< John 17 >

1 After Jesus said those things, he looked [up] toward heaven. Then he prayed, “[My] Father, it is now the time [MTY] [for me to suffer and die]. Honor me [as I do that], in order that I may honor you.
Yesu atatha kunena izi, anayangʼana kumwamba ndipo anapemphera: “Atate, nthawi yafika. Lemekezani Mwana wanu, kuti Mwana wanuyo akulemekezeni Inu.
2 You gave me authority over all people, in order that I might enable all those whom you chose [to come] to me to live eternally. (aiōnios g166)
Pakuti Inu munamupatsa Iye ulamuliro pa anthu onse kuti apereke moyo wosatha kwa onse amene mwamupatsa. (aiōnios g166)
3 [The way for people] to live eternally is for them to know that you are the only true God, and to know that [I], Jesus, am the Messiah, the one you have sent. (aiōnios g166)
Tsono moyo wosathawo ndi uwu: Iwo akudziweni Inu, Mulungu yekhayo woona, ndi Yesu Khristu, amene Inu mwamutuma. (aiōnios g166)
4 I have honored you here on this earth by completing all the work that you gave me to do.
Ine ndabweretsa ulemerero wanu pa dziko pamene ndamaliza ntchito imene munandipatsa kuti ndi igwire.
5 [My] Father, now honor me when I am with you [again], by causing me to have the greatness I had when I was with you before the world began.”
Ndipo tsopano, Atate, ndilemekezeni Ine pamaso panu ndi ulemerero uja umene ndinali nawo kwa Inu dziko lapansi lisanayambe.
6 “I have revealed [what] you [are like] to the people whom you brought to me from among those who do not belong to you [MTY]. Those [who came to me] belonged to you, and you brought them to me. Now they have obeyed your message.
“Ine ndawadziwitsa za Inu anthu amene munandipatsa mʼdziko lapansi. Iwo anali anu. Inu munawapereka kwa Ine ndipo amvera mawu anu.
7 Now they know that everything you have given me, [your message and your work], comes from you.
Tsopano akudziwa kuti zonse zimene munandipatsa nʼzochokera kwa Inu.
8 I gave them the message that you gave me, and they have accepted it. They now know for certain that I came from you. They now believe that you sent me.
Pakuti Ine ndiwapatsa mawu amene Inu munandipatsa ndipo awalandira. Iwo akudziwa ndithu kuti Ine ndinachokera kwa Inu, ndipo akukhulupirira kuti Inu ndiye amene munandituma Ine.
9 I am praying for them. I am not praying for those [who do not belong to you] [MTY]. Instead, [I am praying] for those whom you have brought to me, because they belong to you.
Ine ndikuwapempherera. Ine sindikupempherera dziko lapansi, koma anthu amene Inu mwandipatsa, pakuti ndi anu.
10 All [the disciples] that I have belong to you, and all those who belong to you also belong to me. They have shown how great I am.
Zonse zimene Ine ndili nazo ndi zanu, ndipo zonse zimene Inu muli nazo ndi zanga. Choncho Ine ndalemekezedwa mwa iwowo.
11 I will not be [staying] in the world any longer. I will be coming back to you. They, however, will be [here] in the world [among those who are opposed to you]. [My] Holy Father, protect them from spiritual harm by your power [MTY], the power that you gave me, in order that they may be united as we are united.
Ine sindikukhalanso mʼdziko lapansi nthawi yayitali, koma iwo akanali mʼdziko lapansi. Ine ndikubwera kwa Inu. Atate Woyera, atetezeni ndi mphamvu za dzina lanu. Dzina limene munandipatsa Ine, kuti iwo akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
12 While I have been with them, I have [completely] protected them by the power [MTY] that you gave me. As a result, only one of them will be eternally separated from you. He is the one who was doomed to be eternally separated from you. [That has happened] to fulfill [what a prophet wrote] in the Scriptures [would happen].
Pamene ndinali nawo, ndinawateteza ndi kuwasunga mosamala mʼdzina limene munandipatsa. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatayika kupatula yekhayo amene anayenera kuwonongeka kuti malemba akwaniritsidwe.
13 [Father], now I am about to return to you. I have said these things while I am still [here] in the world in order that my [disciples] may fully experience being joyful, as I have been joyful.
