< John 18 >
1 After Jesus finished praying, he went across the Kidron Brook, along with [us] disciples, to a grove [of olive trees].
Yesu atamaliza kupemphera, Iye anachoka ndi ophunzira ake ndi kuwoloka chigwa cha Kidroni. Kumbali inayo kunali munda wa Olivi, ndipo Iye ndi ophunzira ake analowamo.
2 Judas, who was [about to] enable Jesus’ enemies to seize him, knew that [he would probably be] there. [He knew that because] Jesus often gathered there with us.
Tsopano Yudasi, amene anamupereka amadziwa malowo chifukwa Yesu ankakumana ndi ophunzira ake kumeneko.
3 So Judas came to that grove. He was leading a troop of Roman [soldiers] and some Temple guards who had been sent by the Pharisees and chief priests. They were carrying torches and lamps and weapons.
Choncho Yudasi anabwera ku munda, akutsogolera gulu la asilikali ndi akuluakulu ena ochokera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi. Iwo anali atanyamula miyuni, nyale ndi zida.
4 Jesus knew everything that was about to happen to him. So [as they approached], he stepped forward and asked them, “Who are you looking for?”
Yesu, podziwa zonse zimene zimati zichitike kwa Iye, anatuluka ndi kuwafunsa kuti, “Kodi mukufuna ndani?”
5 They replied to him, “Jesus, the man from Nazareth.” He replied, “That is who I am.” Judas, the one who was enabling his enemies to seize him, was with them.
Iwo anayankha kuti, “Yesu wa ku Nazareti.” Yesu anati, “Ndine.” (Ndipo Yudasi womuperekayo anali atayima nawo pamenepo).
6 When Jesus told them, “That is who I am,” they lurched backward and fell down on the ground [because of his power].
Pamene Yesu anati, “Ndine,” iwo anabwerera mʼmbuyo ndi kugwa pansi.
7 He asked them again, “Who are you looking for?” They said, “Jesus, [the man] from Nazareth.”
Iye anawafunsanso kuti, “Kodi mukumufuna ndani?” Ndipo iwo anati, “Yesu wa ku Nazareti.”
8 Jesus replied, “I told you that I am Jesus. So since I am the one you are looking for, allow these [disciples of mine] to go.”
Yesu anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kuti Ndine. Ngati inu mukufuna Ine, asiyeni anthu awa apite.”
9 [This happened] in order that [when they did what he asked them to do], the words would be fulfilled that he had prayed, “I will never lose any of those whom God has brought to me.”
Izi zinachitika kuti mawu amene Iye anayankhula akwaniritsidwe: “Ine sindinataye ndi mmodzi yemwe mwa iwo amene mwandipatsa.”
10 Simon Peter had a [long] dagger. So he drew it and [tried to kill] the high priest’s servant, [but he only] cut off the man’s right ear. The servant’s name was Malchus.
Kenaka Simoni amene anali ndi lupanga analitulutsa ndi kutema nalo wantchito wa wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake la kudzanja lamanja. (Dzina la wantchitoyo ndi Makusi).
11 Jesus said to Peter, “Put your sword [back] into its sheath! (I must endure what [my] Father wants me to suffer./Do you not think that I must endure what [my] Father wants me to suffer?) [MET, RHQ]”
Yesu analamula Petro kuti, “Bwezera lupanga mʼchimake! Kodi Ine ndisamwere chikho chimene Atate andipatsa?”
12 Then the troop of soldiers, along with their commander and the Jewish Temple guards, seized Jesus. They tied his hands [behind his back].
Kenaka gulu la asilikali ndi olamulira wawo ndi akuluakulu a Ayuda anamugwira Yesu. Iwo anamumanga.
13 Then they took him first to Annas, [who was previously the high priest]. He was the father-in-law of Caiaphas. Caiaphas was the high priest that year.
Poyamba anapita naye kwa Anasi amene anali mkamwini wa Kayafa, mkulu wa ansembe chaka chimenecho.
14 Caiaphas was the one who [previously] advised the Jewish [Council] that it would be better if one man died for the sake of the people [than for all the people of the Jewish nation to die].
Kayafa anali amene analangiza Ayuda kuti kukanakhala kwabwino ngati munthu mmodzi akanafera anthu.
15 Simon Peter and [I] were following Jesus. Because the high priest knew [me], [his doorkeeper permitted me] to enter the courtyard.
Simoni Petro ndi ophunzira wina ankamutsatira Yesu chifukwa ophunzira uyu amadziwika kwa mkulu wa ansembe. Iye analowa ndi Yesu mʼbwalo la mkulu wa ansembe
16 But Peter [had to] wait outside near the doorway. However, since I knew the high priest, I went back to the doorway and spoke to the girl who was guarding the entrance. Then [she allowed] Peter to come in.
koma Petro anadikira kunja pa khomo. Ophunzira winayo amene amadziwika kwa mkulu wa ansembe, anatuluka ndi kuyankhula ndi mtsikana amene anali mlonda wa pa khomo ndi kumulowetsa Petro.
