< Job 12 >
1 Then Job said [to his three friends],
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “You (talk as though/You think) [SAR] that you are the people [whom everyone should listen to], and that when you die, there will be no more wise people.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 But I have as much good sense as you do; I am (not less wise than/certainly as wise as [LIT]) you. Certainly everyone knows [RHQ] all that you have said.
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 My friends all laugh at me now. Previously I habitually requested God to help me, and he answered/helped me. I am righteous, a very godly man [DOU], but everyone laughs at me.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Those [like you] who have no troubles make fun of me; they cause those [like me] who are already suffering to have more troubles.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Bandits live peacefully, and no one threatens those who cause God to become angry; their own strength is the god [that they worship].
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 “But ask the wild animals [what they know about God], and [if they could speak] they would teach you. [If you could] ask the birds, they would tell you.
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 [If you could] ask the creatures [that crawl] on the ground, or the fish in the sea, they would tell you [about God].
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 All of them certainly know [RHQ] that it is Yahweh who has made them with his hands.
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 He directs the lives of all living creatures; he gives breath to all [us] humans [to enable us to remain alive].
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 And when we [SYN] hear what other people [like you] say, we [RHQ] think carefully about what they say [to determine what is good and what is bad], like we [SYN] taste food [to determine what is good and what is bad].
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Old people are [often] very wise, and because of having lived many years, they understand much,
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 but God is wise and very powerful; he has good sense and understands [everything].
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 If he tears [something] down, no one can rebuild it; if he puts someone in prison, no one can open [the prison doors to allow that person to escape].
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 When he prevents rain from falling, everything dries up. When he causes a lot of rain to fall, [the result is that] there are floods.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 He is the one who is truly strong and wise; he rules over those who deceive others and those whom they deceive.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 He [sometimes] causes [the king’s] officials to no longer be wise, and he causes judges to become foolish.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 He takes from kings the robes that they wear and puts loincloths around their waists, [causing them to become slaves].
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 He takes from priests the sacred clothes that they wear, [with the result that they no longer can do their work], and takes power from those who rule others.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 He [sometimes] causes those whom others trust to be unable to speak, and he causes old men to no longer have good sense.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 He causes those who have authority to be despised, and he causes those who are powerful to no longer have any power/strength.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 He causes things that are hidden in the darkness to be revealed.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 He causes some nations to become very great, and [later] he destroys them; he causes the territory of some nations to become much larger, and [later] he causes them to be defeated and their people to be scattered.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 He causes [some] rulers to become foolish/stupid, and then he causes them to wander around, lost, in an barren desert.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 They grope around in the darkness, without any light, and he causes them to stagger like [SIM] people who are drunk.”
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.