< Job 2 >

1 On another day, the angels came again and gathered together in front of Yahweh, and Satan came too.
Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
2 Yahweh asked Satan, “Where have you come from?” Satan replied, “I have come from the earth, where I have been traveling back and forth, seeing what is happening.”
Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
3 Yahweh asked Satan, “Have you (noticed/thought about) my [faithful] servant Job? He is very godly/righteous [DOU], he greatly respects/reveres me, and he [always] avoids doing evil things. And he still acts in a very godly/righteous manner, even though you persuaded me to [let you] cause disastrous things to happen to him for no reason.”
Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
4 Satan replied to Yahweh, “He praises you only because you bless him [IDM]. People will give up everything they have to save their own lives.
Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
5 But if you harm his body [MTY], he will surely curse you openly [IDM]!”
Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
6 Yahweh replied to Satan, “(All right/Okay), you may do to him whatever you want to do, but do not cause him to die.”
Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
7 So Satan left, and he caused Job to be afflicted with very painful boils, from the top of his head to the soles of his feet.
Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
8 Job took a piece of broken pottery and scraped the boils on his skin, and he sat in ashes [as people did when they were mourning for those who had died].
Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
9 His wife said to him, “Are you still trying to (be loyal to/faithfully trust in) God? You should curse God, and then you will die.”
Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
10 But Job replied, “You talk like people who do not know God talk. (Should we accept only the good things that God [does for us]?/We should not accept only the good things that God [does for us].) [RHQ] We should also accept bad things.” So in spite of all these [things that happened to] Job, [he] did not say anything against God.
Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
11 Among Job’s friends were Eliphaz from Teman [town], Bildad from Shuah [land] and Zophar from Naamah [land]. When they heard about all the terrible things that had happened to Job, they left their home areas and went together to Job to console/comfort him [DOU].
Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
12 When they saw Job from a distance, they almost did not recognize him. They wailed loudly, they tore their robes, and they threw dust over their heads [to show how sorry they were because of what had happened to Job].
Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
13 Then they sat on the ground with Job for seven days. None of them said anything to Job, because they saw that he was suffering greatly, [and they did not think that anything that they said would lessen his pain].
Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.

< Job 2 >