17 The servant girl who was guarding the doorway said to Peter, “Surely you are not another disciple of that man [they have arrested], are you?” He said, “I am not.”
Mtsikanayo anafunsa Petro kuti, “Kodi iwe sindiwe mmodzi wa ophunzira a Munthu uyu?” Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”
18 It was cold, so the high priest’s slaves and Temple guards made a charcoal fire and were standing around it to keep warm. Peter was also standing near it, warming himself.
Popeza kunkazizira, anyamata antchito ndi akuluakulu ena anasonkha moto wamakala namawotha atayimirira mozungulira. Petro nayenso anayimirira pamodzi ndi iwo namawotha nawo motowo.
19 [While Peter was doing that], the high priest asked Jesus about his disciples and about what he was teaching people.
Pa nthawi imeneyi, mkulu wa ansembe anamufunsa Yesu za ophunzira ake ndi chiphunzitso chake.
20 Jesus replied, “I have always spoken where many people [MTY, HYP] could hear me. I have taught them in (the synagogues/their meeting places) and in the Temple courtyard, in places where many [HYP] Jews come together. I have spoken nothing secretly.
Yesu anayankha kuti, “Ine ndinayankhula poyera ku dziko lapansi. Nthawi zonse ndimaphunzitsa mʼsunagoge kapena mʼNyumba ya Mulungu kumene Ayuda onse amasonkhana pamodzi. Ine sindimanena kanthu mseri.
21 [So] (why are you asking me questions [like this illegally]?/you should not be asking me questions [like this illegally]!) [RHQ] Ask the people who heard what I taught! They certainly know what I said!”
Nʼchifukwa chiyani mukundifunsa Ine? Afunseni amene amamva. Zoonadi akudziwa zimene Ine ndinanena.”
22 After Jesus said that, one of the Temple guards standing near him slapped him on his face. He said, “(That is not the way you should answer the high priest!/Is that the way you should answer the high priest?) [RHQ]”
Yesu atanena izi, mmodzi wa akuluakulu amene anali pafupi anamumenya kumaso. Iye anafunsa kuti, “Mayankhidwe awa ndi woti ndi kuyankha mkulu wa ansembe?”
23 Jesus replied to him, “If I said something that was contrary [to your laws], you could tell [me that what I said that] was wrong. But because I said only what was right, (you should not be striking me!/why are you striking me?) [RHQ]”
Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndanena kanthu kolakwika, chitirani umboni chimene ndalakwa. Koma ngati ndanena zoona, nʼchifukwa chiyani mwandimenya?”
24 Then after Jesus’ hands were tied {after they tied Jesus hands} [again], Annas sent him to Caiaphas, the high priest.
Kenaka Anasi anamutumiza Iye, ali womangidwabe, kwa Kayafa, mkulu wa ansembe.
25 As Simon Peter was standing warming himself [at the fire], someone else said to him, “You are not one of that man’s disciples, are you?” He denied [that he was], and said, “I am not.”
Pamene Simoni Petro anali chiyimirire kuwotha moto, anafunsidwa kuti, “Kodi iwe si mmodzi wa ophunzira ake?” Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”
26 [Later] one of the high priest’s servants, a man who was a relative of the man whose ear Peter had cut off [before], said to him, “I saw you with that man in the grove [of olive trees], did I not?”
Mmodzi wa antchito a mkulu wa ansembe, mʼbale wa munthu amene anadulidwa khutu ndi Petro anamutsutsa iye kuti, “Kodi sindinakuone iwe pamodzi ndi Iye mʼmunda muja?”
27 Peter again denied it. Immediately a rooster crowed, [as Jesus had said would happen].
Petro anakananso, ndipo pa nthawi yomweyo tambala analira.
28 Then the [Jewish leaders] [SYN] led Jesus from the [home of] Caiaphas to the headquarters [of Pilate, the Roman governor]. It was before dawn. [Pilate was a non-Jew], [and they thought that if they entered his headquarters], they would become unacceptable to God {God would reject them}, [and as a result] they would not be able to eat [the food during] the Passover [celebration]. [Because of that, they did not want to enter Pilate’s headquarters].
Kenaka Ayuda anamutenga Yesu kuchoka kwa Kayafa ndi kupita ku nyumba yaufumu ya bwanamkubwa wa Chiroma. Tsopano kunali mmamawa, ndipo polewa kudetsedwa monga mwa mwambo Ayuda sanalowe mʼnyumba yaufumuyo; iwo anafuna kuti adye Paska.