“Tsopano ndikubwera kwa Inu. Ndikunena izi ndikanali mʼdziko lapansi, kuti iwo akhale ndi muyeso wodzaza wachimwemwe changa mʼkati mwawo.
14 I have given them your message. As a result, those who are opposed to you [MTY] have hated them, because [my disciples] do not belong to those who oppose you [MTY], just like I do not belong to those who oppose you [MTY].
Ine ndawapatsa mawu anu ndipo dziko lapansi likudana nawo, pakuti sali a dziko lapansi monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
15 I am asking you, not that you take them out of this world, but instead that you protect them from [Satan], the evil one.
Sindikupempha kuti muwachotse mʼdziko lapansi koma kuti muwateteze kwa woyipayo.
16 They do not belong to those who are opposed to you [MTY], just like I also do not belong to them.
Iwo si a dziko lapansi, monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
17 Set [my disciples] apart so that they may (completely belong to/serve) you, by [enabling them to live in accordance with] what is true. Your message is true.
Ayeretseni ndi choonadi chanu. Mawu anu ndiye choonadi.
18 Just like you sent me here into this world, now I surely will be sending them [to other places] in [MTY] the world.
Monga Inu munandituma Ine mʼdziko lapansi, Inenso ndikuwatuma mʼdziko lapansi.
19 I dedicate myself to completely belong to you, in order that they also may truly be dedicated {dedicate themselves} completely to you.”
Chifukwa cha iwowa Ine ndikudziyeretsa, kuti iwo ayeretsedwenso kwenikweni.
20 “I am praying not only for these [eleven disciples]. I am praying also for those who [will] believe in me as a result of [hearing] their message.
“Ine sindikupempherera iwo okhawa, komanso amene adzandikhulupirira chifukwa cha uthenga wawo.
21 [My] Father, [I want] all of them to be united, just like I am united with you because of my relationship with you, and as you are united with me because of your relationship with me. I also want them to be united with us. [I want that to happen] so that those who do not know you [MTY] may know that you sent me.
Ndikuwapempherera kuti onsewa akhale amodzi. Monga Inu Atate muli mwa Ine ndi Ine mwa Inu, iwonso akhale mwa Ife kuti dziko lapansi likhulupirire kuti Inu munandituma Ine.
22 I have honored my disciples just like you honored me, in order that they may be united, as we are united.
Ine ndawapatsa ulemerero umene munandipatsa Ine, kuti akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
23 I want them to be united just like they are united with me and as you are united with me. May they be completely united, in order that those who do not belong to you [MTY] may know that you sent me and that you have loved them just like you have loved me.
Ine ndikhale mwa iwo ndipo Inu mwa Ine kuti umodzi wawo ukhale wangwiro. Choncho dziko lapansi lidzadziwa kuti Inu munandituma Ine ndipo Inu mwawakonda iwowa monga momwe Inu munandikondera Ine.
24 [My] Father, I want [the disciples] you have brought to me to [some day] be with me [in heaven], where I will be. I want them to see my greatness. I want them to see the greatness you gave me because you loved me. You gave me that greatness before you created the world.
“Atate, Ine ndikufuna kuti anthu amene mwandipatsa Ine adzakhale ndi Ine kumene kuli Ine, ndi kuona ulemerero wanga, ulemerero umene munandipatsa chifukwa Inu munandikonda dziko lapansi lisanalengedwe.
25 [My] righteous Father, although the people who do not belong to you [MTY] do not know what you [are like], I know what you [are like], and my disciples know that you sent me.
“Atate wolungama, ngakhale kuti dziko lapansi silikudziwani Inu, Ine ndimakudziwani, ndipo iwo amadziwa kuti Inu munandituma Ine.
26 I have revealed to them [what] you [are like], and I will continue to reveal to them [what] you [are like]. I will do that in order that they may love [others] just like you love me, and in order that I may be in them [by my Spirit].”
Ine ndawadziwitsa dzina lanu, ndipo ndidzapitiriza kuwadziwitsa dzina lanulo, kuti chikondi chomwe munandikonda nacho chikhale mwa iwo, ndipo Ine mwa iwo.”

< John 17 >