< John 20 >

1 Early on Sunday morning, while it was still dark, Mary, the woman from Magdala [village], went to the [burial] cave [with some other women]. They saw that the stone had been removed {that someone had removed the stone} from the [entrance to the] cave.
Mmamawa tsiku loyamba la sabata, kukanali kamdimabe, Mariya wa ku Magadala anapita ku manda ndipo anaona kuti mwala unali utachotsedwa pa khomo la manda.
2 So Mary ran to where Simon Peter and I [were staying in Jerusalem]. She said to us, “They have taken the Lord’s [body] out of the burial cave, and we do not know where they have put it!”
Choncho anabwerera akuthamanga kwa Simoni Petro ndi wophunzira winayo, amene Yesu anamukonda, ndipo anati, “Iwo amuchotsa Ambuye mʼmanda, ndipo ife sitikudziwa kumene iwo amuyika Iye!”
3 So Peter and I started going to the cave.
Choncho Petro ndi wophunzira winayo ananyamuka kupita ku manda.
4 We were both running, but I ran faster than Peter and got there first.
Onse awiri anathamanga pamodzi koma wophunzira winayo anamupitirira Petro, nafika ku manda moyambirira.
5 I stooped down [at the entrance] and looked inside. I saw the strips of linen cloth lying there [where his body had been laid], but I did not go inside.
Ndipo mmene anawerama nasuzumira mʼkati mwa manda anaona nsalu zili potero koma sanalowemo.
6 Then Simon Peter, who was running behind me, arrived. He went inside the cave. He, too, saw the strips of linen cloth lying there.
Kenaka Simoni Petro, amene anali pambuyo pake, anafika ndi kulowa mʼmanda. Iye anaona nsaluzo zili pamenepo,
7 He also [saw the] cloth that they had [wrapped] around Jesus’ head. It had been folded and put {Someone had folded it and put it} aside, separate from the linen strips.
pamodzinso ndi nsalu imene anakulungira nayo mutu wa Yesu. Nsaluyi inali yopindidwa pa yokha yosiyanitsidwa ndi inayo.
8 Then I also went inside. I saw [those things] and I believed [that Jesus had truly become alive again].
Pomaliza wophunzira winayo, amene anafika ku manda moyambirira, analowanso mʼkati, iye anaona ndi kukhulupirira.
9 Before this happened, we did not understand from [what the prophets had written in] the Scriptures, that he had to become alive again after he died.
(Iwo sanazindikire kuchokera mʼmalemba kuti Yesu anayanera kuuka kuchokera kwa akufa).
10 Then [we two] disciples went back to where we were staying. [In the meantime], Mary [returned to the cave].
Kenaka ophunzira anabwerera ku nyumba zawo,
11 As she stood outside the cave crying, she stooped down to look inside the cave.
koma Mariya anayima kunja kwa manda akulira. Pamene akulira, anawerama ndi kusuzumira mʼmanda
12 She saw two angels in very white [clothing], sitting at the place where Jesus’ body had been laid. One was where his head had been, and the other was where his feet had been.
ndipo anaona angelo awiri atavala zoyera, atakhala pamene panali mtembo wa Yesu, mmodzi kumutu ndi wina kumapazi.
13 They said to her, “Woman, why are you crying?” She said to them, “They have taken away [the body of] my Lord, and I do not know where they have put it!”
Iwo anamufunsa iye kuti, “Amayi, nʼchifukwa chiyani mukulira?” Iye anati, “Amuchotsa Mbuye wanga, ndipo ine sindikudziwa kumene iwo amuyika.”
14 After she said that, she turned around and saw Jesus standing [there], but she did not know that it was Jesus.
Atanena izi, iye anatembenuka ndipo anaona Yesu atayima potero koma iye sanazindikire kuti anali Yesu.
15 He said to her, “Woman, why are you crying? Who are you looking for?” Thinking that he was the gardener, she said to him, “Sir, if you have taken his [body] away, tell me where you have put it. Then I will get it [and bury it properly].”
Iye anati, “Amayi, mukulira chifukwa chiyani? Ndani amene mukumufunafuna?” Poganiza kuti anali mwini munda, iye anati, “Bwana, ngati inu mwamuchotsa, ndiwuzeni kumene mwamuyika, ndipo ine ndikamutenga.”
16 Jesus said to her, “Mary!” She turned toward him [again and recognized him]. Then she exclaimed in Aramaic, “Rabboni!” which means ‘Teacher’.
Yesu anati kwa iye, “Mariya.” Anatembenukira kwa Iye nafuwula mu Chiaramaiki kuti, “Raboni!” (kutanthauza Mphunzitsi).
17 Jesus said to her, “Stop clinging to me, because I have not yet returned to my Father. Go to my disciples and tell them, ‘I am about to return to my Father and your Father, to the one who is my God and your God’.”
