< Job 37 >

1 “My heart pounds [DOU] when [I think about] that.
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 Listen, all of you, to the thunder, which is like God’s voice [DOU].
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 He causes thunder to be heard all across the sky, and he causes lighting to flash to the most distant places on the earth.
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 After [the lightning flashes], we hear the thunder which is like [MET] God’s majestic voice; he does not restrain the lightning when he speaks.
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
5 When God speaks, it is awesome, like thunder; he does amazing things which we cannot [fully] understand.
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 He commands the snow to fall on the ground, and [sometimes] he causes it to rain very hard.
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 And [when God does that, ] it prevents people [SYN] from working, in order that all people may know that he is the one who has done that (OR, what he can do).
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 [When it rains, ] animals go into their hiding places, and they remain there [until the rain stops].
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 The storms/hurricanes come from the place [in the south where they start], and the cold wind comes from the north.
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 [In the (winter/cold season), the cold north wind is like] God’s breath [that] causes [MET] water to freeze; he causes the lakes/streams to become ice.
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 God fills the clouds with moisture/hail, and lightning flashes from the clouds.
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 He guides the clouds and causes them to move back and forth in order that they may accomplish all that he commands them to do, all over the world.
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 Sometimes God sends rain to punish us, and sometimes he sends rain to show us that he acts kindly toward us.
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 “Job, listen to this; stop and think about the wonderful things that God does.
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 (Do you know how God commands the lightning to flash down from the clouds?/We do not know how God commands the lightning to flash down from the clouds.) [RHQ]
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Only God knows everything perfectly; so (do you know how he causes the clouds to (move/float) (amazingly/wonderfully) across the sky?/you certainly do not know how he causes the clouds to (move/float) (amazingly/wonderfully) across the sky!) [RHQ]
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 No, you just sweat there in your clothes; [it is very oppressive] when the [hot] wind stops blowing from the south and [all the leaves on the trees] (become still/do not move).
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 (Can you stretch out the skies like God does and make them as hard as [SIM] a sheet of polished brass?/You certainly cannot stretch out the skies like God does and make them as hard as [SIM] a sheet of polished brass!) [RHQ]
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 “Job, tell us(exc) what we should say to God; we do not know anything [IDM]. As a result, we do not know what to say to him to defend ourselves.
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Should I tell God that I want to speak to him? No, because [if I did that, ] he might destroy me.
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 Now, people cannot look [directly] at the sun when it shines brightly in the sky after the wind has blown the clouds away; [so, we certainly cannot look at the brightness of God].
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 God comes out of the north with a light [that shines like] gold; his glory causes us to be afraid.
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 Almighty God is very powerful, and we cannot come near to him. He always acts righteously, and he will never oppress us.
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 That is the reason that we have an awesome respect for him; he does not pay attention to those who proudly, [but wrongly], think that they are wise.”
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

< Job 37 >