29 So Pilate came out to [talk to] them. He said, “What law do you say that this man has disobeyed?”
Choncho Pilato anatuluka napita kwa iwo ndipo anati, “Kodi ndi milandu yanji imene mukumuzenga munthu uyu?”
30 [They knew that Jesus had not disobeyed any Roman law, so they did not want to answer him. Instead], they said, “If this man were not a criminal, we would not have brought him to you!”
Iwo anayankha kuti, “Ngati Iye akanakhala kuti si wolakwa, ife sitikanamupereka kwa inu.”
31 Then Pilate said to them, “Take him yourselves, and judge him according to your own laws!” Then the Jewish [leaders] [SYN] said, “[No! We want him executed, but we want you Romans to execute him, because] we Jews have no right to execute anyone!”
Pilato anati, “Mutengeni inu eni ake ndi kumuweruza Iye monga mwa malamulo anu.” Ayuda anatsutsa nati, “Koma tilibe ulamuliro wakupha aliyense.”
32 [The Romans executed people by nailing them to a cross]. [So], as a result of what [the Jewish leaders said], it was fulfilled {[the Romans] would fulfill} what Jesus had said previously about the way he was going to die.
Izi zinachitika kuti mawu a Yesu amene anayankhula kusonyeza mtundu wa imfa imene Iye anati adzafe nayo akwaniritsidwe.
33 Pilate then went back inside his headquarters. He summoned Jesus. [Because the Jewish leaders had said that Jesus claimed to be a king], Pilate said to Jesus [scornfully], “Are you the king of the Jews?”
Kenaka Pilato anapita mʼkati mwa nyumba yaufumu nayitanitsa Yesu, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi iwe ndi mfumu ya Ayuda?”
34 Jesus replied, “Are you asking that because you yourself [want to know if I claim to be a king], or because (someone else/Caiaphas) said [that I claim to be their king]?”
Yesu anafunsa kuti, “Kodi amenewo ndi maganizo anu wokha? Kapena kuti ena anakuwuzani za Ine?”
35 Pilate replied, “I am not a Jew, [so] ([I cannot understand these matters!/how can I understand these matters]?) [RHQ] It was your fellow Jews and your chief priests who brought you to me! What have you done [to make them want to execute you]?”
Pilato anayankha kuti, “Kodi iwe ukuganiza kuti ine ndine Myuda? Ndi anthu ako ndi akulu a ansembe ako amene akupereka iwe kwa ine. Kodi walakwanji?”
36 Jesus replied, “It is not people in [MTY] this world who are [making me] king. If it was people in this world who were making me a king, my disciples would have fought in order that the Jewish [leaders] [SYN] would be prevented {to prevent the Jewish [leaders] [SYN]} from seizing me. But it is not [someone here in] this world who is making me a king.”
Yesu anati, “Ufumu wanga si wa dziko lapansi lino. Ukanakhala wa pansi pano, antchito anga akanachita nkhondo kulepheretsa Ayuda kundigwira. Koma tsopano ufumu wanga ndi wochokera kumalo ena.”
37 Then Pilate said to him, “So [are you saying that] you are a king?” Jesus replied, “[Yes], what you have said about my being a king [is correct]. I was born to become a king, and I came into this world to tell people the truth [about God]. Everyone who [believes] the truth pays attention to what I say.”
Pilato anati, “Kani ndiwe mfumu!” Yesu anayankha kuti, “Inu mwalondola ponena kuti, Ine ndine mfumu. Kunena zoona, Ine ndinabadwa chifukwa cha chimenechi, ndipo nʼchifukwa chake ndinabwera mʼdziko lapansi, kudzachitira umboni choonadi. Aliyense amene ali mbali yachoonadi amamvera mawu anga.”
38 Pilate said to him, “[How can anyone know] what the truth is?” After he said that, he went outside and talked to the Jewish [leaders] [SYN] again. He said to them, “I do not find that he has done anything at all for which I should punish him.
Pilato anafunsa kuti, “Kodi choonadi nʼchiyani?” Ndi mawu awa iye anapitanso kwa Ayuda ndipo anati, “Ine sindikupeza mlandu mwa Iye.
39 But you [Jews] customarily, [every year] during the Passover [celebration], ask me to release for you [someone who is in prison]. So would you like for me to release for you the [man who you] Jews [say is your] king?”
Koma ndi mwambo wanu kuti pa nthawi ya Paska, ine ndikumasulireni wamʼndende mmodzi. Kodi mufuna ndikumasulireni ‘Mfumu ya Ayuda?’”
40 They shouted again, “No, do not [release] this man! Instead, [release] Barrabas!” But Barrabas was [in prison because he was] a revolutionist!
Iwo anafuwula nati, “Ameneyu ayi! Mutipatse ife Baraba!” Barabayo anali wachifwamba.