Yesu anati, “Usandigwire Ine, pakuti sindinapite kwa Atate. Mʼmalo mwake pita kwa abale anga ndikukawawuza kuti, ndikupita kwa Atate ndi kwa Atate anunso, kwa Mulungu wanga ndi Mulungu wanunso.”
18 So Mary went to where [we] disciples were and told us that she had seen the Lord [alive again]. She also told us what Jesus said that she [should tell us].
Mariya wa ku Magadala anapita kwa ophunzira ndi uthenga wakuti, “Ndamuona Ambuye!” Iye anawawuza iwo kuti Yesu ananena zinthu izi kwa iye.
19 On that Sunday evening [we] disciples gathered together. The doors were locked {[We] locked the doors} because we were afraid that [the Jewish leaders] [SYN] [might arrest us. Suddenly] Jesus appeared [miraculously] and stood among us! He said to us, “May God give you [inner] peace!”
Madzulo a tsiku limenelo limene linali loyamba la Sabata ophunzira ake ali pamodzi, atatseka ndi kukhoma zitseko chifukwa choopa Ayuda, Yesu anabwera ndi kuyima pakati pawo nati, “Mtendere ukhale nanu!”
20 After he said that, he showed us [the wounds in] his hands and his side. We were very happy when we saw the Lord!
Iye atatha kunena izi, anawaonetsa manja ake ndi mʼnthiti mwake. Ophunzira anasangalala kwambiri pamene anaona Ambuye.
21 Jesus said to us again, “May God give you peace! Just like [my] Father sent me, now I am sending you [to proclaim my message].”
Yesu anatinso, “Mtendere ukhale nanu! Monga Atate anandituma Ine, Inenso ndikukutumani.”
22 After saying that, he breathed on us and said, “Receive the Holy Spirit!
Ndi mawu amenewo Iye anawapumira ndipo anati, “Landirani Mzimu Woyera.
23 If you forgive people for their having sinned, [God will already] have forgiven them. If you do not forgive them, [God] has not forgiven them.”
Ngati mukhululukira aliyense machimo ake, iwo akhululukidwa; ngati simuwakhululukira, iwo sanakhululukidwe.”
24 One of us disciples, Thomas, the one whom we called The Twin, was not with us when Jesus appeared to us.
Koma Tomasi (otchedwa Didimo), mmodzi wa khumi ndi awiriwo, sanali ndi ophunzira pamene Yesu anabwera.
25 When the rest of us told him that we had seen the Lord, he said to us, “If I do not see the marks of the nails in his hands and put my fingers in the place where the nails were, and put my hands into the place in his side [where the soldier thrust the spear], I will certainly not believe [that he was the one you saw]!”
Ophunzira enawo atamuwuza Tomasi kuti iwo anaona Ambuye, iye ananenetsa kuti, “Pokhapokha nditaona zizindikiro za misomali mʼmanja ake ndi kuyikamo chala changa mʼmene munali misomali ndi kukhudza dzanja langa mʼnthiti mwake, ine sindidzakhulupirira.”
26 A week later we were in [the house] again. This time Thomas was with us. Although the doors had been locked {[we] had locked the doors}, Jesus [again] appeared [miraculously] and stood among us. He said, “May God give peace to you!”
Patapita sabata, ophunzira ake analinso mʼnyumbamo ndipo Tomasi anali nawo. Ngakhale makomo anali otsekedwa, Yesu anabwera nayima pakati pawo, ndipo anati, “Mtendere ukhale nanu!”
27 Then he [showed] Thomas [his hands] and said to him, “Put your finger here! Look at [the wounds in] my hands! Reach out your hand and put it in [the wound in] my side! Stop doubting [LIT/DOU]! Instead, believe [that I am alive again]!”
Kenaka anati kwa Tomasi, “Ika chala chako apa; ona manja anga. Tambasula dzanja lako ndi kukhudza mʼnthiti mwanga. Leka kukayika, khulupirira.”
28 Thomas answered him, “[You are truly] my Lord and my God!”
Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye wanga ndi Mulungu wanga!”
29 Jesus said to him, “Because you have seen me, you have believed [that about me]. But God [is truly] pleased with those who have believed [that about me], even though they have not seen me!”
Kenaka Yesu anamuwuza kuti, “Kodi wakhulupirira chifukwa wandiona Ine? Ndi odala amene amakhulupirira ngakhale asanaone.”
30 [We] disciples saw Jesus perform many other miracles, but [I] have not written about them in this book.
Yesu anachita zodabwitsa zambiri pamaso pa ophunzira ake zimene sizinalembedwe mʼbuku lino.
31 But these [that I have written about, I] have written about them in order that you may believe that Jesus is the Messiah, (the Son of God/the man who is also God), and in order that you may have [eternal] life [by trusting] (in him/ in what he [has done for you]) [MTY].
Koma izi zalembedwa kuti mukhulupirire kuti Yesu ndi Khristu, Mwana wa Mulungu, ndi kuti mukakhulupirira mukhale nawo moyo mʼdzina lake.

< John 20 >