Koma Yehova anati, “Iwe ukumvera chisoni msatsiwo, ngakhale kuti sunawugwirire ntchito kapena kuwukulitsa. Inamera pa usiku umodzi ndipo inafanso pa usiku umodzi.
11 But there are more than 120,000 people in Nineveh who [are very young, and because of that], they cannot tell which is their right hand and which is their left hand, and there are also many cattle, [and none of these have done anything to displease me]. So (is it not right for me to be concerned about the people of that huge city, [and not want to destroy them]?/it is certainly right for me to be concerned about the people of that huge city [and not want to destroy them]!) [RHQ]”
Koma mu Ninive muli anthu opitirira 120,000 amene sadziwa kusiyanitsa kuti chabwino nʼchiti ndipo choyipa nʼchiti, mulinso ziweto zochuluka. Kodi sindiyenera kumvera chisoni mzinda waukulu ngati uwu?”