< Job 26 >

1 Job replied [to Bildad], saying this [sarcastically]:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “I am a very weak and helpless man; and (you [certainly] have not helped me [SAR] very much!/[do you think that] you have helped me [SAR] very much?) [RHQ]
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 (You certainly have counseled me well—I, who am not wise at all./[Do you think that] you have counseled me well—I, who am not wise at all?) [RHQ] ([I’m sure you think that] you have given a lot of very good advice to me. [RHQ]
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 Who helped you to say all those [great/wise] things? Who inspired you to speak like you did?”
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 “[Because] the spirits of dead people [are afraid], [they] tremble in the waters that are deep under the earth.
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 God knows all about [those who are in] the place of the dead; there is nothing down there that prevents God from seeing what is there. (Sheol h7585)
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
7 God stretched out the earth over the huge empty space and caused the earth to have nothing [to support it].
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 He fills the thick/dense clouds with water and prevents that water from bursting the clouds.
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 He causes clouds to (obscure/prevent us from seeing) the moon.
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 He separated the light from the darkness and put the horizon to mark the place where the night ends and the daytime begins.
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 When [he is angry, it is as though] he rebukes the pillars that hold up the sky. They are (shocked/very fearful), and they tremble.
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 With his power he calmed the sea; with his skill/wisdom he destroyed Rahab, the huge sea monster.
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 With his breath he caused the sky to be bright/clear; with his hand he killed the great dragon in the sea.
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 But those events show only a small amount of his power; [it is as though] we are hearing only whispers of his powerful voice. When we hear thunder, [we say, ] ‘(Who can really understand [how great] his power [is]/No one can [really] understand [how great] his power [is]!) [RHQ]’”
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

< Job 26 >