< Job 42 >
1 Then Job replied to Yahweh. [He said],
Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
2 “I know that you can do everything and that no one can stop you from doing what you want to do.
“Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
3 [You asked me], ‘(Who are you, who by speaking ignorantly, question what I plan to do?/You have no right to question what I plan to do by speaking ignorantly.)’ [RHQ] It is true that I spoke about things that I did not understand, things that are very wonderful/marvelous, and therefore I am not able to know them.
Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
4 You said to me, ‘Listen while I talk to you. I want to ask you some questions, so prepare yourself to answer them.’
“Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
5 I had heard about you previously, but now [it is as though] I have seen you with my own eyes.
Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
6 Therefore I (am ashamed of/withdraw) what I said, and I sit in dust and ashes to show that I am sorry [for what I said].”
Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
7 After Yahweh said these things to Job, he said to Eliphaz, “I am angry with you and your two friends, [Bildad and Zophar], because what my servant Job said about me was right/true, but what you have spoken about me was not right/true.
Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
8 So now you must take to Job seven young bulls and seven rams and [kill them and] burn them on the altar as a sacrifice for yourselves. Then Job will pray for you, and I will do what he requests me to do, [and I will forgive you for speaking wrongly about me]. I will not punish you, even though you deserve to be punished, because what you said about me was not right/true, but what Job said about me was right/true.”
Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
9 So Eliphaz, Bildad, and Zophar did what Yahweh commanded them to do, and Yahweh did what Job requested him to do [for the three of them].
Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
10 After Job prayed for his three friends, Yahweh [healed him and] caused him to become rich again. Yahweh gave him twice as many things as he had before.
Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
11 Then all his brothers and sisters, and all the people who had known him before, came to his house, and they ate a meal together. They consoled/comforted [DOU] him because of all the troubles that Yahweh had allowed him to experience.
Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
12 Then Yahweh blessed Job in the second half of his life more than he had blessed him in the first half of his life. He now acquired/owned 14,000 sheep, 6,000 camels, 2,000 oxen, and 1,000 female donkeys.
Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
13 And he also had seven [more] sons and three [more] daughters.
Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
14 He named the first daughter Jemimah, he named the second daughter Keziah, and he named the third daughter Keren-Happuch.
Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
15 In all of [Uz] land there were no young women who were as beautiful as the daughters of Job, and Job declared that they would inherit some of his possessions, just like their brothers would inherit some.
Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
16 After that, Job lived 140 more years. Before he died, he (saw/enjoyed being with) his great-great-grandchildren.
Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
17 He was very old [DOU] when he died.
Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.